< Mika 3 >

1 Ndipo ine ndinati, “Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli. Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
Protož pravím: Slyštež již přední v Jákobovi, a vůdcové domu Izraelského: Zdaliž vy nemáte povědomi býti soudu?
2 inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa; inu amene mumasenda khungu la anthu anga, ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
Nenávidí dobrého a milují zlé, sdírají s lidu kůži jejich, a maso jejich s kostí jejich.
3 inu amene mumadya anthu anga, mumasenda khungu lawo ndi kuphwanya mafupa awo; inu amene mumawadula nthulinthuli ngati nyama yokaphika?”
A jedí maso lidu mého, a kůži jejich s nich svláčejí, i kosti jejich rozlamují, a rozdělují jako do hrnce, a jako maso do kotlíku.
4 Pamenepo adzalira kwa Yehova, koma Iye sadzawayankha. Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
Tehdy volati budou k Hospodinu, a nevyslyší jich, ale skryje tvář svou před nimi v ten čas, tak jakž oni vykonávali zlá předsevzetí svá.
5 Yehova akuti, “Aneneri amene amasocheretsa anthu anga, ngati munthu wina awapatsa chakudya amamufunira ‘mtendere;’ ngati munthu wina sawapatsa zakudya amamulosera zoyipa.
Takto praví Hospodin o těch prorocích, kteříž v blud uvodí lid můj, a hryzouce zuby svými, vyhlašují pokoj, a proti tomu, kdož by jim nic do úst nedal, válku vyzdvihují.
6 Nʼchifukwa chake kudzakuderani, simudzaonanso masomphenya, mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso. Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
A protož obrátí se vám vidění v noc, a předpovídání vaše v tmu; nebo zajde slunce těm prorokům, a zatmí se jim den.
7 Alosi adzachita manyazi ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa. Onse adzaphimba nkhope zawo chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
I budou se hanbiti ti vidoucí, a styděti ti věštci, a zastrou bradu svou všickni napořád, proto že nebude žádné odpovědi Boží.
8 Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu, ndi Mzimu wa Yehova, ndi kulungama, ndi kulimba mtima, kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo, kwa Israeli za tchimo lake.
Ale já naplněn jsem silou Ducha Hospodinova, a soudem i udatností, abych oznámil Jákobovi zpronevěření jeho, a Izraelovi hřích jeho.
9 Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo, inu olamulira nyumba ya Israeli, inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama; ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
Slyštež již toto přední v domě Jákobově, a vůdcové domu Izraelského, kteříž v ošklivosti mají soud, a cožkoli jest pravého, převracejí:
10 inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi, ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
Každý vzdělává Sion vraždami, a Jeruzalém nepravostí.
11 Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze, ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire, ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama. Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti, “Kodi Yehova sali pakati pathu? Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
Jehož přední podlé darů soudí, a kněží jeho ze mzdy učí, a proroci jeho z peněz hádají, a však na Hospodina zpoléhají, říkajíce: Zdaliž Hospodina není u prostřed nás? Nepřijdeť na nás nic zlého.
12 Choncho chifukwa cha inu, Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.
A protož vaší příčinou Sion jako pole orán bude, a Jeruzalém v hromady obrácen bude, a hora domu toho v vysoké lesy.

< Mika 3 >