< Mika 6 >

1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Écoutez maintenant ce que dit l'Éternel: Lève-toi, plaide devant les montagnes, et que les collines entendent ta voix
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Écoutez, montagnes, le procès de l'Éternel, et vous, immobiles fondements de la terre! Car l'Éternel a un procès avec son peuple, et il veut plaider avec Israël.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
Mon peuple, que t'ai-je fait, ou en quoi t'ai-je causé de la peine? Réponds-moi.
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
Car je t'ai fait monter du pays d'Égypte, je t'ai racheté de la maison de servitude, et j'ai envoyé devant toi Moïse, Aaron et Marie.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
Mon peuple, rappelle-toi donc ce que projetait Balak, roi de Moab, et ce que lui répondit Balaam, fils de Béor, et ce que je fis depuis Sittim à Guilgal, afin que tu connaisses les justes voies de l'Éternel!
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
Avec quoi me présenterai-je devant l'Éternel, et me prosternerai-je devant le Dieu souverain? Irai-je au-devant de lui avec des holocaustes, avec des veaux d'un an?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
L'Éternel prendra-t-il plaisir à des milliers de béliers, à des myriades de torrents d'huile? Donnerai-je mon premier-né pour mon forfait, le fruit de mes entrailles pour le péché de mon âme?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
Il t'a déclaré, ô homme, ce qui est bon. Et qu'est-ce que l'Éternel demande de toi, sinon de faire ce qui est droit, d'aimer la miséricorde, et de marcher humblement avec ton Dieu?
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
La voix de l'Éternel crie à la ville; et celui qui est sage craindra ton nom. Écoutez la verge, et celui qui l'a ordonnée!
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Y a-t-il encore, dans la maison de l'injuste, des trésors injustement acquis, et un épha trop petit, ce qui est abominable?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Serais-je pur avec des balances fausses et de faux poids dans le sac?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
Car ses riches sont pleins de violence, ses habitants profèrent le mensonge, et ils ont une langue trompeuse dans la bouche.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
C'est pourquoi je te frapperai mortellement; je te dévasterai à cause de tes péchés.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
Tu mangeras et tu ne seras point rassasiée, et le vide sera au-dedans de toi; tu mettras de côté, mais tu ne sauveras point, et ce que tu auras sauvé, je le livrerai à l'épée.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
Tu sèmeras, mais tu ne moissonneras point; tu presseras l'olive, mais tu ne t'oindras point d'huile; tu fouleras le moût, et tu ne boiras point de vin.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
On observe les ordonnances d'Omri, et toute la manière de faire de la maison d'Achab, et vous marchez d'après leurs conseils. C'est pourquoi je te livrerai à la désolation, je ferai de tes habitants un objet de raillerie, et vous porterez l'opprobre de mon peuple.

< Mika 6 >