< Mika 2 >
1 Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
Malheur à ceux qui conçoivent l'iniquité. et travailler le mal sur leurs lits! Quand le matin est clair, ils le pratiquent, parce que c'est au pouvoir de leur main.
2 Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
Ils convoitent les champs et les saisissent, et les maisons, alors emmenez-les. Ils oppriment un homme et sa maison, même un homme et son héritage.
3 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
C'est pourquoi Yahvé dit: « Voici que je prépare contre ce peuple un désastre, dont vous ne sortirez pas le cou, vous ne marcherez pas non plus de manière hautaine, car c'est un mauvais moment.
4 Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
En ce jour-là, ils inventeront une parabole contre toi, et se lamenter avec une lamentation lugubre, en disant, Nous sommes complètement ruinés! Les biens de mon peuple sont divisés. En effet, il me le prend et attribue nos champs à des traîtres! »
5 Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
C'est pourquoi, dans l'assemblée de l'Éternel, vous n'aurez pas de personne qui partage le pays par tirage au sort.
6 Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
« Ne prophétisez pas! » - ils prophétisent... « Ne prophétisez pas sur ces choses. La disgrâce ne nous rattrapera pas. »
7 Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
On dira: Maison de Jacob, « L'Esprit de Yahvé est-il en colère? Est-ce que ce sont ses actes? Mes paroles ne font-elles pas du bien à celui qui marche sans reproche? »
8 Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
Mais ces derniers temps, mon peuple s'est levé comme un ennemi. Vous dépouillez la robe et les vêtements de ceux qui passent sans s'en soucier, au retour de la bataille.
9 Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
Vous chassez les femmes de mon peuple de leurs maisons agréables; de leurs jeunes enfants, vous enlevez ma bénédiction pour toujours.
10 Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
Levez-vous, et partez! Car ceci n'est pas votre lieu de repos, à cause de l'impureté qui détruit, même avec une grave destruction.
11 Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
Si un homme, marchant dans un esprit de mensonge, ment en disant, « Je vous prophétiserai du vin et des boissons fortes, » il serait le prophète de ce peuple.
12 “Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
Je vous rassemblerai tous, Jacob. Je rassemblerai le reste d'Israël. Je les rassemblerai comme les moutons de Bozrah, comme un troupeau au milieu de leur pâturage. Ils vont grouiller de monde.
13 Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”
Celui qui ouvre le chemin monte devant eux. Ils franchissent la porte et sortent. Leur roi s'éteint avant eux, avec Yahvé à leur tête.