< Mika 2 >
1 Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
Ils se préparent des peines; même sur leurs couches, ils songent à faire le mal; ils le font, dès que le jour paraît, parce qu'ils n'ont pas élevé les mains vers Dieu.
2 Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
Ils ont désiré des champs, et ils ont dépouillé des orphelins; ils ont opprimé des familles; ils ont pris l'un avec sa demeure, l'autre avec son héritage.
3 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
À cause de cela, le Seigneur a dit: Voilà que Je pense à me venger de cette tribu; vous ne relèverez plus la tête, et vous ne marcherez plus droit d'un pas superbe, parce que les temps sont mauvais.
4 Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
En ces jours-là, vous serez des sujets de fables, et l'on chantera sur vous une lamentation, disant: Nous sommes accablés de misère; la part de mon peuple a été mesurée au cordeau, et nul n'était là pour empêcher le ravisseur et le mettre en fuite, et nos champs ont été partagés.
5 Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
À cause de cela, nul n'étendra plus le cordeau pour te faire ta part de terre. Dans l'Église du Seigneur,
6 Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
ne versez point de larmes, et qu'on ne pleure point sur ces choses; car Il ne rétractera pas Ses reproches,
7 Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
Celui qui dit: La maison de Jacob a irrité l'Esprit du Seigneur. N'est-ce point sa coutume? Les paroles du Seigneur ne sont-elles pas justes sur ce peuple? Et n'ont-elles pas cheminé avec droiture?
8 Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
Jadis Mon peuple s'est soulevé en ennemi contre Sa paix. On l'a écorché et on lui a enlevé la peau comme pour lui ôter l'espérance, dans les brisements de la guerre.
9 Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
Les chefs de Mon peuple seront précipités de leurs maisons de délices; et à cause de leurs mœurs perverses, ils ont été rejetés. Allez aux montagnes éternelles.
10 Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
Lève-toi et marche; car il n'est plus pour toi de repos à cause de ton impureté. Vous êtes perdus de corruption;
11 Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
vous avez fui quand personne ne vous poursuivait. L'esprit du mal a produit le mensonge, il s'est infiltré en toi comme le vin et l'ivresse. Et voici ce qui arrivera: d'une goutte de sang de ce peuple,
12 “Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
il en naîtra la réunion de Jacob et de toutes ses tribus; Je recueillerai avec amour les restes d'Israël, et Je les ferai retourner au même lieu. Comme des brebis dans l'angoisse, comme un menu troupeau au milieu de son parc, ils s'élanceront des contrées des hommes,
13 Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”
à travers la brèche ouverte devant eux; ils en ont franchi l'ouverture, ils ont passé la porte par où ils étaient sortis; leur roi est devant eux, et le Seigneur sera le premier à leur tête.