< Mika 6 >
1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Kuulkaa, mitä Herra sanoo: Nouse ja käy oikeutta vuorten kanssa, ja kukkulat kuulkoot sinun äänesi.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Kuulkaa Herran oikeudenkäyntiä, vuoret, te iäti kestävät, maan perustukset; sillä oikeudenkäynti on Herralla kansaansa vastaan, ja Israelin kanssa hän käy tuomiolle:
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
"Minun kansani, mitä minä olen sinulle tehnyt, ja millä olen sinut väsyttänyt? Vastaa minulle!
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
Minähän olen johdattanut sinut Egyptin maasta, vapahtanut sinut orjuuden pesästä; ja minä lähetin Mooseksen, Aaronin ja Mirjamin käymään sinun edelläsi.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
Muista, kansani, mitä oli mielessä Baalakilla, Mooabin kuninkaalla, ja mitä Bileam, Beorin poika, hänelle vastasi, Sittimistä lähtien Gilgaliin asti, että käsittäisit Herran vanhurskaat teot." -
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
"Mitä tuoden minä voisin käydä Herran eteen, kumartua korkeuden Jumalan eteen? Käynkö hänen eteensä tuoden polttouhreja, vuodenvanhoja vasikoita?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Ovatko Herralle mieleen tuhannet oinaat, kymmenettuhannet öljyvirrat? Annanko esikoiseni rikoksestani, ruumiini hedelmän sieluni syntiuhriksi?" -
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
Hän on ilmoittanut sinulle, ihminen, mikä hyvä on; ja mitä muuta Herra sinulta vaatii, kuin että teet sitä, mikä oikein on, rakastat laupeutta ja vaellat nöyrästi Jumalasi edessä?
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
Herran ääni huutaa kaupungille-ja ymmärtäväisyyttä on, että sinun nimestäsi otetaan vaari. Totelkaa vitsaa ja häntä, joka on sen määrännyt.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Vieläkö ovat jumalattoman talossa vääryyden aarteet ja vajaa, kirottu eefa-mitta?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Olisinko minä puhdas, jos minulla olisi väärä vaaka ja kukkarossa petolliset punnuskivet?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
Sen rikkaat ovat täynnä väkivaltaa, sen asukkaat puhuvat valhetta, kieli heidän suussansa on pelkkää petosta.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
Niinpä minäkin lyön sinut sairaaksi, teen sinut autioksi sinun syntiesi tähden.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
Sinä syöt, mutta et tule ravituksi, ja sinun vatsassasi on tyhjyys. Minkä viet pois, sitä et saa pelastetuksi; ja minkä pelastetuksi saat, sen minä annan alttiiksi miekalle.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
Sinä kylvät, mutta et leikkaa. Sinä puserrat öljyä, mutta et öljyllä itseäsi voitele, ja rypälemehua, mutta et viiniä juo.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
Mutta Omrin ohjeita noudatetaan ja kaikkia Ahabin suvun tekoja; ja heidän neuvojensa mukaan te vaellatte, että minä saattaisin sinut autioksi ja sen asukkaat pilkaksi; ja te saatte kantaa minun kansani häväistyksen.