< Mika 4 >

1 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
But in the latter days it shall come to pass, that the mountain of Jehovah's house shall be established on the top of the mountains, and it shall be exalted above the hills, and peoples shall flow to it.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
And many nations shall go and say, Come ye, and let us go up to the mountain of Jehovah, and to the house of the God of Jacob, and he will teach us of his ways, and we will walk in his paths. For out of Zion shall go forth the law, and the word of Jehovah from Jerusalem.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
And he will judge between many peoples, and will decide concerning strong nations afar off. And they shall beat their swords into plowshares, and their spears into pruning-hooks. Nation shall not lift up sword against nation, nor shall they learn war any more.
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
But they shall sit every man under his vine and under his fig tree, and none shall make them afraid. For the mouth of Jehovah of hosts has spoken it.
5 Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
For all the peoples walk each one in the name of his god. And we will walk in the name of Jehovah our God forever and ever.
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
In that day, says Jehovah, I will assemble that which is lame, and I will gather that which is driven away, and that which I have afflicted.
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
And I will make that which was lame a remnant, and that which was cast far off a strong nation. And Jehovah will reign over them in mount Zion from henceforth even forever.
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
And thou, O tower of the flock, the hill of the daughter of Zion, to thee it shall come. Yea, the former dominion shall come, the kingdom of the daughter of Jerusalem.
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
Now why do thou cry out aloud? Is there no king in thee? Has thy counselor perished, that pangs have taken hold of thee as of a woman in travail?
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
Be in pain, and labor to bring forth, O daughter of Zion, like a woman in travail. For now thou shall go forth out of the city, and shall dwell in the field, and shall come even to Babylon. There thou shall be rescued. There Jehovah will redeem thee from the hand of thine enemies.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
And now many nations are assembled against thee, who say, Let her be defiled, and let our eye see our desire upon Zion.
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
But they know not the thoughts of Jehovah, nor do they understand his counsel, for he has gathered them as the sheaves to the threshing-floor.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Arise and thresh, O daughter of Zion, for I will make thy horn iron, and I will make thy hoofs brass, and thou shall beat many peoples in pieces. And I will devote their gain to Jehovah, and their substance to the Lord of the whole earth.

< Mika 4 >