< Mika 5 >

1 Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
ای دختر افواج، الان در فوجها جمع خواهی شد! ایشان به ضد ما سنگرهابسته‌اند. با عصا بر رخسار داور اسرائیل خواهندزد.۱
2 “Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
و تو‌ای بیت لحم افراته اگر‌چه در هزاره های یهودا کوچک هستی، از تو برای من کسی بیرون خواهد آمد که بر قوم من اسرائیل حکمرانی خواهد نمود و طلوع های او از قدیم و از ایام ازل بوده است.۲
3 Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
بنابراین ایشان را تا زمانی که زن حامله بزاید تسلیم خواهد نمود و بقیه برادرانش با بنی‌اسرائیل بازخواهند گشت.۳
4 Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
و او خواهدایستاد و در قوت خداوند و در کبریایی اسم یهوه خدای خویش (گله خود را) خواهد چرانید وایشان به آرامی ساکن خواهند شد زیرا که او الان تا اقصای زمین بزرگ خواهد شد.۴
5 Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
و او سلامتی خواهد بود. هنگامی که آشور به زمین ما داخل شده، برقصرهای ما قدم نهد، آنگاه هفت شبان و هشت سرور آدمیان را به مقابل او برپا خواهیم داشت.۵
6 Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
و ایشان زمین آشور و مدخل های زمین نمرود رابا شمشیر حکمرانی خواهند نمود و او ما را ازآشور رهایی خواهد داد، هنگامی که به زمین ماداخل شده، حدود ما را پایمال کند.۶
7 Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
و بقیه یعقوب در میان قوم های بسیار مثل شبنم از جانب خداوند خواهد بود و مانند بارشی که بر گیاه می‌آید که برای انسان انتظار نمی کشد و به جهت بنی آدم صبر نمی نماید.۷
8 Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
و بقیه یعقوب در میان امت‌ها و در وسط قوم های بسیار، مثل شیر درمیان جانوران جنگل و مانند شیر ژیان در میان گله های گوسفندان خواهند بود که چون عبورمی نماید پایمال می‌کند و می‌درد و رهاننده‌ای نمی باشد.۸
9 Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
و دست تو بر خصمانت بلند خواهدشد و جمیع دشمنانت منقطع خواهند گردید.۹
10 Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
و خداوند می‌گوید که در آن روز اسبان تورا از میانت منقطع و ارابه هایت را معدوم خواهم نمود.۱۰
11 Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
و شهرهای ولایت تو را خراب نموده، همه قلعه هایت را منهدم خواهم ساخت.۱۱
12 Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
وجادوگری را از دست تو تلف خواهم نمود که فالگیران دیگر در تو یافت نشوند.۱۲
13 Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
و بتهای تراشیده و تمثالهای تو را از میانت نابود خواهم ساخت که بار دیگر به صنعت دست خود سجده ننمایی.۱۳
14 Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
و اشیره هایت را از میانت کنده، شهرهایت را منهدم خواهم ساخت.۱۴
15 Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”
و با خشم و غضب از امت هایی که نمی شنوند انتقام خواهم کشید.۱۵

< Mika 5 >