< Mika 7 >

1 Tsoka ine! Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe, pa nthawi yokolola mphesa; palibe phava lamphesa loti nʼkudya, palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
woe! to/for me for to be like/as gathering summer like/as gleaning vintage nothing cluster to/for to eat early fig to desire soul: appetite my
2 Anthu opembedza atha mʼdziko; palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala. Anthu onse akubisalirana kuti aphane; aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
to perish pious from [the] land: country/planet and upright in/on/with man nothing all their to/for blood to ambush man: anyone [obj] brother: compatriot his to hunt net
3 Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa; wolamulira amafuna mphatso, woweruza amalandira ziphuphu, anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna, onse amagwirizana zochita.
upon [the] bad: evil palm to/for be good [the] ruler to ask and [the] to judge (in/on/with recompense *L(abh)*) and [the] great: large to speak: speak desire soul: appetite his he/she/it and to weave her
4 Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga, munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga. Tsiku limene alonda ako ananena lafika, tsiku limene Mulungu akukuchezera. Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
pleasant their like/as briar upright from hedge day to watch you punishment your to come (in): come now to be confusion their
5 Usadalire mnansi; usakhulupirire bwenzi. Usamale zoyankhula zako ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
not be faithful in/on/with neighbor not to trust in/on/with tame from to lie down: lay down bosom: embrace your to keep: guard entrance lip your
6 Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake, mwana wamkazi akuwukira amayi ake, mtengwa akukangana ndi apongozi ake, adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.
for son: child be senseless father daughter to arise: attack in/on/with mother her daughter-in-law in/on/with mother-in-law her enemy man human house: household his
7 Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo, ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga; Mulungu wanga adzamvetsera.
and I in/on/with LORD to watch to wait: wait to/for God salvation my to hear: hear me God my
8 Iwe mdani wanga, usandiseke! Ngakhale ndagwa, ndidzauka. Ngakhale ndikukhala mu mdima, Yehova ndiye kuwunika kwanga.
not to rejoice enemy my to/for me for to fall: fall to arise: rise for to dwell in/on/with darkness LORD light to/for me
9 Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova, chifukwa ndinamuchimwira, mpaka ataweruza mlandu wanga ndi kukhazikitsa chilungamo changa. Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika; ndidzaona chilungamo chake.
rage LORD to lift: bear for to sin to/for him till which to contend strife my and to make: do justice: judgement my to come out: send me to/for light to see: see in/on/with righteousness his
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi nadzagwidwa ndi manyazi, iye amene anandifunsa kuti, “Ali kuti Yehova Mulungu wako?” Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga; ngakhale tsopano adzaponderezedwa ngati matope mʼmisewu.
and to see: see enemy my and to cover her shame [the] to say to(wards) me where? he LORD God your eye my to see: see in/on/with her now to be to/for trampling like/as mud outside
11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu, nthawi yokulitsanso malire anu.
day to/for to build wall your day [the] he/she/it to remove statute: allotment
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto, ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
day he/she/it and till you to come (in): come to/for from Assyria and city Egypt and to/for from Egypt and till River and sea from sea and mountain: mount [the] mountain: mount
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.
and to be [the] land: country/planet to/for devastation upon to dwell her from fruit deed their
14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza, nkhosa zimene ndi cholowa chanu, zimene zili zokha mʼnkhalango, mʼdziko la chonde. Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi monga masiku akale.
to pasture people your in/on/with tribe: staff your flock inheritance your to dwell to/for isolation wood in/on/with midst plantation to pasture Bashan and Gilead like/as day forever: antiquity
15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga, ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”
like/as day to come out: come you from land: country/planet Egypt to see: see him to wonder
16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi, ngakhale ali ndi mphamvu zotani. Adzagwira pakamwa pawo ndipo makutu awo adzagontha.
to see: see nation and be ashamed from all might their to set: put hand upon lip ear their be quiet
17 Adzabwira fumbi ngati njoka, ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi. Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo; mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu ndipo adzachita nanu mantha.
to lick dust like/as serpent like/as to crawl land: soil to tremble from perimeter their to(wards) LORD God our to dread and to fear: revere from you
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu, amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa za anthu otsala amene ndi cholowa chake? Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
who? God like you to lift: forgive iniquity: crime and to pass upon transgression to/for remnant inheritance his not to strengthen: strengthen to/for perpetuity face: anger his for delighting kindness he/she/it
19 Inu mudzatichitiranso chifundo; mudzapondereza pansi machimo athu ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
to return: again to have compassion us to subdue iniquity: crime our and to throw in/on/with depth sea all sin their
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo, ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu, monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu masiku amakedzana.
to give: do truth: faithful to/for Jacob kindness to/for Abraham which to swear to/for father our from day front: old

< Mika 7 >