< Mika 4 >

1 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
And it will be - at [the] end of the days it will be [the] mountain of [the] house of Yahweh established at [the] head of the mountains and it will be lifted up it more than [the] hills and they will stream to it peoples.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
And they will come nations many and they will say come - so we may go up to [the] mountain of Yahweh and to [the] house of [the] God of Jacob so he may teach us from ways his so we may walk in paths his for from Zion it will go out instruction and [the] word of Yahweh from Jerusalem.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
And he will judge between peoples many and he will decide for nations mighty to far away and they will beat swords their into plowshares and spears their into pruning knives not they will lift up nation against nation a sword and not they will learn! again warfare.
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
And they will dwell everyone under own vine his and under own fig tree his and there not [will be one who] terrifies for [the] mouth of Yahweh of hosts it has spoken.
5 Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
For all the peoples they walk everyone in [the] name of own god his and we we will walk in [the] name of Yahweh God our for ever and ever.
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
In the day that [the] utterance of Yahweh I will gather the [one who is] lame and the [one who is] outcast I will assemble and [those] whom I have done harm to.
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
And I will make the [one who was] lame into a remnant and the [one who was] straying into a nation mighty and he will reign Yahweh over them in [the] mountain of Zion from now and until perpetuity.
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
And you O Migdal Eder O hill of [the] daughter of Zion to you it will come and it will come the dominion former a kingdom to [the] daughter of Jerusalem.
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
Now why? do you shout shouting ¿ a king [is] there not in you or? counselor your has he perished that it has taken hold of you anguish like [woman] giving birth.
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
Writhe in pain and burst forth O daughter of Zion like [woman] giving birth for now you will go out from [the] town and you will dwell in the open country and you will go to Babylon there you will be delivered there he will redeem you Yahweh from [the] hand of enemies your.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
And now they have gathered on you nations many that are saying let her be polluted and let it look on Zion eyes our.
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
And they not they know [the] thoughts of Yahweh and not they understand counsel his that he has gathered them like cut grain [the] threshing floor towards.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Arise and thresh O daughter of Zion for horn your I will make iron and hooves your I will make bronze and you will crush peoples many and I will dedicate to destruction to Yahweh unjust gain their and wealth their to [the] lord of all the earth.

< Mika 4 >