< Mika 4 >
1 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
Et il arrivera au dernier des jours que la montagne de la maison du Seigneur sera préparée sur le sommet des montagnes, et élevée au-dessus des collines; et des peuples y afflueront.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Et beaucoup de nations se hâteront et diront: Venez, montons à la montagne du Seigneur et à la maison du Dieu de Jacob; et il nous instruira de ses voies, et nous marcherons dans ses sentiers, parce que de Sion sortira la loi, et la parole du Seigneur de Jérusalem.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Et il exercera son jugement sur beaucoup de peuples, et il châtiera des nations puissantes jusqu’aux pays lointains, et ils tailleront leurs glaives en socs de charrue et leurs lances en boyaux; une nation ne prendra pas le glaive contre une autre nation, et ils n’apprendront plus à faire la guerre,
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
Et chacun se reposera sous sa vigne et sous son figuier, et il n’y aura personne qui les effraye, parce que c’est la bouche du Seigneur qui a parlé.
5 Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
Car tous les peuples marcheront chacun au nom de son Dieu; mais nous, nous marcherons au nom du Seigneur Dieu, jusque dans l’éternité et au-delà.
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
En ce jour-là, dit le Seigneur, je rassemblerai celle qui était boiteuse, et je recueillerai celle que j’avais rejetée et celle que j’avais affligée.
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
Je ferai que celle qui était boiteuse ait des restes, et que celle qui avait été dans la peine devienne une nation puissante; et le Seigneur régnera sur eux, sur la montagne de Sion, depuis ce moment jusqu’à jamais.
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
Et toi, tour du troupeau, environnée de nuages, fille de Sion, jusqu’à toi viendra, oui elle viendra, la puissance souveraine, l’empire de la fille de Jérusalem.
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
Pourquoi es-tu maintenant tourmentée par le chagrin? Est-ce que tu n’as point de roi, ou ton conseiller a-t-il péri, puisque la douleur t’a saisie comme une femme qui est en travail?
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
Afflige-toi, et tourmente-toi, fille de Sion, comme une femme en travail, parce que maintenant tu sortiras de la cité, et tu habiteras dans une région étrangère, et tu viendras jusqu’à Babylone; là, tu seras délivrée; là, le Seigneur te rachètera de la main de tes ennemis.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
Et maintenant se sont rassemblées contre toi beaucoup de nations, qui disent: Qu’elle soit lapidée, et que notre œil considère Sion.
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
Mais eux-mêmes n’ont pas connu les pensées du Seigneur, et ils n’ont pas compris que son dessein était de les assembler comme le foin de l’aire.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Fille de Sion, lève-toi et foule aux pieds tes ennemis; parce que je te poserai une corne de fer, et je te poserai des ongles d’airain, et tu briseras beaucoup de peuples, et tu immoleras au Seigneur leurs rapines, et leur puissance au Seigneur de toute la terre.