< Mika 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
The word of the Lord that came to Micah the Moreshethite, in the days of Jotham, Ahaz, and Hezekiah, kings of Judah, which he saw about Samaria and Jerusalem.
2 Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
All peoples, listen. And may the earth and its fullness pay attention. And may the Lord God be a witness to you, the Lord from his holy temple.
3 Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
For behold, the Lord will go forth from his place. And he will descend, and he will trample over the high places of the earth.
4 Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
And the mountains will be consumed under him, and the valleys will be torn apart, like wax before the face of fire, and like waters that rush swiftly downward.
5 Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
All this is for the wickedness of Jacob and for the sins of the house of Israel. What is the wickedness of Jacob? Is it not Samaria? And what is the loftiness of Judah? Is it not Jerusalem?
6 “Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
And I will place Samaria like a pile of stones in the field, when a vineyard is planted. And I will pull down its stones into the valley, and I will reveal her foundations.
7 Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
And all her graven images will be cut to pieces, and all her rewards will be burned with fire, and I will place all her idols in perdition. For they have been gathered together from the pay of a kept woman, and even to the pay of a kept woman, they will return.
8 Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
I will lament and wail about this. I will go out despoiled and naked. I will make a howl like the dragons, and a mourning like the ostriches.
9 Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
For her wound has been in despair. For it has come even to Judah. It has touched the gate of my people, even to Jerusalem.
10 Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
Do not be willing to announce it in Gath; may you not lament with tears. In the house of Dust, besprinkle yourselves with dust.
11 Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
And cross over to your dwelling place, Beauty, bewildered by disgrace. She did not depart, who dwells at the place of departure. The House nearby, which remained firm by herself, will receive mourning from you.
12 Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
For she has been weakened in goodness, who dwells in bitterness. For disaster has descended from the Lord to the gate of Jerusalem.
13 Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
A tumult of four-horse chariots has stupefied the inhabitants of Lachish. The beginning has been sin for the daughter of Zion, because in you have been found the evil deeds of Israel.
14 Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
Because of this, she will send emissaries to the inheritance of Gath: the house of Lying in order to deceive the kings of Israel.
15 Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
Nevertheless, I will lead an heir to you, who dwell in Mareshah: the glory of Israel will reach all the way to Adullam.
16 Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.
Become bald and shaved for your delicate sons. Increase your baldness like the eagle. For they have been carried into captivity from you.

< Mika 1 >