< Mika 6 >
1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Listen to what the Lord is saying. Stand up and plead your case. Let the mountains and the hills hear your voice.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
And now, mountains, hear the Lord's argument. Listen, everlasting foundations of the earth, for the Lord has a case against his people. He will bring charges against Israel.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
My people, what have I done to you? What is it that I have done to make you tired of me?
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
For I brought you out of the land of Egypt and rescued you from slavery. I sent Moses, Aaron, and Miriam to lead you.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
My people, remember what Balak, king of Moab, planned to do, and what Balaam, son of Beor, told him, and what happened from Shittim to Gilgal, so you could know all the good things the Lord does.
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
What should I take with me when I approach the Lord, when I bow down before the God of heaven? Shall I come before him with burnt offerings, with calves a year old?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Will the Lord be pleased with thousands of rams, or ten thousand rivers of olive oil? Shall I sacrifice my firstborn child for my rebellion, my own flesh and blood for the sins I have committed?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
The Lord has told you what is good, and what the Lord asks from you: to do what is right, to love kindness, and to walk in humility with your God.
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
The voice of the Lord calls to the city—to respect your name is to be wise—pay attention to the rod and who summoned it.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Are there still ill-gotten gains in the houses of the wicked? Are they still using dishonest measures in selling grain?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
How can I accept those who use unfair scales and dishonest weights?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
Your rich people make money by using violence; they tell lies and practice deceit.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
So I will strike you to make you ill; I will ruin you because of your sins.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
You will eat, but never be satisfied; inside you will still feel hungry. Even though you try to save money, what you save won't be worth anything because I will give it to the sword.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
You will sow, but you won't reap; you will press your olives, but not use the oil; you will make your wine, but drink none of it.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
You have kept the laws of Omri, and adopted all the practices of the house of Ahab, you have followed their ways. So I will make your country desolate and the people who live there an object of scorn; you will bear the shame of my people.