< Mika 7 >

1 Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
Вай де мине! Кэч паркэ сунт ла стрынӂеря поамелор ши ла стрынӂеря бобицелор дупэ кулесул стругурилор: ну май есте ничун стругуре де мынкаре, нич чя динтый смокинэ, доритэ де суфлетул меу!
2 Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
С-а дус омул де бине дин царэ ши ну май есте ничун ом чинстит принтре оамень; тоць стау ла пындэ ка сэ версе сынӂе, фиекаре ынтинде о курсэ фрателуй сэу.
3 Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
Мыниле лор сунт ындрептате сэ факэ рэу: кырмуиторул чере дарурь, жудекэторул чере платэ, чел маре ышь аратэ пе фацэ че дореште ку лэкомие, ши астфел мерг мынэ-н мынэ.
4 Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
Чел май бун динтре ей есте ка ун мэрэчине, чел май чинстит есте май рэу декыт ун туфиш де спинь. Зиуа веститэ де тоць пророчий Тэй, педяпса Та, се апропие! Атунч ва фи улуяла лор.
5 Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
Ну креде пе ун приетен, ну те ынкреде ын руда чя май де апроапе; пэзеште-ць уша гурий де чя каре ыць стэ ын браце!
6 Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
Кэч фиул батжокореште пе татэл, фата се скоалэ ымпотрива мамей ей, нора ымпотрива соакрей сале; врэжмаший омулуй сунт чей дин каса луй!
7 Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
Еу ынсэ вой приви спре Домнул, ымь вой пуне нэдеждя ын Думнезеул мынтуирий меле, Думнезеул меу мэ ва аскулта.
8 Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
Ну те букура де мине, врэжмашэ, кэч, кяр дакэ ам кэзут, мэ вой скула ярэшь; кяр дакэ стау ын ынтунерик, тотушь Домнул есте Лумина мя!
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
Вой суфери мыния Домнулуй – кэч ам пэкэтуит ымпотрива Луй – пынэ че Ел ымь ва апэра причина ши-мь ва фаче дрептате; Ел мэ ва скоате ла луминэ ши вой приви дрептатя Луй.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
Кынд ва ведя врэжмаша мя лукрул ачеста, ва фи акоперитэ де рушине, еа, каре-мь зичя: „Унде есте Домнул Думнезеул тэу?” Окий мей ышь вор ведя доринца ымплинитэ фацэ де еа. Атунч, еа ва фи кэлкатэ ын пичоаре ка нороюл де пе улицэ.
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
Ын зиуа кынд ыць вор зиди ярэшь зидуриле, ын зиуа ачея ци се вор лэрӂи хотареле.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
Ын зиуа ачея, вор вени ла тине, дин Асирия пынэ ын Еӂипт, дин Еӂипт пынэ ла рыу, де ла о маре ла алта ши де ла ун мунте ла алтул.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
Дар, май ынтый, цара ва фи пустиитэ дин причина локуиторилор ей, ын урма фаптелор лор реле.
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
Паште-Ць попорул ку тоягул Тэу, паште турма моштенирий Тале, каре локуеште сингурэ ын пэдуря дин мижлокул Кармелулуй; ка сэ паскэ пе Басан ши ын Галаад, ка ын зилеле де алтэдатэ.
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
„Ыць вой арэта лукрурь минунате”, зиче Домнул, „ка ын зиуа кынд ай ешит дин цара Еӂиптулуй.”
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
Нямуриле вор ведя лукрул ачеста ши се вор рушина ку тоатэ путеря лор; вор пуне мына ла гурэ ши ышь вор аступа урекиле.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
Вор линӂе пулберя ка шарпеле; вор еши тремурынд ка тырытоареле пэмынтулуй, афарэ дин четэцуиле лор, вор вени плине де фрикэ ынаинтя Домнулуй Думнезеулуй ностру ши се вор теме де Тине.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
Каре Думнезеу есте ка Тине, каре ерць нелеӂюиря ши тречь ку ведеря пэкателе рэмэшицей моштенирий Тале? Ел ну-Шь цине мыния пе вечие, чи Ый плаче ындураря!
19 Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
Ел ва авя ярэшь милэ де ной, ва кэлка ын пичоаре нелеӂюириле ноастре ши ва арунка ын фундул мэрий тоате пэкателе лор.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.
Вей да ку крединчошие луй Иаков ши вей цине ку ындураре фацэ де Авраам че ай журат пэринцилор ноштри ын зилеле де одиниоарэ.

< Mika 7 >