< Mika 4 >
1 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
And this shall be: In the last days, the mountain of the house of the Lord will be prepared at the top of the mountains and high above the hills. And the people will flow to it.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
And many nations will hurry, and will say: “Come, let us ascend to the mountain of the Lord and to the house of the God of Jacob. And he will teach us about his ways, and we will walk in his paths.” For the law will go forth from Zion, and the word of the Lord from Jerusalem.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
And he will judge among the many peoples, and he will correct strong nations, even from afar. And they will cut up their swords into plows, and their spears into hoes. Nation will not take up the sword against nation, and they will no longer learn to wage war.
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
And a man will sit under his vine and under his fig tree, and there will be no one to fear, for the mouth of the Lord of hosts has spoken.
5 Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
For all people will walk, each one in the name of his god. But we will walk in the name of the Lord our God, forever and ever.
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
In that day, says the Lord, I will gather together the lame. And I will recover her whom I had rejected, and her whom I had afflicted.
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
And I will place the lame within the remnant, and she who had been in distress, within a healthy people. And the Lord will reign over them on Mount Zion, from the present time and even unto eternity.
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
And you, cloudy tower of the flock of the daughter of Zion, even to you it will come. And the first power will arrive, the kingdom to the daughter of Jerusalem.
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
Now, why have you come together in grief? Is there not a king in you, or has your counselor gone away? For sorrow has overtaken you, like the pain of giving birth.
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
Be grieved and overwhelmed, daughter of Zion, like a woman giving birth. For now you must depart from the city and dwell in the countryside, and you will approach even to Babylon. There you will be delivered. There the Lord will redeem you from the hand of your adversaries.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
And now many peoples have been gathered together against you, and they say, “Let her be stoned and let our eyes gaze upon Zion.”
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
But they have not known the thoughts of the Lord, and they have not understood his counsel. For he has gathered them together like hay on a threshing floor.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Rise and thresh, daughter of Zion. For I will set your horn like iron, and I will set your hoofs like brass. And you will shatter many peoples, and you will immolate their spoils for the Lord, and their strength for the Lord of the whole earth.