< Mika 4 >
1 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
Ngem iti maudi nga al aldaw, mapasamakto a ti bantay ti balay ni Yahweh ket maipasdekto iti rabaw dagiti kabambantayan. Maitan-okto daytoy iti ngatoen dagiti turod, ket agdarisonto dagiti tattao ditoy.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Adu a nasion ti mapan ket kunaenda, “Umaykayo, sumang-attayo idiay bantay ni Yahweh, iti balay ti Dios ni Jacob. Isurona kadatayo dagiti dalanna, ket magnatayo kadagiti dananna. Manipud Sion ket rummuar ti linteg, ken aggapu ti Jerusalem ti sao ni Yahweh.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Mangukomto isuna kadagiti adu a tattao ken mangikeddeng ti maipanggep kadagiti adu a nasion iti adayo. Pitpitendanto dagiti kampilanda tapno agbalin nga arado, ken tapno agbalin met a kumpay dagiti gayangda. Saanton nga ilayat ti nasion ti kampilanna a maibusor iti nasion, wenno adalen no kasano ti makigubat.
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
Ngem ketdi, agtugawto ti tunggal maysa a tao iti sirok ti kaubasanna, ken iti sirok ti kayona nga igos. Awanto ti mangpabuteng kadakuada, ta ti ngiwat ni Yahweh a Mannakabalin amin iti nagsao.
5 Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
Ta magna amin a tattao, tunggal maysa, iti nagan iti diosda. Ngem magnatayonto iti nagan ni Yahweh a Diostayo iti agnanayon nga awan patinggana.
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
“Iti dayta nga aldaw”, kuna ni Yahweh, “Ummongekto dagiti pilay ket urnongekto dagiti napagtalaw, a pinagsagabak.
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
Ket pagbalinekto dagiti pilay a tidda, ken dagiti naitalaw iti nabileg a nasion, ket Siak ni Yahweh ti agturayto kadakuada idiay bantay Sion, ita ken iti agnanayon.
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
Ket sika a pagwanawanan iti arban, turod ti babai nga anak iti Sion, umayto kenka— umayto ti sigud a turay, ti pagarian iti anak a babai ti Jerusalem.
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
Ita, apay nga agsangitka iti nakapigpigsa? Awan kadi ti ari, napukaw kadin ti mammagbagam, dagita nga ut-ot a mangtengtengngel kenka a kasla iti babai nga agpasikal?
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
Agtuok ket agpasngayka, anak a babai ti Sion, a kas iti babai nga agpasikal. Ta manipud ita ket rummuarka iti siudad, agnaedka iti langalang, ken mapanka idiay Babilonia. Maispalkanto sadiay. Isalakanakanto sadiay ni Yahweh manipud kadagiti ima ti kabusormo.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
Adu a nasion ti naguornong ita a maibusor kenka; ket kunada, 'Matulawan koma isuna; makitatayo koma ti pannakadadael ti Sion.'”
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
Kuna dagiti profeta, Saanda nga ammo dagiti pampanunoten ni Yahweh, ken saanda a maawatan dagiti panggepna, ta inurnongna ida a kasla rineppet iti pagir-irikan.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Kuna ni Yahweh, “Bumangonka ket agirikka, O anak a babai ti Sion, ta aramidekto a landok ti saram, ken aramidekto a gambang ti kukom. Adunto ti maparmekmo a tattao. Siak ni Yahweh ket subliekto dagiti binallikogda a kinabaknang, dagiti sanikuada, subliekto, Siak ti Apo ti sangalubongan.”