< Mika 6 >
1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Listen to what the Lord says: Rise, contend in judgment against the mountains, and let the hills hear your voice.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Let the mountains listen to the judgment of the Lord, and the strong foundations of the earth. For the judgment of the Lord is with his people, and he will enter into judgment with Israel.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
My people, what have I done to you, or how have I assailed you? Respond to me.
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
For I led you out of the land of Egypt, and I freed you from the house of servitude, and I sent before your face Moses, and Aaron, and Miriam.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
My people, remember, I ask you, what Balak the king of Moab planned, and how Balaam the son of Beor responded to him, from Shittim even to Gilgal, so that you may know the justice of the Lord.
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
What worthy thing might I offer to the Lord, as I bend the knee before God on high? How could I offer holocausts to him, and one year-old calves?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Would the Lord be pleased with thousands of rams, or with many thousands of fat he-goats? How could I give up my firstborn because of my evil deed, the fruit of my womb because of the sin of my soul?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
I will reveal to you, O man, what is good, and what the Lord requires from you, and how to act with judgment, and to love mercy, and to walk carefully with your God.
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
The voice of the Lord cries out to the city, “Listen, you tribes,” and who will confirm it? And salvation will be for those who fear your name.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Nevertheless, there is a fire in the house of the impious, the treasury of iniquity, and a small measure, filled with wrath.
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Shall I justify unfaithful balances, and the deceitful weighing of a small bag?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
By this, her wealthy have been filled with iniquity, and her inhabitants have spoken lies, and their tongue was deceitful in their mouth.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
And I, therefore, began to strike you with perdition because of your sins.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
You will consume and not be satisfied, and your humiliation will be in your midst. And you will take hold, and not save, and those whom you will save, I will deliver to the sword.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
You will sow, and not reap. You will tread the olives, and not be anointed with oil, and crush the grapes, and not drink the wine.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
For you have kept the precepts of Omri, and all the works of the house of Ahab. And you have walked according their wills, so that I should give you over to perdition and its hissing inhabitants, and you would carry the disgrace of my people.