< Mika 3 >
1 Ndipo ine ndinati, “Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli. Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
Przetoż mówię: Słuchajcie przedniejsi w Jakóbie, i wodzowie domu Izraelskiego! izali wy nie macie być powiadomi sądu?
2 inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa; inu amene mumasenda khungu la anthu anga, ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
Ale oni nienawidzą dobrego, a miłują złe; odzierają lud z skóry ich, i mięso ich z kości ich;
3 inu amene mumadya anthu anga, mumasenda khungu lawo ndi kuphwanya mafupa awo; inu amene mumawadula nthulinthuli ngati nyama yokaphika?”
A jedzą mięso ludu mojego, a skórę ich z nich zdzierają, i kości ich łamią, i rąbią je jako do garnca, a jako mięso do kotła.
4 Pamenepo adzalira kwa Yehova, koma Iye sadzawayankha. Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
Tedy do Pana wołać będą, a nie wysłucha ich, owszem, zakryje oblicze swoje przed nimi czasu onego, tak jako oni wykonywali złe przedsięwzięcia swoje.
5 Yehova akuti, “Aneneri amene amasocheretsa anthu anga, ngati munthu wina awapatsa chakudya amamufunira ‘mtendere;’ ngati munthu wina sawapatsa zakudya amamulosera zoyipa.
Tak mówi Pan o tych prorokach, którzy w błąd zawodzą lud mój, a kąsając zębami swemi opowiadają pokój, a przeciwko temu, któryby im nic do gęby nie dał, wojnę podnoszą.
6 Nʼchifukwa chake kudzakuderani, simudzaonanso masomphenya, mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso. Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
Dlatego się wam widzenie obróci w noc, a wieszczba wasza w ciemność; bo tym prorokom słońce zajdzie, a dzień im się zaćmi.
7 Alosi adzachita manyazi ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa. Onse adzaphimba nkhope zawo chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
I będą się wstydzili oni widzący, a wieszczkowie się zapłoną, a ci wszyscy zakryją zwierzchnią wargę swoję, przeto, że nie będzie żadnej odpowiedzi Bożej.
8 Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu, ndi Mzimu wa Yehova, ndi kulungama, ndi kulimba mtima, kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo, kwa Israeli za tchimo lake.
Alem ja napełniony siłą ducha Pańskiego i sądem i mocą, abym oznajmił Jakóbowi przestępstwa jego, a Izraelowi grzech jego.
9 Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli, inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama; ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
Słuchajcież już tego przedniejsi w domu Jakóbowym, i wodzowie domu Izraelskiego, którzy macie sąd w obrzydliwości, a co jest sprawiedliwego, podwracacie.
10 inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi, ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
Każdy buduje Syon krwią, a Jeruzalem nieprawością.
11 Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze, ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire, ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama. Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti, “Kodi Yehova sali pakati pathu? Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
Przedniejsi jego sądzą według darów, a kapłani jego za zapłatę uczą, a prorocy jego za pieniądze prorokują; a przecie na Panu polegają, mówiąc: Izali nie jest Pan w pośrodku nas? Nie przyjdzieć na nas nic złego.
12 Choncho chifukwa cha inu, Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.
Przetoż Syon dla was jako pole poorany będzie, a Jeruzalem w gromady gruzu obrócone będzie, a góra domu Bożego w wysokie lasy.