< Mika 1 >

1 Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.
La parole de l'Éternel, qui fut adressée à Michée, de Morésheth, aux jours de Jotham, d'Achaz, d'Ézéchias, rois de Juda, et qui lui fut révélée touchant Samarie et Jérusalem.
2 Tamverani, inu anthu a mitundu yonse, mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo, pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani, Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.
Écoutez, vous tous, peuples! Sois attentive, ô terre, avec tout ce qui est en toi! Que le Seigneur, l'Éternel, soit témoin contre vous, le Seigneur, du palais de sa sainteté!
3 Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake; Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.
Car voici, l'Éternel sort de sa demeure; il descend, et marche sur les lieux élevés de la terre.
4 Mapiri akusungunuka pansi pake, ndipo zigwa zikugawikana ngati phula pa moto, ngati madzi ochokera mʼphiri.
Les montagnes se fondent sous lui, les vallées s'entrouvrent, comme la cire devant le feu, comme des eaux qui coulent sur une pente.
5 Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo, chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli. Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani? Kodi si Samariya? Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati? Kodi si Yerusalemu?
Tout cela arrivera à cause du crime de Jacob, à cause des péchés de la maison d'Israël. - Quel est le crime de Jacob? N'est-ce pas Samarie? Quels sont les hauts lieux de Juda? N'est-ce pas Jérusalem?
6 “Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja, malo odzalamo mphesa. Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa ndipo ndidzafukula maziko ake.
Je ferai de Samarie un monceau de pierres dans les champs, un lieu où l'on plante la vigne. Je ferai rouler ses pierres dans la vallée, et je mettrai à nu ses fondements.
7 Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
Toutes ses images taillées seront brisées, et tous les salaires de sa prostitution seront brûlés au feu, et je mettrai en désolation toutes ses idoles; car elle les a rassemblées avec le salaire de la prostitution: elles retourneront aussi au salaire de prostitution.
8 Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni; ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche. Ndidzafuwula ngati nkhandwe ndi kulira ngati kadzidzi.
C'est pourquoi je mènerai deuil, et je me lamenterai; j'irai dépouillé et nu; je ferai une lamentation comme les chacals, et un cri de deuil comme les autruches.
9 Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika; chafika ku Yuda. Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga, mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.
Car sa plaie est incurable; elle s'étend jusqu'à Juda, elle atteint jusqu'à la porte de mon peuple, jusqu'à Jérusalem.
10 Musanene zimenezi ku Gati; musalire nʼkomwe. Mugubuduzike mu fumbi ku Beti-Leafura.
Ne l'annoncez point dans Gath! Ne pleurez point! A Beth-Léaphra je me roule dans la poussière.
11 Inu anthu okhala ku Safiro, muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi. Iwo amene akukhala ku Zanaani sadzatuluka. Beti-Ezeli akulira mwachisoni; chitetezo chake chakuchokerani.
Passe, habitante de Shaphir, dans la nudité et la honte! L'habitante de Tsaanan n'ose sortir. Le deuil de Beth-Haetsel vous prive de son soutien.
12 Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu, akuyembekezera thandizo, chifukwa Yehova wabweretsa tsoka, lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.
Car l'habitante de Maroth est dans l'angoisse à cause de son bien; parce que le mal descend de la part de l'Éternel jusqu'à la porte de Jérusalem.
13 Inu anthu okhala ku Lakisi mangani akavalo ku magaleta. Inu amene munayamba kuchimwitsa mwana wamkazi wa Ziyoni, pakuti zolakwa za Israeli zinapezeka pakati panu.
Attelle les coursiers au char, habitante de Lakis! Tu as été le commencement du péché pour la fille de Sion; car en toi ont été trouvés les crimes d'Israël.
14 Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana ndi a ku Moreseti Gati. Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama kwa mafumu a Israeli.
C'est pourquoi tu dois renoncer à Morésheth-Gath; les maisons d'Aczib seront une déception pour les rois d'Israël.
15 Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.
Je t'amènerai un autre possesseur de tes biens, habitante de Marésha! La gloire d'Israël s'en ira jusqu'à Adullam.
16 Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira ana anu amene mumawakonda; mudzichititse dazi ngati dembo, pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.
Rends-toi chauve et rase-toi, à cause de tes enfants chéris; rends-toi chauve comme le vautour, car ils s'en vont en captivité loin de toi!

< Mika 1 >