< Mika 6 >

1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Now listen to what Yahweh says, “Arise and state your case before the mountains; let the hills hear your voice.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Listen to Yahweh's lawsuit, you mountains, and you enduring foundations of the earth. For Yahweh has a lawsuit with his people, and he will fight in court against Israel.”
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
“My people, what have I done to you? How have I wearied you? Testify against me!
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
For I brought you up out of the land of Egypt and rescued you out of the house of bondage. I sent Moses, Aaron, and Miriam to you.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
My people, remember what Balak king of Moab devised, and how Balaam son of Beor answered him as you went from Shittim to Gilgal, so you may know the righteous acts of Yahweh.”
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
What should I bring to Yahweh, as I bow down to the high God? Should I come to him with burnt offerings, with calves a year old?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Will Yahweh be pleased with thousands of rams, or with ten thousand rivers of oil? Should I give my firstborn for my transgression, the fruit of my body for my own sin?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
He has told you, man, what is good, and what Yahweh requires from you: Act justly, love kindness, and walk humbly with your God.
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
The voice of Yahweh is making a proclamation to the city— even now wisdom acknowledges your name: “Pay attention to the rod, and to the one who has put it in place.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
There is wealth in the houses of the wicked that is dishonest, and false measures that are abominable.
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Should I consider a person to be innocent if he uses fraudulent scales, with a bag of deceptive weights?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
The rich men are full of violence, the inhabitants have spoken lies, and their tongue in their mouth is deceitful.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
Therefore I will strike you with a terrible blow, and I will make you desolate because of your sins.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
You will eat but not be satisfied; your emptiness will remain inside you. You will store goods away but not save, and what you do save I will give to the sword.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
You will sow but not reap; you will tread the olives but not anoint yourselves with oil; you will press grapes but drink no wine.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
The regulations made by Omri have been kept, and all the deeds of the house of Ahab. You walk by their advice. So I will make you, city, a ruin, and you inhabitants an object of hissing, and you will bear the reproach of my people.”

< Mika 6 >