< Mika 4 >
1 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
Ale się stanie w ostateczne dni, że utwierdzona będzie góra domu Pańskiego na wierzchu gór, i wywyższona nad pagórki, a narody się do niej zbiegać będą.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
I pójdzie wiele narodów, mówiąc: Pójdźcie, a wstąpmy na górę Pańską, to jest do domu Boga Jakóbowego, a będzie nas nauczał dróg swoich, i będziemy chodzili ścieszkami jego; bo zakon z Syonu wyjdzie, a słowo Pańskie z Jeruzalemu.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Onci sądzić będzie między wieloma narodami, a karać będzie narody mocne na długie czasy; i przekują miecze swe na lemiesze, a oszczepy swe na kosy: nie podniesie miecza naród przeciwko narodowi, ani się więcej ćwiczyć będą do boju
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
Ale każdy będzie siedział pod winną macicą swoją, i pod figowem drzewem swojem, a nie będzie nikt, coby ich przestraszył; bo to usta Pana zastępów mówiły.
5 Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
Bo wszystkie narody chodzić będą, każdy w imieniu boga swego; ale my chodzić będziemy w imieniu Pana, Boga naszego, na wieki wieków.
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
Dnia onego, mówi Pan, zgromadzę chromą i wygnaną zbiorę, i onę, którejm był źle uczynił:
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
A dam tej chromej potomstwo, a precz wygnanej naród możny; i będzie Pan królował nad nimi na górze Syon odtąd aż na wieki.
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
A ty, wieżo trzody, baszto córki Syońskiej! wiedz, że aż do ciebie przyjdzie; przyjdzie mówię, pierwsze państwo, i królestwo córki Jeruzalemskiej.
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
Czemuż teraz tak bardzo krzyczysz? Izali króla niemasz w tobie? Izali radca twój zginął, że cię zjął ból, jako rodzącą?
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
Bolej a stękaj, córko Syońska? jako rodząca; bo już wyjdziesz z miasta, i będziesz mieszkała w polu, a przyjdziesz aż do Babilonu; tam będziesz wybawiona, tam cię Pan odkupi z rąk nieprzyjaciół twoich.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
A choć się teraz zebrało przeciwko tobie wiele narodów, które mówią: Niech będzie splugawiony Syon, a niech na to patrzy oko nasze,
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
Wszakże one nie znają myśli Pańskich, ani rozumieją rady jego, iż je zgromadza jako snopy na bojewisko.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Wstańże, a młóć, córko Syońska! bo róg twój uczynię żelazny, a kopyta twoje uczynię miedziane, i pokruszysz wiele narodów; i poświęcę Panu korzyści ich, a majętności ich Panu wszystkiej ziemi.