< Mika 6 >

1 Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
Slyštež nyní, co praví Hospodin: Vstaň, suď se s těmito horami, a nechť slyší pahrbkové hlas tvůj.
2 Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
Slyštež hory rozepři Hospodinovu, i nejpevnější základové země; nebo má rozepři Hospodin s lidem svým, a proti Izraelovi odpor povede.
3 “Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
Lide můj, cožť jsem učinil? A čím jsem tě obtěžoval? Vydej svědectví proti mně.
4 Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
Ješto jsem tě vyvedl z země Egyptské, a z domu služebníků vykoupil jsem tě, a poslal jsem před tváří tvou Mojžíše, Arona a Marii.
5 Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
Lide můj, rozpomeň se nyní, jakou radu skládal Balák král Moábský, a co jemu odpovídal Balám syn Beorův, od Setim až do Galgala, abys poznal hojnou spravedlnost Hospodinovu.
6 Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
Èímž předejdu Hospodina? Skloniti-liž se mám před Bohem nejvyšším? Předejdu-liž ho zápaly, volky ročními?
7 Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
Zalíbí-liž sobě Hospodin v tisících skopců, v mnohokrát desíti tisících potoků oleje? Dám-liž prvorozeného svého za přestoupení své, plod života svého za hřích duše své?
8 Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
Oznámiltě tobě, ó člověče, co jest dobrého, i čehož Hospodin vyhledává od tebe, jediné, abys činil soud, a miloval milosrdenství, a pokorně chodil s Bohem svým.
9 Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
Hlas Hospodinův na město volá (ale sám rozumný spatřuje jméno tvé, ): Slyštež o metle, a kdo ji uložil.
10 Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
Ještě-liž jsou v domě bezbožného pokladové nespravedliví, a míra nespravedlivá a ohavná?
11 Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
Zdaliž ospravedlniti mám vážky nepravé, a v pytlíku kamení falešné?
12 Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
Bohatí jeho plní jsou nátisku, a obyvatelé jeho mluví lež, a jazyk jejich lstivý jest v ústech jejich.
13 Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
Pročež i já také nemoc dopustím, bíti a pléniti tě budu pro hříchy tvé.
14 Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
Ty budeš jísti, a nenasytíš se, a snížení tvé bude u prostřed tebe. Vyneseš zajisté, ale neodneseš, a co vyneseš, vydám pod meč.
15 Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
Ty budeš síti, ale nebudeš žíti; ty tlačiti budeš olivky, ale nebudeš se pomazovati olejem, i mest, ale nebudeš píti vína.
16 Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”
Nebo snažně ostříhá ustanovení Amri, i každého skutku domu Achabova, a spravujete se radami jejich, tak abych tě vydal v zpuštění, a obyvatele jeho v posměch. A protož pohanění lidu mého ponesete.

< Mika 6 >