< Mika 1 >
1 Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
Riječ Jahvina, upućena Miheju Morešećaninu u vrijeme Jotama, Ahaza i Ezekije, kraljeva judejskih. Njegova viđenja o Samariji i o Jeruzalemu.
2 Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
Čujte, narodi, vi svi! Slušaj, zemljo, i sve što te ispunja! Gospod Jahve protiv vas će svjedočiti - Gospod iz svetoga Hrama svojega!
3 Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
Jer evo: Jahve izlazi iz svetoga mjesta svojega, silazi i hodi po visovima zemaljskim.
4 Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
Gore se rastapaju pod njegovim koracima i doline rasijedaju kao vosak pred ognjem, kao voda što se razlijeva niz obronak.
5 Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
Sve je to za zločinstvo Jakovljevo i za grijehe doma Izraelova. Koje je zločinstvo Jakovljevo? Nije li Samarija? Što su uzvišice Judine? Nije li Jeruzalem?
6 “Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
“Učinit ću od Samarije kamenu gomilu u polju, ledinu za vinograd. Zavaljat ću kamenje njezino u dolinu, otkrit ću joj temelje.
7 Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
Razbit će se svi njeni kipovi, sva će joj se plaća bludnička ognjem spaliti, raskomadat ću sve njene idole, jer su od bludničke plaće nakupljeni, i opet će postati plaćom bludničkom.”
8 Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
“Zato ću zakukati i zaridati, ići ću gol i bos, zavijat ću kao šakali, urlikat ću kao nojevi.
9 Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
Jer njenoj rani nema lijeka, sve do Jude dopire, dotiče Vrata moga naroda, sve do Jeruzalema!
10 Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
Ne objavljujte toga u Gatu, u Akonu nemojte plakati! U Bet Leafri valjajte se u prašini!
11 Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
Odlazi sramotno, stanovnice šafirska! Iz svoga grada nije izašla stanovnica saananska! Bet Haesel iščupan je iz temelja, iz svojih čvrstih osnova.
12 Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
Kako se može nadati sreći stanovnica marotska? Jer nesreća silazi od Jahve sve do vrata jeruzalemskih.
13 Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
Upregni brze konje u bojna kola, stanovnice lakiška! To je bio početak grijeha Kćeri sionske, jer su se u tebi našla zločinstva Izraelova.
14 Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
Zato ćeš dati otpusnicu Morešet Gatu, domovi će akzipski razočarati kraljeve izraelske.
15 Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
Još ću ti dovesti osvajača, stanovnice mareška, stići će do Adulama slava Izraelova.
16 Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.
Čupaj kosu i ostriži se za milom djecom svojom! Postani ćelava kao orao lešinar, jer su izgnana daleko od tebe.”