< Mika 3 >
1 Ndipo ine ndinati, “Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli. Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
Da sagde jeg: Hør dog, I Jakobs Høvdinger, I Dommere af Israels Hus! Kan Kendskab til Ret ej ventes af eder,
2 inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa; inu amene mumasenda khungu la anthu anga, ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
I, som hader det gode og elsker. det onde, I, som flår Huden af Folk. og Kødet af deres Ben,
3 inu amene mumadya anthu anga, mumasenda khungu lawo ndi kuphwanya mafupa awo; inu amene mumawadula nthulinthuli ngati nyama yokaphika?”
æder mit Folks Kød og flænger dem Huden af Kroppen, sønderbryder deres Ben. og breder dem som Kød i en Gryde, som Suppekød i en Kedel?
4 Pamenepo adzalira kwa Yehova, koma Iye sadzawayankha. Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
Engang skal de råbe til HERREN, han lader dem uden Svar; da skjuler han sit Åsyn for. dem, fordi deres Gerninger er onde.
5 Yehova akuti, “Aneneri amene amasocheretsa anthu anga, ngati munthu wina awapatsa chakudya amamufunira ‘mtendere;’ ngati munthu wina sawapatsa zakudya amamulosera zoyipa.
Så siger HERREN om Profeterne, de, som vildleder mit Folk, de, som råber om Fred, når kun de får noget at tygge, men ypper Krig med den, der intet giver dem i Munden:
6 Nʼchifukwa chake kudzakuderani, simudzaonanso masomphenya, mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso. Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
Derfor skal I opleve Nat uden. Syner, Mørke, som ej bringer Spådom; Solen skal gå ned for Profeterne, Dagen skal sortne for dem.
7 Alosi adzachita manyazi ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa. Onse adzaphimba nkhope zawo chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
Til Skamme skal Seeren blive, blues skal de, som spår; alle skal tilhylle Skægget, thi Svar er der ikke fra Gud.
8 Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu, ndi Mzimu wa Yehova, ndi kulungama, ndi kulimba mtima, kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo, kwa Israeli za tchimo lake.
Jeg derimod er ved HERRENs Ånd fuld af Styrke, af Ret og af Kraft til at forkynde Jakob dets Brøde, Israel, hvad det har syndet.
9 Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli, inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama; ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
Hør det, I Jakobs Huses Høvdinger, I Dommere af Israels Hus, I, som afskyr Ret og gør alt, som er lige, kroget,
10 inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi, ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
som bygger Zion med Blod. og Jerusalem med Uret.
11 Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze, ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire, ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama. Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti, “Kodi Yehova sali pakati pathu? Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
Dets Høvdinger dømmer for Gave, dets Præster kender Ret for Løn; dets Profeter spår for Sølv og støtter sig dog til HERREN: "Er HERREN ej i vor Midte? Over os kommer intet ondt."
12 Choncho chifukwa cha inu, Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.
For eders, Skyld skal derfor Zion pløjes som en Mark, Jerusalem blive til Grushobe, Tempelbjerget til Krathøj.