< Mika 7 >
1 Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
Biada mi! Jestem bowiem jak ostatki po letnich zbiorach, jak pokłosie grona po winobraniu. Nie ma żadnego grona do zjedzenia, moja dusza pragnęła pierwocin z owocu.
2 Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
Pobożny zginął z ziemi, nie ma prawego wśród ludzi. Wszyscy czyhają na krew, każdy zastawia sieci dla swego brata.
3 Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
By chętnie czynić zło obiema rękami, książę i sędzia żądają datku; zamożny [człowiek] wypowiada swoją przewrotną żądzę. I razem wszystko splatają.
4 Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
Najlepszy z nich jest jak oset; najuczciwszy – jak płot ciernisty. Nadchodzi dzień twoich stróżów [i] twojego nawiedzenia; już nastanie ich zamieszanie.
5 Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
Nie wierzcie przyjacielowi, nie ufajcie wodzowi. Strzeż bramy swoich ust przed tą, która leży na twoim łonie.
6 Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
Syn bowiem lekceważy ojca, córka powstaje przeciwko swojej matce, synowa przeciwko swojej teściowej, [a] wrogami człowieka [są] jego domownicy.
7 Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
Dlatego będę wypatrywał PANA, będę oczekiwać Boga mego zbawienia. Mój Bóg mnie wysłucha.
8 Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
Nie ciesz się z mojego powodu, moja nieprzyjaciółko! Chociaż upadłem, powstanę; choć siedzę w ciemności, PAN jest moją światłością.
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
Zniosę gniew PANA, bo zgrzeszyłem przeciwko niemu, aż będzie bronił mojej sprawy i wykona dla mnie sąd. Wyprowadzi mnie na światło i ujrzę jego sprawiedliwość.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
Ujrzy to moja nieprzyjaciółka i wstyd okryje tę, która do mnie mówi: Gdzie jest PAN, twój Bóg? Moje oczy będą patrzyć na nią, gdy będzie podeptana jak błoto na ulicach.
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
W [tym] dniu, kiedy będą odbudowywać twoje mury, w tym dniu dekret rozejdzie się daleko.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
W tym dniu będą przychodzić do ciebie od Asyrii aż po miasta obronne, od miast obronnych aż po rzekę, od morza aż do morza i od góry aż do góry.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
Ta ziemia jednak będzie spustoszona z powodu swoich mieszkańców, z powodu owocu ich czynów.
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
Paś swój lud laską swoją, trzodę swojego dziedzictwa, która mieszka samotnie w lesie i w środku Karmelu. Niech się pasą w Baszanie i Gileadzie [jak] za dawnych dni.
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
Ukażę mu cudowne rzeczy jak za dni, gdy wyszedłeś z ziemi Egiptu.
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
Ujrzą to narody i zawstydzą się całej swojej potęgi. Przyłożą rękę do ust, a ich uszy ogłuchną.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
Będą lizać proch jak wąż, wyjdą ze swoich nor jak zwierzęta pełzające do PANA, naszego Boga, ze strachem i będą się bać ciebie.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
Któż jest Bogiem jak ty, który przebacza nieprawość i daruje występek resztki swego dziedzictwa? Nie chowa swego gniewu na wieki, bo ma upodobanie w miłosierdziu.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
Odwróci się i zlituje się nad nami; pokona nasze nieprawości i wrzuci w głębiny morza wszystkie nasze grzechy.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.
Pokażesz prawdę Jakubowi i [okażesz] miłosierdzie Abrahamowi, tak jak przysiągłeś naszym ojcom za dawnych dni.