< Mika 3 >
1 Ndipo ine ndinati, “Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli. Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
Then I said, “Please listen, leaders of the descendants of Jacob, people of Israel. You are meant to know the difference between right and wrong,
2 inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa; inu amene mumasenda khungu la anthu anga, ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
you who hate good and love evil! You tear off their skin, and rip the flesh from their bones.
3 inu amene mumadya anthu anga, mumasenda khungu lawo ndi kuphwanya mafupa awo; inu amene mumawadula nthulinthuli ngati nyama yokaphika?”
You eat the flesh of my people, you strip off their skin, you break their bones. You chop them up like meat for the saucepan, like flesh for the cooking pot.”
4 Pamenepo adzalira kwa Yehova, koma Iye sadzawayankha. Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
Then they'll cry out to the Lord, but he won't answer them. He will turn away from them at that time because of the evil things they have done.
5 Yehova akuti, “Aneneri amene amasocheretsa anthu anga, ngati munthu wina awapatsa chakudya amamufunira ‘mtendere;’ ngati munthu wina sawapatsa zakudya amamulosera zoyipa.
This is what the Lord says about the prophets who deceive my people. To those who feed them they prophesy peace to them, while to those who do not they prophesy war against them.
6 Nʼchifukwa chake kudzakuderani, simudzaonanso masomphenya, mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso. Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
Therefore it will be like night for you, with no visions; dark, with no predictions. The sun will set on these prophets; their day will end in darkness.
7 Alosi adzachita manyazi ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa. Onse adzaphimba nkhope zawo chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
The seers will be disgraced, the fortune-tellers put to shame, and they will cover their faces because none of them receive any answer from God.
8 Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu, ndi Mzimu wa Yehova, ndi kulungama, ndi kulimba mtima, kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo, kwa Israeli za tchimo lake.
But as for me, I am filled with power, with the spirit of the Lord. I am filled with justice and strength to make clear to the descendants of Jacob their rebellion, and to the people of Israel their sin.
9 Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli, inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama; ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
Listen to me, leaders of the descendants of Jacob and the people of Israel, you who hate justice and distort all that is right.
10 inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi, ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
You are building Zion with blood, and Jerusalem with evil.
11 Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze, ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire, ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama. Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti, “Kodi Yehova sali pakati pathu? Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
Your leaders judge for a bribe, and your priests teach for a price, and your prophets only prophesy for pay. Yet they all lean on the Lord saying, “Isn't the Lord here with us? Nothing bad can happen to us!”
12 Choncho chifukwa cha inu, Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.
Therefore because of you Zion will become a ploughed field and Jerusalem a heap of rubble, and the Temple mount will be overgrown.