< Mika 4 >

1 Mʼmasiku otsiriza, phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse. Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse, ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.
Eso da misunu amoga goumi amo da Debolo diasu danebe amo goumi da eno agolo baligili gadodafa heda: i ba: mu. Fifi asi gala bagohame da amo goumiga gilisila misunu.
2 Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti, “Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova, ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo. Iye adzatiphunzitsa njira zake, ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.” Malangizo adzachokera ku Ziyoni, mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.
Amogai dunu ilia da amane sia: mu, “Niniamone, Hina Gode Ea agologa heda: la: di! Niniamone Isala: ili Hina Gode Ea Debolo Diasuga ahoa: di! E da ninia hamoma: ne, Ea dawa: i amo ninima olelemu. Ninia da logo Ea nini masa: ne ilegei, amoga masunu. Bai Hina Gode Ea olelesu da Yelusalemeganini maha. Amola Saione amoganini E da Ea fi dunuma adosa.
3 Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe. Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera. Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina, kapena kuphunziranso za nkhondo.
Hina Gode da fifi asi gala (gasa bagade fi badilia amola gadenene esalebe) amo ganodini sia: waisu olofoma: ne hahamonesimu. Ilia da ilila: gegesu gobihei dadabili salalu, bu osobo gidinasu hamomu. Amola ilia: goge agei dadabili salalu, ifa dadamusu gobihei hamomu. Fifi asi gala da bu hamedafa ha lamu, amola bu gegemusa: hamedafa momagemu.
4 Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu, ndipo palibe amene adzawachititse mantha, pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.
Dunu huluanedafa da olofole esalumu. Ilia da ilila: waini sagai amola figi sagai ouligisa esalumu, amola dunu enoga ili beda: ma: ne hame hamomu. Bai Hina Gode Bagadedafa da amane ilegele sia: i dagoi.
5 Mitundu yonse ya anthu itha kutsatira milungu yawo; ife tidzayenda mʼnjira za Yehova Mulungu wathu mpaka muyaya.
Fifi asi gala higagale da ilila: loboga hahamoi ‘gode’ ilima nodone sia: ne gadosa, amola ilima fa: no bobogesa. Be ninia da ninia: Hina Godema nodone sia: ne gadosa, amola Ea hamoma: ne sia: i defele hahamona ahoanumu.
6 “Tsiku limenelo, Yehova akuti, “ndidzasonkhanitsa olumala; ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa ndiponso amene ndinawalanga.
Hina Gode da amane sia: sa, “Eso da mana, amoga, Na da dunu ilima Na se bidi i, amola mugululi asiba: le se nabalu, amo huluane gegedole gilisilisimu.
7 Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala. Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu. Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.
Ilia da lologoidafa amola ilia sogedafa amoga badiliadafa esafula. Be Na da hame bogogia: i esalebe dunu, ilima hou gaheabolo hemomu. Amasea ilia da gasa bagade fi ba: mu. Na da amogainini Saione Goumia ili mae fisili ouligilalumu.”
8 Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga, iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni, ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe; ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”
Gode da Yelusaleme amo ganodini esala. E da sibi ouligisu dunu agoane Ea fi dunu sosodo ouligisa. Amo esoha, Yelusaleme da ea musa: ouligi soge (Isala: ili) amoma bisilua moilai bai bagade bu ba: mu.
9 Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula, kodi ulibe mfumu? Kodi phungu wako wawonongedwa, kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?
Yelusaleme fi! Dilia abuliba: le ha: gidafa uli sasalisa disala: ? Abuliba: le uda mano lasea, se nababe defele a: iya gusa: sala: ? Bai dilia da hina bagade hame ganabela: ? Amola dili fada: i sia: su dunu da bogobela: ?
10 Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mayi pa nthawi yake yobereka, pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda ndi kugona kunja kwa mzindawo. Udzapita ku Babuloni; kumeneko udzapulumutsidwa, kumeneko Yehova adzakuwombola mʼmanja mwa adani ako.
Yelusaleme fi dunu, dili da uda ilia mano lasea sega soiyalabe amo defele soiyalaha gusa: ma! Be waha dilia da moilai bai bagade fi bai amo yolesili amola soge hamega fimu. Dilia da Ba: bilonega masunu, be amoga Hina Gode da dima ha lai dunu ilia di wadela: lesisa: besa: le gaga: mu.
11 Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu yasonkhana kulimbana nawe. Iwo akuti, “Tiyeni timudetse, maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”
Fifi asi gala bagohame da dima doagala: musa: gilisi dagoi. Ilia da amane sia: sa, “Yelusaleme da gugunufinisi dagoi ba: ma: ma! Ninia da amo Yelusaleme fi bagade amo wadela: le gugunufinisi ba: ma: ma!”
12 Koma iwo sakudziwa maganizo a Yehova; iwo sakuzindikira cholinga chake, Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.
Be amo fifi asi gala ilia Hina Gode Ea asigi dawa: su amo ganodini dialebe, amo hamedafa dawa: sa. Gode da ili gilisilisilalu, se iasu amo da widi dadabisu defele ilima se imunu, amo ilia hame dawa: digisa.
13 “Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo; ndidzakupatsa ziboda zamkuwa ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.” Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova, chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.
Hina Gode da amane sia: sa, “Yelusaleme fi dunu! Dilia da asili, dilima ha lai dunu ilima se ima. Na da dilima gasa bagade bulamagau amo da gula ‘hono’ agoai amola balasega hamoi emosasafo adobo amo ea gasa agoane hamomu. Dilia da fifi asi gala bagohame banenesimu. Ilia da gegenana lai liligi amo huluane Nama udigili imunu. Bai Na osobo bagade fifi asi gala huluanedafa amo ilia Hina Gode esala.

< Mika 4 >