< Mika 7 >

1 Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
Maye kimi! Ngoba nginjengokuvunwa kwezithelo zasehlobo, njengokukhothozwa kwesivini; kakulahlukuzo lokudliwa; umphefumulo wami uloyisa isithelo sokuqala esivuthiweyo.
2 Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
Olungileyo ubhubhile esuka emhlabeni; njalo kakho oqotho phakathi kwabantu; bonke bacathamele igazi, bayazingela ngulowo lalowo umfowabo ngembule.
3 Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
Ukuze benze okubi ngezandla zombili ngokutshiseka, isiphathamandla siyacela, lomahluleli uyacela umvuzo; lomkhulu ukhuluma inkanuko yomphefumulo wakhe, bayakwelukanisa.
4 Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
Ongcono wabo unjengameva; oqotho kubo mubi kulothango; usuku lwabalindi bakho, ukuhanjelwa kwakho sekufikile; khathesi kuzakuba khona ukudideka kwabo.
5 Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
Lingabeki ithemba kumngane, lingakholwa umhlobo; gcina iminyango yomlomo wakho kuye umfazi olala esifubeni sakho.
6 Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
Ngoba indodana idelela uyise, indodakazi ivukela unina, umalokazana avukele uninazala; izitha zomuntu ngabantu bendlu yakhe.
7 Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
Ngakho mina ngizakhangela eNkosini, ngilindele uNkulunkulu wosindiso lwami; uNkulunkulu wami uzangizwa.
8 Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
Ungathokozi ngami, sithakazi sami; lapho ngisiwa, ngizavuka; lapho ngihlezi emnyameni, iNkosi izakuba yikukhanya kimi.
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
Ngizaluthwala ulaka lweNkosi, ngoba ngonile kuyo, ize imele udaba lwami, ingenzele isahlulelo. Izangikhuphela ekukhanyeni, ngibone ukulunga kwayo.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
Ngakho isithakazi sami sizabona, lehlazo limembese yena owathi kimi: Ingaphi iNkosi uNkulunkulu wakho? Amehlo ami azambona; khathesi uzanyathelelwa phansi njengodaka lwezitalada.
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
Ngosuku imiduli yakho ezakwakhiwa ngalo, ngalolosuku isimiso sizakuba khatshana.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
Ngalolosuku uzafika lakuwe evela eAsiriya, lemizini ebiyelweyo; njalo kusukela ezinqabeni kuze kube semfuleni, kusukela elwandle kusiya elwandle, kusukela entabeni kusiya entabeni.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
Lanxa kunjalo ilizwe lizakuba yincithakalo ngenxa yabahlali balo, ngenxa yesithelo sezenzo zabo.
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
Yelusa abantu bakho ngentonga yakho, umhlambi welifa lakho, ohlala wodwaehlathini, phakathi kweKharmeli. Kabadle eBashani leGileyadi, njengensukwini zasendulo.
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
Njengezinsukwini zokuphuma kwakho elizweni leGibhithe, ngizamtshengisa izimangaliso.
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
Izizwe zizabona ziyangeke ngamandla azo wonke; zizabeka isandla phezu komlomo; indlebe zazo zibe yizacuthe.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
Zizakhotha uthuli njengenyoka, njengezihuquzelayo zomhlaba zizathuthumela ekuvalekeni kwazo, zizamesaba uJehova uNkulunkulu wethu, zesabe ngenxa yakho.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
Ngubani onguNkulunkulu njengawe, othethelela isono, adlule esiphambekweni sensali yelifa lakhe? Kagcini ulaka lwakhe kuze kube phakade, ngoba ethokoza emuseni.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
Uzaphenduka, asihawukele; uzanyathelela phansi iziphambeko zethu; wena uzaphosela zonke izono zabo ezinzikini zolwandle.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.
Uzanika iqiniso kuJakobe, umusa kuAbrahama, owakufungela obaba bethu kusukela ensukwini zendulo.

< Mika 7 >