< Mika 6 >

1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Lalelani okutshiwo nguThixo ukuthi: “Sukumani lilandise indaba yenu phambi kwezintaba; amaqaqa kawezwe lokho elikutshoyo.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Zwanini, lina zintaba, icala elethulwa nguThixo; lalelani lina zisekelo zomhlaba ezingulaphakade. Ngoba kulecala uThixo alibeka ebantwini bakhe, wethesa u-Israyeli icala.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
Bantu bami, ngenzeni kini na? Ngilihluphe ngani na? Ngiphendulani.
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
Ngalikhupha eGibhithe ngalikhulula elizweni lobugqili. Ngathuma uMosi ukuba alikhokhele kanye lo-Aroni loMiriyemu.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
Bantu bami, khumbulani izicebiso zikaBhalaki inkosi yaseMowabi lokuthi uBhalamu indodana kaBheyori waphendula wathini. Khumbulani uhambo lwenu kusukela eShithima kusiya eGiligali, ukuze lazi imisebenzi elungileyo kaThixo.”
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
Kuyini engizakuza lakho phambi kukaThixo ngikhothame phambi kukaNkulunkulu ophakemeyo na? Ngizakuza phambi kwakhe ngilomnikelo wokutshiswa, ngilamathole alomnyaka owodwa na?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
UThixo angathokoziswa zinqama eziyizinkulungwane, izinkulungwane ezilitshumi zemifula yamafutha na? Ngizanikela izibulo lami ngenxa yokona kwami, isithelo somzimba wami ngenxa yesono somphefumulo wami na?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
Ukutshengisile wena muntu okuhle. UThixo ufunani kuwe na? Ukwenza okulungileyo lokuthanda umusa kanye lokuhamba ngokuzithoba loNkulunkulu wakho.
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
Lalelani! UThixo umemezela kulo idolobho, lokwesaba ibizo lakho kuyikuhlakanipha, “Qaphelani umqwayi laLowo owubekileyo.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Wena ndlu yobubi, kufanele lakhathesi ngiyikhohlwe inotho yakho eyazuzwa ngobubi, lehefa elinganelanga, eliqalekisiweyo na?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Ngizamkhulula yini ecaleni umuntu olezilinganiso zobuqili, lesaka lezilinganiso zamanga na?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
Abantu bakhona abanothileyo balochuku; abantu bakhona ngabaqambi bamanga, lezilimi zabo zikhuluma inkohliso.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
Ngakho sengiqalisile ukukuchitha, ukukuqothula ngenxa yezono zakho.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
Uzakudla kodwa ungasuthi; isisu sakho sizakuba silokhu singelalutho. Uzabuthelela kodwa ungalondolozi lutho, ngoba lokho okulondolozayo ngizakupha inkemba.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
Uzalima kodwa ungavuni; uzakhama ama-oliva kodwa amafutha awo ungawagcobi, uzakhama amavini kodwa iwayini lawo ungalinathi.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
Ugcinile imithetho ka-Omri layo yonke imikhutshana yasendlini ka-Ahabi, walandela lamasiko abo. Ngakho-ke ngizakunikela ekubhujisweni, labantu bakho ekubeni yinhlekisa; uzathwala ihlazo lezizwe.”

< Mika 6 >