< Mika 2 >
1 Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
Malheur à vous, qui songez à l’inutile, et qui inventez le mal sur vos lits; à la lumière du matin ils l’accomplissent, parce que c’est contre Dieu qu’est élevée leur main.
2 Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
Et ils ont convoité des champs, et ils les ont pris violemment; et ils ont usurpé des maisons; et ils opprimaient un homme et sa maison; un autre homme et son héritage.
3 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
C’est pour cela, voici ce que dit le Seigneur: Voici que moi je prépare pour cette famille un malheur dont vous ne retirerez pas vos cous, et vous ne marcherez pas en superbes, parce que c’est un temps très mauvais.
4 Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
En ce jour-là, vous serez pris pour un sujet de parabole, et avec un doux plaisir sera chantée la chanson de ceux qui diront: Par la désolation nous avons été ravagés; la portion de mon peuple a été changée; comment se retirera-t-il de moi, puisqu’il reviendra pour partager nos contrées?
5 Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
À cause de cela, il n’y aura personne qui mette le cordeau de partage dans l’assemblée du Seigneur.
6 Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
Ne dites point sans cesse: Il ne répandra pas ses oracles sur eux, la confusion ne les couvrira pas.
7 Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
La maison de Jacob dit: Est-ce que l’esprit du Seigneur a été raccourci, ou est-ce que telles sont ses pensées? Mes paroles ne sont-elles pas favorables à celui qui marche dans la droiture?
8 Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
Mais, au contraire, mon peuple s’est levé en adversaire; de dessus la tunique, vous avez enlevé le manteau; et ceux qui passaient de bonne foi, vous les avez tournés à la guerre.
9 Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
Vous avez chassé les femmes de mon peuple de la maison de leurs délices; vous avez enlevé ma louange à leurs petits enfants pour jamais.
10 Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
Levez-vous, et allez, parce qu’il n’y a point de repos ici pour vous; à cause de son impureté, cette terre sera corrompue d’une putréfaction horrible.
11 Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
Plût à Dieu que je fusse un homme n’ayant pas l’esprit prophétique, et que je parlasse plutôt mensonge! je le verserai le vin de la colère de Dieu, et je t’enivrerai; et celui pour qui il sera versé, sera ce peuple.
12 “Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
Je te rassemblerai certainement tout entier, ô Jacob; je réunirai les restes d’Israël; je les mettrai tous ensemble comme dans une bergerie, comme un troupeau au milieu de son parc; une multitude d’hommes y causera du tumulte.
13 Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”
Car celui qui ouvrira le chemin, montera devant eux: ils se partageront, et passeront à la porte et entreront par elle; et leur roi passera en leur présence, et le Seigneur sera à leur tête.