< Mateyu 9 >

1 Yesu analowa mʼbwato nawoloka, ndipo anabwera ku mudzi wa kwawo.
ישוע חזר לסירה, חצה את האגם ושב לכפר־נחום עיר מגוריו.
2 Amuna ena anabwera ndi munthu wakufa ziwalo kwa Iye atamugoneka pa mphasa. Yesu ataona chikhulupiriro chawo anati kwa wakufa ziwaloyo, “Limba mtima mwana wanga, machimo ako akhululukidwa.”
מספר אנשים הביאו אליו בחור משותק על אלונקה. כשראה ישוע את אמונתם, אמר לבחור:”התעודד, בני, כי נסלחו לך חטאיך!“
3 Pamenepo aphunzitsi ena amalamulo anaganiza mu mtima mwawo kuti, “Munthu uyu akuchitira Mulungu mwano.”
”איש זה מגדף!“אמרו בלבם מספר סופרים. (כי מי מלבד אלוהים יכול לסלוח על חטאים?)
4 Ndipo podziwa maganizo awo Yesu anati, “Bwanji mukuganiza zoyipa mʼmitima mwanu?
ישוע ידע את מחשבותיהם, ולכן שאל אותם:”מדוע אתם חושבים מחשבות רעות?
5 Chapafupi ndi chiti kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa’ kapena kunena kuti, ‘Imirira ndipo yenda?’
לבן האדם, יש סמכות לסלוח על חטאים, אך מכיוון שכל אחד יכול לומר דברים סתם, אז אפגין לכם את סמכותי.“הוא פנה אל הנער המשותק ואמר לו”קום! קפל את האלונקה שלך ולך הביתה!“
6 Tsono kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko wokhululuka machimo, pamenepo anati kwa wakufa ziwaloyo, ‘Imirira, tenga mphasa yako kazipita kwanu.’”
7 Ndipo munthuyo anayimirira napita kwawo.
הבחור קפץ על רגליו לנגד עיניהם, והלך לביתו.
8 Gulu la anthu litaona izi, linadzazidwa ndi mantha ndipo linalemekeza Mulungu amene anapereka ulamuliro kwa anthu.
פחד אחז את הנוכחים, והם הודו לה׳ ושיבחו אותו על שנתן כוח כזה לבני־אדם.
9 Ndipo Yesu atachoka kumeneko, anaona munthu wina dzina lake Mateyu, atakhala mʼnyumba ya msonkho. Anati kwa iye, “Nditsate Ine.” Ndipo iye ananyamuka namutsata.
כשישוע הלך משם הוא ראה בבית־המכס את גובה המכס, מתתיהו.”בוא והיה תלמיד שלי“, אמר לו ישוע. מתתיהו קם, עזב את הכול מאחוריו והלך אחרי ישוע.
10 Ndipo pamene Iye ankadya mʼnyumba, onani, amisonkho ndi ochimwa ambiri anabwera nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake.
בערב כשאכלו ישוע ותלמידיו בביתו של מתתיהו, הצטרפו אליהם מוכסים וחוטאים אחרים.
11 Ndipo Afarisi poona izi, anati kwa ophunzira ake, “Nʼchifukwa chiyani Aphunzitsi anu akudya pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”
הפרושים כעסו מאוד ואמרו לתלמידיו:”מדוע הרב שלכם אוכל בחברת החוטאים האלה?“
12 Yesu atamva, anati, “Munthu wamoyo safuna singʼanga ayi, koma wodwala.
ישוע השיב להם:”אנשים בריאים אינם זקוקים לרופא; אלא שהחולים זקוקים לרופא!“השיב להם ישוע,
13 Koma pitani kaphunzireni tanthauzo la mawu awa: ‘Ndimafuna chifundo osati nsembe ayi.’ Pakuti sindinabwere kudzayitana olungama koma ochimwa.”
והוסיף:”עתה לכו ולימדו את משמעות הפסוק:’כי חסד חפצתי ולא‎ זֶבַח‘. לא באתי לקרוא לצדיקים לחזור בתשובה, כי אם לחוטאים.“
14 Ndipo ophunzira a Yohane anabwera namufunsa Iye kuti, “Bwanji ife ndi Afarisi timasala kudya koma ophunzira anu sasala kudya?”
יום אחד באו תלמידי יוחנן אל ישוע ושאלו:”מדוע תלמידיך אינם צמים כמונו וכמו הפרושים?“
15 Yesu anayankha kuti, “Kodi oyitanidwa ku ukwati angamalire bwanji pamene mkwati ali naye pamodzi? Nthawi idzafika pamene mkwatiyo adzachotsedwa ndi pamene adzasala kudya.”
”האם יכולים ידידי החתן להתאבל ולצום בזמן שהוא נמצא אתם?“השיב להם ישוע בשאלה.”אולם יבוא יום שהחתן יילקח מהם, ואז הם יצומו.“
16 Ndipo palibe munthu amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale chifukwa chigambacho chidzachoka ndipo chibowocho chidzakula kuposa kale.
”מי תופר טלאי מבד חדש על בגד ישן? הרי הטלאי מהבגד החדש יינתק ויגדיל את החור בבגד!
17 Kapena sathira vinyo watsopano mʼmatumba akale; akatero, matumba akalewo adzaphulika ndipo vinyoyo adzatayika, matumbawo adzawonongeka; satero ayi. Amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso ndipo zonse zimasungika.
ומי ממלא יין חדש בחביות רקובות? הרי היין יבקע את החביות ויישפך החוצה! יין חדש יש לשמור בחביות חדשות. כך יישמרו היין והחביות.“
18 Pamene ankanena zimenezi, mkulu wa sunagoge anabwera namugwadira Iye nati, “Mwana wanga wamkazi wamwalira posachedwapa koma tiyeni mukasanjike dzanja lanu pa iye ndipo adzakhala ndi moyo.”
בשעה שישוע דיבר בא אליו הרב של בית־הכנסת המקומי והשתחווה לפניו.”בתי הקטנה מתה ממש עכשיו, “אמר הרב,”אולם אתה תוכל להחיות אותה, אם רק תבוא ותיגע בה.“
19 Yesu ndi ophunzira ake ananyamuka napita naye pamodzi.
ישוע קם והלך אחרי הרב, ותלמידיו הצטרפו אליו.
20 Panali mayi wina amene ankadwala nthenda yotaya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri ndipo anadza mʼmbuyo mwake nakhudza mkanjo wake.
בקרב הקהל שהלך אחריהם הייתה אישה שסבלה משטף דם מתמיד במשך שתים־עשרה שנה. היא עמדה מאחורי ישוע ונגעה בקצה מעילו,
21 Iyeyo anati mwa iye yekha, “Nditangokhudza kasonga ka mkanjo wake, ine ndidzachiritsidwa.”
מפני שחשבה:”אם רק אגע בבגדו, ארפא!“
22 Ndipo Yesu anatembenuka namuona mayiyo nati, “Limbani mtima mayi iwe, chikhulupiriro chako chakuchiritsa.” Nthawi yomweyo mayiyo anachiritsidwa.
ישוע פנה לאחור ואמר לאישה:”התעודדי בתי, אמונתֵך ריפאה אותך.“ובאותו רגע היא נרפאה.
23 Yesu atalowa mʼnyumba ya mkulu wa sunagoge ndi kuona oyimba zitoliro ndi gulu la anthu ochita phokoso,
ישוע הגיע לבית הרב וראה את המתאבלים שבכו וקוננו קינות.
24 anati, “Tulukani, mtsikanayu sanafe koma ali mtulo.” Koma anamuseka Iye.
”לכו מכאן כולכם!“קרא ישוע.”הילדה לא מתה; היא רק ישנה!“אולם כולם צחקו לו.
25 Atangowatulutsa anthuwo, analowa mʼnyumba ndipo anagwira dzanja la mtsikanayo ndipo anauka.
ברגע שיצאו האנשים נכנס ישוע לחדר הילדה, אחז בידה, והיא קפצה ממיטתה בריאה לגמרי.
26 Mbiriyi inamveka mʼdera lonse.
השמועה על הנס הנפלא הזה התפשטה בכל האזור.
27 Yesu atapitirira ulendo wake, amuna awiri osaona anamutsatira Iye, akufuwula kuti, “Tichitireni chifundo, Mwana wa Davide!”
כשעזב ישוע את בית הרב, הלכו בעקבותיו שני עיוורים וצעקו:”בן דוד, רחם עלינו!“
28 Atalowa mʼnyumba, amuna awiri osaonawo anabwera kwa Iye ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukhulupirira kuti ndikhoza kukuchiritsani?” Iwo anayankha kuti, “Inde Ambuye.”
שני העיוורים נכנסו אל הבית שבו התארח ישוע, והוא שאל אותם:”האם אתם מאמינים שאני יכול להשיב לכם את ראייתכם?“”כן, אדון, “ענו השניים,”אנחנו מאמינים.“
29 Pomwepo anakhudza maso awo nati, “Zichitike kwa inu monga mwachikhulupiriro chanu.”
ישוע נגע בעיניהם ואמר:”משום שהאמנתם, תירפאו.“
30 Ndipo anayamba kuona. Yesu anawachenjeza kwambiri nati, “Onani, wina aliyense asadziwe za zimenezi.”
לפתע יכלו השניים לראות. ישוע הזהיר אותם שלא יספרו על כך לאיש,
31 Koma iwo anatuluka mʼnyumbamo nafalitsa za Iye mʼchigawo chonse.
אולם השניים לא שמעו בקולו ופרסמו את דבר הנס בכל הארץ.
32 Pamene iwo ankatuluka kunja, anthu anabwera kwa Iye ndi munthu wogwidwa ndi mzimu wosayankhula.
כשעזב ישוע את המקום הוא פגש אדם אילם שהיה אחוז שד.
33 Ndipo atatulutsa mzimuwo, munthuyo anayankhula. Gulu la anthuwo linadabwa ndipo linati, “Zinthu zotere sizinaonekepo mu Israeli.”
ישוע גירש את השד, והאיש החל לדבר. ההמונים נדהמו וקראו:”מעולם לא נראו דברים כאלה בישראל!“
34 Koma Afarisi anati, “Akutulutsa mizimu yoyipa ndi mphamvu ya mkulu wa ziwanda.”
אולם הפרושים אמרו:”אין פלא שהוא יכול לגרש שדים, הרי הוא מקבל את כוחו משר השדים!“
35 Yesu anayendayenda mʼmizinda yonse ndi mʼmidzi, kuphunzitsa mʼmasunagoge awo, nalalikira Uthenga Wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa nthenda zawo zonse ndi zofowoka za mʼmatupi mwawo.
ישוע עבר בכל הערים והכפרים שבאזור, כשהוא מלמד בבתי־הכנסת ומבשר את החדשות הטובות על מלכות השמים. בכל מקום שבו ישוע ביקר הוא ריפא את האנשים מכל מיני מחלות.
36 Ataona maguluwo, anagwidwa ndi chisoni chifukwa anali ozunzika ndi osowa chithandizo ngati nkhosa zopanda mʼbusa.
הוא ריחם על כל האנשים שלא ידעו מה לעשות ולאן לפנות. הם היו כמו כבשים תועות בלי רועה.
37 Pamenepo anati kwa ophunzira ake, “Zokolola ndi zambiri koma antchito ndi ochepa.
”הקציר כה רב אך הפועלים כה מעטים!“אמר ישוע לתלמידיו.
38 Nʼchifukwa chake, pemphani Ambuye mwini zokolola kuti atumize antchito ku munda wake.”
”התפללו ובקשו מהאחראי על הקציר שידריך ויכשיר לעבודה פועלים רבים יותר!“

< Mateyu 9 >