< Mika 7 >

1 Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
A UWE ia'u! no ka mea, ua like au me ka ohi ai ana o ke kau, E like me na koena huawaina o ka ohi ana: Aohe huhui e ai ai; makemake iho la kuu naau i ka hua fiku mua.
2 Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
Ua nalo ka mea lokomaikai mai ka aina aku: Aohe mea pono iwaena o na kanaka; Ke hoohalua nei lakou a pau no ke koko: Hoohei iho lakou, o kela mea keia mea i kona hoahanau, i ka upena.
3 Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
Hana hewa ikaika hoi lakou me na lima; Noi aku ka luna, a me ka lunakanawai i uku: A o ke kanaka nui, oia ke hoike aku i ka makemake o kona naau; Pela no lakou e huikau ai ia mea.
4 Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
O ka mea maikai o lakou ua like me ka laau ooi; A o ka mea pono, ua oioi ia mamua o ka palaau oioi. O ka la o kou poe kiai, a o kou hoopai ana, e hiki mai no ia; Ano e hiki mai ai ko lakou popilikia.
5 Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
Mai hilinai oukou i ka makamaka, Mai paulele i ka hoalauna: E hoopaa i ka puka o kou waha mai ka mea e moe ana ma kou poli.
6 Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
No ka mea, hoowahawaha ke keikikane i kona makuakane, Ku e mai ke kaikamahine i kona makuwahine, O ka hunonawahine i kona makuahunowaiwahine, O na enemi o ke kanaka, o na kanaka no ia o kona hale iho.
7 Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
A e nana aku au ia Iehova: E kali aku au i ke Akua o kuu ola; E hoolohe mai ko'u Akua ia'u.
8 Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
Mai hauoli oe maluna o'u, e ko'u enemi: No ka mea, a i haule iho au, e ala hou ae no: A i noho au i ka pouli, o Iehova ka malamalama no'u.
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
E hoomanawanui no au i ka inaina o Iehova, No ka mea, ua hana hewa no au ia ia, A hoapono mai ia i ka'u mea, A e hoopai aku no ia no'u; A lawe mai no ia ia'u iwaho i ka malamalama, A e ike aku au i kona pono.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
A e ike kou enemi ia mea, A e uhi mai ka hilahila i ka mea i olelo mai ai ia'u, Auhea o Iehova kou Akua? E ike auanei ko'u mau maka ia ia: Ano e hehiia oia ilalo, e like me ka lepo o na alanui.
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
I ka la e hanaia'i kou mau papohaku, Ia la e lawe loa ia'ku ke kanawai.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
Ia la e hele mai ia i ou la mai Asuria mai, a i Aigupita, A mai Aigupita a ka muliwai, A mai ke kai a ke kai, A mai ka mauna a ka mauna.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
Aka, e lilo ka aina i neoneo no ka poe e noho ana iloko, A no ka hua o ka lakou mau hana.
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
E hanai oe i kou poe kanaka me kou kookoo, Ka poe o kou hooilina, ka poe e noho mehameha ana ma ka ululaau, iwaena o Karemela: E ai lakou ma Basana, a ma Gileada, e like me ka manawa kahiko.
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
E like me na la o kou puka ana, mai ka aina o Aigupita mai, E hoike aku au ia ia i na mea kupanaha.
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
E ike mai na lahuikanaka, a e hilahila no ko lakou ikaika a pau; A e kau lakou i ka lima maluna o ka waha, E kuli hoi ko lakou mau pepeiao.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
E palu lakou i ka lepo me he nahesa la, E kolo lakou mai ka lakou mau lua mai, e like me na mea kolo o ka honua, E weliweli lakou ia Iehova ko kakou Akua, A e makau lakou nou.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
Owai la ke Akua e like me oe, e kala ana i ka hewa, A e maalo ae ana i ka hala o ke koena o kona hooilina? Aole ia e hoomau loa aku i kona inaina, No ka mea, ke makemake nei no ia i ke aloha.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
E hoi hou mai no ia, a e aloha mai no ia ia kakou; A hehi ilalo no ia i ko kakou mau hewa; A e hoolei aku oe i ko lakou hewa a pau iloko o ka hohonu o ke kai.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.
A e haawi mai no oe i ka oiaio ia Iakoba, a me ka lokomaikai ia Aberahama, Ka mea au i hoohiki ai i ko makou mau kupuna mai ka wa kahiko mai.

< Mika 7 >