< Mika 7 >

1 Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
Maye ngosizi lwami! Nginjengomuntu obutha izithelo zehlobo senginjengevini eselivunwe laphela; akuselasixha samavini okudliwa, kayisekho lemikhiwa yakuqala engiyikhanukayo.
2 Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
Abathembekileyo babhujisiwe elizweni, kakho lamunye umuntu olungileyo oseleyo. Abantu bonke bacathamela ukuchitha igazi; lowo lalowo uzingela umfowabo ngombule.
3 Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
Izandla zombili zizingcitshi ekwenzeni okubi; umbusi ufuna izipho ngamandla, umahluleli wamukela isivalamlomo, abalamandla babiza abakufisayo, bonke baceba okubi bendawonye.
4 Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
Ongcono wabo unjengesihlahla sameva, oqotho kakhulu mubi kulothango lwameva. Usuku uNkulunkulu alethekelela ngalo selufikile, usuku lokukhala kophondo lwabalindi. Manje sekuyisikhathi sokuphumputheka kwabo.
5 Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
Ungamethembi umakhelwane; ungagwabi ngomngane wakho. Lalowo olala umgonile, qaphela amazwi akho.
6 Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
Ngoba indodana idumaza uyise, indodakazi ivukela unina, umalukazana avukele uninazala, izitha zomuntu ngamalunga endlu yakhe.
7 Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
Kodwa mina ngilindele uThixo ngethemba, ngilindele uNkulunkulu uMsindisi wami; uNkulunkulu wami uzangizwa.
8 Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
Ungaklolodi wena sitha sami! Lanxa ngiwile, ngizavuka. Lanxa ngihlezi emnyameni, uThixo uzakuba yikukhanya kwami.
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
Ngenxa yokuba ngonile kuye, ngizalumela ulaka lukaThixo, aze angincengele endabeni yami, aveze ukungabi lacala kwami. Uzangikhuphela phandle ekukhanyeni; ngizabona ukulunga kwakhe.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
Lapho-ke isitha sami sizakubona, njalo sibanjwe zinhloni, lowo owathi kimi, “Ungaphi uThixo uNkulunkulu wakho?” Lakhathesi uzagxotshwa ngezinyawo njengodaka emigwaqweni.
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
Usuku lokwakhiwa kwemiduli yakho luzafika, usuku lokuqhelisa imingcele yakho.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
Ngalolosuku abantu bazakuza kuwe bevela e-Asiriya lasemadolobheni aseGibhithe, njalo kusukela eGibhithe kusiya kuYufrathe, kusukela olwandle kusiya olwandle, lakusukela entabeni kusiya entabeni.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
Umhlaba uzachitheka ngenxa yabahlezi kuwo, ngenxa yezenzo zabo.
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
Beluse abantu bakho ngentonga yakho, umhlambi welifa lakho, ohlala wodwa ehlathini emadlelweni avundileyo. Kawudle eBhashani laseGiliyadi njengasezinsukwini zokuphuma.
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
“Njengasezinsukwini zokuphuma kwenu eGibhithe, ngizabatshengisa izimangaliso zami.”
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
Izizwe zizabona ziyangeke, zemukwe wonke amandla azo. Zizabamba imilomo yazo ngezandla, lezindlebe zazo zingabe zisezwa.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
Zizakhotha uthuli njengenyoka, njengezinanakazana ezihuquzela emhlabathini. Zizakuza ziqhaqhazela ziphuma emihomeni yazo; zizaphendukela kuThixo uNkulunkulu wethu ngokwesaba, njalo lawe zizakwesaba.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
Ngubani onguNkulunkulu njengawe, oxolela izono athethelele iziphambeko zensalela zelifa lakhe na? Kawuthukutheli kokuphela kodwa uthokoza ngokutshengisa isihawu.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
Uzakuba lesihawu kithi futhi; uzanyathela izono zethu ngezinyawo uphosele bonke ububi bethu ezinzikini zolwandle.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.
Uzakuba qotho kuJakhobe, ubonakalise isihawu sakho ku-Abhrahama, njengokuthembisa kwakho ngesifungo kubokhokho bethu ensukwini zasendulo.

< Mika 7 >