< Mika 5 >
1 Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo, pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe. Adzakantha ndi ndodo pa chibwano cha wolamulira wa Israeli.
Tanu te hlap laeh. Caem loh mamih taengah vongup a khueh coeng. Israel laitloek kah a kam te caitueng neh a vuek uh pawn ni.
2 “Koma iwe Betelehemu Efurata, ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda, mwa iwe mudzatuluka munthu amene adzalamulira Israeli, amene chiyambi chake nʼchakalekale, nʼchamasiku amakedzana.”
Bethlehem Epharath nang tah Judah a thawng a sang lakli ah a noe la na om. Nang lamkah te kai yueng la thoeng vetih Israel aka taem la om ni. Te dongah hlamat lamkah khosuen tue lamloh a naat nah coeng.
3 Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire. Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.
Te dongah amih te ca-om cacun tue hil a tloeng ni. Te vaengah a manuca hlangrhuel tah Israel ca taengla mael uh ni.
4 Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake mwa mphamvu ya Yehova, mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake. Ndipo iwo adzakhala mu mtendere, pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.
Anih te BOEIPA kah sarhi dongah, a Pathen BOEIPA ming kah mingthennah dongah pai vetih a luem puei ni. Anih te diklai bawt duela rhoeng sak hamla kho a sak ni.
5 Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo. Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa, tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri, ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.
Mamih khohmuen la ha kun vaengah Assyria neh rhoepnah om ni. Mamih kah impuei long a cawt vaengah anih taengah hlang aka dawn parhih neh boeimang hlang parhet neh n'thoo ni.
6 Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga, dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo. Adzatipulumutsa kwa Asiriya akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu kudzatithira nkhondo.
Assyria khohmuen khaw, Nimrod khohmuen neh a thohka khaw cunghang neh luem uh ni. Tedae mamih khohmuen la ha kun tih mah khorhi te a cawt vaengah Assyria lamloh n'huul ni.
7 Otsalira a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu yambiri ya anthu ngati mame ochokera kwa Yehova, ngati mvumbi pa udzu, omwe sulamulidwa ndi munthu kapena kudikira lamulo la anthu.
Jakob kah a meet tah pilnam lakli ah BOEIPA taeng lamkah buemtui bangla, baelhing dongkah mueitui bangla muep om ni. Te te hlang ham lamtawn pawt tih hlang ca ham khaw a ngaiuep dae moenih.
8 Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu, mʼgulu la anthu a mitundu yambiri, ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango. Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa, amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula, ndipo palibe angathe kuzilanditsa.
Jakob rhaengnaeng te pilnam miping khui kah namtom taengah om ni. Duup rhamsa lakli kah sathueng bangla, tuping boiva lakli kah sathuengca bangla te te a pah tih, a taelh tih a baeh phoeiah tah aka huul a om moenih.
9 Mudzagonjetsa adani anu, ndipo adani anu onse adzawonongeka.
Na kut te na rhal soah phuel uh vetih na thunkha rhoek te boeih a saii uh ni.
10 Yehova akuti, “Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse ndi kuphwasula magaleta anu.
BOEIPA kah olphong khohnin te a pai vaengah tah na khui lamkah na marhang te ka hnawt vetih na leng te ka poo sak ni.
11 Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu ndi kugwetsa malinga anu onse.
Na khohmuen kah khopuei rhoek ka hnawt vetih na hmuencak boeih te ka koengloeng ni.
12 Ndidzawononga ufiti wanu ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.
Sungrhai te na kut lamloh ka hnawt vetih kutyaek aka so khaw na taengah om mahpawh.
13 Ndidzawononga mafano anu osema pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu; simudzagwadiranso zinthu zopanga ndi manja anu.
Na mueidaep neh na kaam te na khui lamloh ka hnawt vetih na kut saii taengah na bakop voel mahpawh.
14 Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu, ndipo ndidzawononga mizinda yanu.
Na khui lamloh nang kah Asherah te ka phong vetih na khopuei khaw ka milh sak ni.
15 Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya mitundu imene sinandimvere Ine.”
A yaak uh pawt bangla namtom taengah phulohnah te thintoek neh kosi neh ka saii ni.