< Mika 2 >

1 Tsoka kwa amene amakonzekera chiwembu, kwa amene amakonzekera kuchita zoyipa usiku pa mabedi awo! Kukacha mmawa amakachitadi chifukwa ali ndi mphamvu zochitira zimenezo.
Amo mae golale sidagane esala wadela: i hou hamomusa: ilegelalebe dunu ilia da se bagade nabimu! Soge da hadigila dasea, ilia da hamomu dibi ba: sea, ilia da ili wadela: i hou hamomusa: ilegei amo defele hamosa.
2 Amasirira minda ndi kuyilanda, amasirira nyumba ndi kuzilanda. Amatenga nyumba ya munthu mwachinyengo, munthu mnzawo kumulanda cholowa chake.
Ilia da soge lamusa: dawa: sea, ilia da amo soge ilia suguli lasa. Ilia da diasu lamusa: dawa: sea, ilia da amo diasu lasa. Dunu afae ea sosogo amola liligi da noga: le dialebe da hamedafa ba: sa.
3 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Ine ndikukonzekera kubweretsa tsoka pa anthu awa, tsoka limene simudzatha kudzipulumutsa nokha. Inu simudzayendanso monyada, pakuti idzakhala nthawi ya masautso.
Amaiba: le Hina Gode da amane sia: sa, “Na da dilima gugunufinisisu hou dilima imunusa: ilegelala, amasea dilia da amoga hobeale masunu logo hamedafa ba: mu. Dilia da dilisu fawane bidi hamosu ganodini esalebe ba: mu, amasea dilia da hahawane hidala ahoasu amo bu hame hamomu.
4 Tsiku limenelo anthu adzakuchitani chipongwe; adzakunyogodolani ndi nyimbo iyi yamaliro: ‘Tawonongeka kotheratu; dziko la anthu anga lagawidwa. Iye wandilanda! Wapereka minda yathu kwa anthu otiwukira.’”
Amo esoha da doaga: sea, dunu ilia da gugunufinisisu hou dilima doaga: i, dunu eno gugunufinisisu hou dawa: digima: ne ilima adodolalumu, amola ilia dilima hamoi amo dadawa: lu, heawini goe gesami hea: mu; “Nini da dafawanedafa wadela: lesi dagoi. Hina Gode da ninia soge amo lale fasi. Amalu amo soge, bu ninima hohonosu dunu amo iligili iasi dagoi.”
5 Nʼchifukwa chake simudzakhala ndi munthu mu msonkhano wa Yehova kuti agawe dziko pochita maere.
Amaiba: le, soge amo da bu Hina Gode Ea fidafa dunu ilima bu imunu esoha doaga: sea, dunu afae diliga da amo soge amoga afae hame lamu.
6 Aneneri awo amanena kuti, “Usanenere! Usanenere ndi pangʼono pomwe zimenezi; ife sitidzachititsidwa manyazi.”
Dunu ilia da nama olelelala, agoane sia: sa, “Ninima mae olelema! Amo huluane mae olelema! Gode da nini gogosiama: ne hame hamomu!
7 Inu nyumba ya Yakobo, monga zimenezi ndi zoyenera kuzinena: “Kodi Mzimu wa Yehova wakwiya? Kodi Iye amachita zinthu zotere?” “Kodi mawu ake sabweretsa zabwino kwa amene amayenda molungama?
Dilia dawa: lobada, Isala: ili fi dunu da aligima: ne gagabui amoha esalabala? Hina Gode Ea asaboi hou amo da yolebela: ? E da dafawane amo se iasu liligi hahamoma: bela: ? E da moloidafa hamobe dunu ilima asigili hame sia: nanabela: ?”
8 Posachedwapa anthu anga andiwukira ngati mdani. Mumawavula mkanjo wamtengowapatali anthu amene amadutsa mosaopa kanthu, monga anthu amene akubwera ku nkhondo.
Hina Gode da dabe sia: sa, “Dilia da Na dunuma ha lai agoane doagala: sa! Dunu ilia da gegenanu ili diasuga buhagibiba: le ilia da gaga: i dagoi amane dadawa: dudala, be amoga dilia da ilia anegagi abula amo ilia baligidu wamolamusa: oulelefula.
9 Mumatulutsa akazi a anthu anga mʼnyumba zawo zabwino. Mumalanda ana awo madalitso anga kosatha.
Dilia da na fi dunu ilia uda amo huluane ili hanai soge amoga esalu, amo oule sese ahoa, amola dilia da Na eso huluane hahawane fidisu hou amo Na da ilia manoma hamoi, amo lale fasi dagoi.
10 Nyamukani, chokani! Pakuti ano si malo anu opumulirapo, chifukwa ayipitsidwa, awonongedwa, sangatheke kuwakonzanso.
Wa: legadole masa! Goeguda: da gaga: su hamedafa gala! Dilia da wadela: le hamobeba: le, Na da amo soge gugunufinisimusa: ilegei dagoi!
11 Ngati munthu wabodza ndi wachinyengo abwera nʼkunena kuti, ‘Ine ndidzanenera ndipo mudzakhala ndi vinyo ndi mowa wambiri, woteroyo adzakhala mneneri amene anthu awa angamukonde!’
Amo dunu ilia da ogogole olelesu balofede dunu hanai gala. Agoai balofede da agoane ba: lala, “Na ba: laloba amo waini hano da dilia moma: ne, hano agoane ai masunu.
12 “Inu banja la Yakobo, ndidzakusonkhanitsani nonse; ndidzawasonkhanitsa pamodzi otsala a ku Israeli. Ndidzawabweretsa pamodzi ngati nkhosa mʼkhola, ngati ziweto pa msipu wake; malowo adzadzaza ndi chinamtindi cha anthu.
Be Na fi dunu! Na da dili Isala: ili hame bogoi esalebe dunu amo dili gilisilisimu. Sibi da ilia gagoiga buhagibi, amo defele Na da dili gagadole, dilia sogega bu oule masunu. Sibi da gisi noga: i sogebi amogai gilisibi defele, dilia soge da dunu bagohamedafa amoga nabai ba: mu.”
13 Amene adzawapulumutse adzayenda patsogolo pawo; iwo adzathyola chipata ndipo adzatuluka. Mfumu yawo idzawatsogolera, Yehova adzakhala patsogolo pawo.”
Gode da Ea fidafa ilia buhagima: ne logo doasimu. Ilia mugululi asi amo fisili, Gode Hi da ilima bisili gadili oule masunu. Ilia da moilai logo holei fili asili, hahawane udigili masunu. Ilia Hina Bagade, Hina Gode Hisu, da ili bisili gadili oule masunu.

< Mika 2 >