< Mika 6 >

1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Hear please [that] which Yahweh [is] saying arise conduct a case with the mountains so they may hear the hills voice your.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Hear O mountains [the] case of Yahweh and O enduring [ones] [the] foundations of [the] earth for a case at law [belongs] to Yahweh with people his and with Israel he will argue.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
O people my what? have I done to you and what? have I made weary you testify against me.
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
For I brought up you from [the] land of Egypt and from a house of slaves I ransomed you and I sent before you Moses Aaron and Miriam.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
O people my remember please what? did he plan Balak [the] king of Moab and what? did he answer him Balaam [the] son of Beor from Shittim to Gilgal so as to know [the] righteousness of Yahweh.
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
With what? will I come to meet Yahweh will I bend myself down? to [the] God of height ¿ will I come to meet him with burnt offerings with calves sons of a year.
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
¿ Will he take pleasure Yahweh in thousands of rams in tens of thousands of torrents of oil ¿ will I give firstborn my transgression my [the] fruit of belly my [the] sin of self my.
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
He has told to you O humankind what? [is] good and what? [is] Yahweh requiring from you that except to do justice and to love covenant loyalty and to be modest to walk with God your.
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
[the] voice of Yahweh to the city it calls out and success it will see name your hear O tribe and whoever he appointed it.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Still ¿ [are] there house of [the] wicked treasures of wickedness and an ephah of scantness accursed.
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
¿ Will I be clear with balances of wickedness and with a bag of weights of deceit.
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
Which rich [people] its they are full violence and inhabitants its they speak falsehood and tongue their [is] deceit in mouth their.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
And also I I will make sick [by] striking you I will make desolate [you] on sins your.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
You you will eat and not you will be satisfied and emptiness your [will be] in midst your and you will carry away and not you will bring to safety and [that] which you will bring to safety to the sword I will give.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
You you will sow and not you will reap you you will tread olive[s] and not you will anoint yourself oil and new wine and not you will drink wine.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
So may be kept [the] statutes of Omri and every deed of [the] house of Ahab and you have walked in schemes their so as to make I you into a horror and inhabitants its into hissing and [the] reproach of people my you will bear.

< Mika 6 >