< Mika 6 >

1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Аскултаць дар че зиче Домнул: „Скоалэ-те, жудекэ-те ынаинтя мунцилор ши дялуриле сэ-ць аудэ гласул!…
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Аскултаць, мунць, причина Домнулуй ши луаць аминте, темелий тарь але пэмынтулуй! Кэч Домнул аре о жудекатэ ку попорул Сэу ши вря сэ Се жудече ку Исраел.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
Попорул Меу, че ць-ам фэкут ши ку че те-ам остенит? Рэспунде-Мь!
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
Кэч те-ам скос дин цара Еӂиптулуй, те-ам избэвит дин каса робией ши ам тримис ынаинтя та пе Мойсе, Аарон ши Мария!
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
Попорул Меу, аду-ць аминте че плэнуя Балак, ымпэратул Моабулуй, ши че й-а рэспунс Балаам, фиул луй Беор, ши че с-а ынтымплат дин Ситим пынэ ла Гилгал, ка сэ куношть бинефачериле Домнулуй!”
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
Ку че вой ынтымпина пе Домнул ши ку че мэ вой плека ынаинтя Думнезеулуй челуй Пряыналт? Ыл вой ынтымпина оаре ку ардерь-де-тот, ку вицей де ун ан?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Дар примеште Домнул оаре мий де бербечь сау зечь де мий де рыурь де унтделемн? Сэ дау еу пентру фэрэделеӂиле меле пе ынтыюл меу нэскут, родул трупулуй меу, пентру пэкатул суфлетулуй меу?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
Ци с-а арэтат, омуле, че есте бине! Ши че алта чере Домнул де ла тине декыт сэ фачь дрептате, сэ юбешть мила ши сэ умбли смерит ку Думнезеул тэу?
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
Гласул Домнулуй стригэ четэций ши омул ынцелепт се теме де Нумеле Тэу. „Аскултаць педяпса ши пе Чел че о тримите!
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Май сунт ын каса челуй рэу коморь нелеӂюите ши блестемата ефэ микэ?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Пот сокоти Еу курат пе чел че аре о кумпэнэ недряптэ ши греутэць стрымбе ын сак?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
Пентру кэ богаций луй сунт плинь де силничие, локуиторий луй спун минчунь ши лимба лор есте нумай ыншелэторие ын гура лор,
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
де ачея, ши Еу те вой лови ку суферинцэ, те вой пустии пентру пэкателе тале.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
Вей мынка, ши тот ну те вей сэтура, чи фоамя ва рэмыне ын тине; че вей луа динаинтя врэжмашулуй ну вей скэпа, кэч че вей скэпа, вой да прадэ сабией.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
Вей семэна, дар ну вей сечера; вей стоарче мэслине, дар ну те вей унӂе ку унтделемнул лор; вей фаче муст, дар ну вей бя вин!
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
Кэч ей пэзеск тоате орындуириле луй Омри ши лукрязэ токмай кум а лукрат каса луй Ахаб ши умблэ дупэ сфатуриле лор, де ачея те вой фаче де поминэ, ыць вой фаче локуиторий де батжокурэ ши вей пурта окара попорулуй Меу.”

< Mika 6 >