< Mika 1 >
1 Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
Słowo PANA, które doszło do Micheasza z Moreszet za dni Jotama, Achaza [i] Ezechiasza, królów Judy – to, co widział o Samarii i Jerozolimie.
2 Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
Słuchajcie, wszystkie narody; słuchaj, ziemio, i wszystko, co na niej jest. A niech Pan BÓG będzie świadkiem przeciwko wam, Pan ze swego świętego przybytku.
3 Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
Oto bowiem PAN wychodzi ze swojego miejsca, zstąpi i będzie deptać po wysokościach ziemi.
4 Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
I stopnieją pod nim góry, a doliny rozdzielą się tak, jak wosk przed ogniem [i] jak wody, które spływają po zboczu.
5 Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
To wszystko [się stanie] z powodu przestępstwa Jakuba i z powodu grzechów domu Izraela. Jakie jest przestępstwo Jakuba? Czy to nie Samaria? Co jest wyżyną Judy? Czy nie Jerozolima?
6 “Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
Dlatego zamienię Samarię w kupę gruzu na polu, w miejsce pod założenie winnicy. Powrzucam w dolinę jej kamienie i odkryję jej fundamenty.
7 Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
I wszystkie jej wyrzeźbione obrazy będą potłuczone, wszystkie jej dary spalone ogniem i wszystkie jej bożki zamienię w ruinę. [To] bowiem zgromadziła z zapłaty nierządnicy, to więc obróci się w zapłatę nierządnicy.
8 Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
Nad tym będę zawodzić i lamentować, chodząc nagi, bez ubrań. Podnoszę zawodzenie jak smoki i lament jak młode strusie;
9 Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
Jej rana bowiem [jest] nieuleczalna, gdyż doszła aż do Judy, [a] dotarła do bramy mego ludu aż do Jerozolimy.
10 Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
Nie opowiadajcie [tego] w Gat ani nie płaczcie. Tarzajcie się w prochu, w domu Afra.
11 Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
Przejdź [ty], która mieszkasz w Szafirze w haniebnej nagości. Ta, która mieszka w Saananie, nie wyszła na żałobę w Bet-Hezel; weźmie od was swoją żywność.
12 Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
Ta, która mieszka w Marot, oczekiwała dobra, ale zło zstąpiło od PANA aż do bramy Jerozolimy.
13 Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
Zaprzęgaj konie do rydwanu, mieszkanko Lakisz, która jesteś powodem grzechu córki Syjonu, gdyż w tobie znalezione są przestępstwa Izraela.
14 Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
Dlatego poślesz dary do Moreszet-Gat. Domy Akzibu [będą] ułudą dla królów Izraela.
15 Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
Jeszcze przyprowadzę ci dziedzica, mieszkanko Mareszy. Przyjdzie [aż] do Adullam, do chwały Izraela.
16 Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.
Ogol się i ostrzyż z powodu swoich ukochanych synów; rozszerz swą łysinę jak orzeł, bo poszli od ciebie do niewoli.