< Mateyu 8 >

1 Iye atatsika ku phiri kuja, anthu ambirimbiri anamutsata.
yadA sa parvvatAd avArohat tadA bahavo mAnavAstatpashchAd vavrajuH|
2 Ndipo munthu wakhate anadza kwa Yesu namugwadira nati, “Ambuye, ngati mufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
ekaH kuShThavAn Agatya taM praNamya babhAShe, he prabho, yadi bhavAn saMmanyate, tarhi mAM nirAmayaM karttuM shaknoti|
3 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” Nthawi yomweyo anachiritsidwa khate lake.
tato yIshuH karaM prasAryya tasyA NgaM spR^ishan vyAjahAra, sammanye. ahaM tvaM nirAmayo bhava; tena sa tatkShaNAt kuShThenAmochi|
4 Ndipo Yesu anati kwa iye, “Taona, usawuze wina aliyense. Koma upite kwa mkulu wa ansembe ukadzionetse wekha ndi kupereka mphatso imene Mose analamulira, kuti ukhale umboni kwa iwo.”
tato yIshustaM jagAda, avadhehi kathAmetAM kashchidapi mA brUhi, kintu yAjakasya sannidhiM gatvA svAtmAnaM darshaya manujebhyo nijanirAmayatvaM pramANayituM mUsAnirUpitaM dravyam utsR^ija cha|
5 Yesu atalowa mʼKaperenamu, Kenturiyo anabwera kwa Iye napempha chithandizo,
tadanantaraM yIshunA kapharnAhUmnAmani nagare praviShTe kashchit shatasenApatistatsamIpam Agatya vinIya babhAShe,
6 nati, “Ambuye, wantchito wanga ali chigonere ku nyumba, sakuthanso kuyenda, akumva kuwawa kwambiri.”
he prabho, madIya eko dAsaH pakShAghAtavyAdhinA bhR^ishaM vyathitaH, satu shayanIya Aste|
7 Ndipo Yesu anati kwa iye, “Ine ndibwera kudzamuchiritsa.”
tadAnIM yIshustasmai kathitavAn, ahaM gatvA taM nirAmayaM kariShyAmi|
8 Kenturiyo uja anayankha kuti, “Ambuye, ndine wosayenera kuti Inu mukalowe mʼnyumba mwanga. Koma mungonena mawu ndipo wantchito wanga adzachiritsidwa.
tataH sa shatasenApatiH pratyavadat, he prabho, bhavAn yat mama gehamadhyaM yAti tadyogyabhAjanaM nAhamasmi; vA NmAtram Adishatu, tenaiva mama dAso nirAmayo bhaviShyati|
9 Pakuti inenso ndili pansi pa ulamuliro ndipo ndili ndi asilikali amene ndiwalamulira. Ndikalamulira mmodzi kuti, ‘Pita,’ amapita; ndi kwa wina kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikawuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ iye amachita.”
yato mayi paranidhne. api mama nideshavashyAH kati kati senAH santi, tata ekasmin yAhItyukte sa yAti, tadanyasmin ehItyukte sa AyAti, tathA mama nijadAse karmmaitat kurvvityukte sa tat karoti|
10 Yesu atamva zimenezi, anadabwa ndipo anati kwa omutsatira, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti sindinapeze wina aliyense mu Israeli wachikhulupiriro chachikulu chotere.
tadAnIM yIshustasyaitat vacho nishamya vismayApanno. abhUt; nijapashchAdgAmino mAnavAn avochcha, yuShmAn tathyaM vachmi, isrAyelIyalokAnAM madhye. api naitAdR^isho vishvAso mayA prAptaH|
11 Ndikuwuzani kuti ambiri adzabwera kuchokera kummawa ndi kumadzulo, nadzakhala nawo pa phwando pamodzi ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo mu ufumu wakumwamba.
anyachchAhaM yuShmAn vadAmi, bahavaH pUrvvasyAH pashchimAyAshcha disha Agatya ibrAhImA ishAkA yAkUbA cha sAkam militvA samupavekShyanti;
12 Koma eni ake ufumuwo adzaponyedwa ku mdima wakunja kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
kintu yatra sthAne rodanadantagharShaNe bhavatastasmin bahirbhUtatamisre rAjyasya santAnA nikShesyante|
13 Pamenepo Yesu anati kwa Kenturiyo, “Pita! Zichitike monga momwe wakhulupirira.” Ndipo wantchito wake anachira pa nthawi yomweyo.
tataH paraM yIshustaM shatasenApatiM jagAda, yAhi, tava pratItyanusArato ma NgalaM bhUyAt; tadA tasminneva daNDe tadIyadAso nirAmayo babhUva|
14 Ndipo Yesu atalowa mʼnyumba ya Petro, anaona mpongozi wake wa Petro ali gone akudwala malungo.
anantaraM yIshuH pitarasya gehamupasthAya jvareNa pIDitAM shayanIyasthitAM tasya shvashrUM vIkShA nchakre|
15 Ndipo Yesu anakhudza dzanja lake ndipo pomwepo anachira nayamba kumutumikira.
tatastena tasyAH karasya spR^iShTatavAt jvarastAM tatyAja, tadA sA samutthAya tAn siSheve|
16 Itafika nthawi yamadzulo, anthu anabweretsa kwa Iye anthu ambiri ogwidwa ndi ziwanda ndipo anatulutsa ziwandazo ndi mawu okha, nachiritsa odwala onse.
anantaraM sandhyAyAM satyAM bahusho bhUtagrastamanujAn tasya samIpam AninyuH sa cha vAkyena bhUtAn tyAjayAmAsa, sarvvaprakArapIDitajanAMshcha nirAmayAn chakAra;
17 Uku kunali kukwaniritsa zimene ananena mneneri Yesaya kuti, “Iye anatenga zofowoka zathu, nanyamula nthenda zathu.”
tasmAt, sarvvA durbbalatAsmAkaM tenaiva paridhAritA| asmAkaM sakalaM vyAdhiM saeva saMgR^ihItavAn| yadetadvachanaM yishayiyabhaviShyadvAdinoktamAsIt, tattadA saphalamabhavat|
18 Yesu ataona gulu la anthu litamuzungulira, analamula kuti awolokere kutsidya lina la nyanja.
anantaraM yIshushchaturdikShu jananivahaM vilokya taTinyAH pAraM yAtuM shiShyAn Adidesha|
19 Ndipo mphunzitsi wa malamulo anabwera kwa Iye nati, “Aphunzitsi, ine ndidzakutsatani kulikonse kumene muzipita.”
tadAnIm eka upAdhyAya Agatya kathitavAn, he guro, bhavAn yatra yAsyati tatrAhamapi bhavataH pashchAd yAsyAmi|
20 Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ndi mbalame zamlengalenga zili ndi zisa, koma Mwana wa Munthu alibe malo ogona ngakhale potsamira mutu wake.”
tato yIshu rjagAda, kroShTuH sthAtuM sthAnaM vidyate, vihAyaso viha NgamAnAM nIDAni cha santi; kintu manuShyaputrasya shiraH sthApayituM sthAnaM na vidyate|
21 Wophunzira wina anati kwa Iye, “Ambuye, mundilole ndiyambe ndakayika maliro a abambo anga.”
anantaram apara ekaH shiShyastaM babhAShe, he prabho, prathamato mama pitaraM shmashAne nidhAtuM gamanArthaM mAm anumanyasva|
22 Koma Yesu anamuwuza kuti, “Nditsate Ine ndipo uwaleke akufa ayikane akufa okhaokha.”
tato yIshuruktavAn mR^itA mR^itAn shmashAne nidadhatu, tvaM mama pashchAd AgachCha|
23 Iye atalowa mʼbwato, ophunzira ake anamutsatira.
anantaraM tasmin nAvamArUDhe tasya shiShyAstatpashchAt jagmuH|
24 Ndipo taonani mwadzidzidzi mphepo yayikulu yamkuntho inawomba pa nyanjapo, kotero kuti bwatolo linayamba kumizidwa ndi mafunde. Koma Yesu anali mtulo.
pashchAt sAgarasya madhyaM teShu gateShu tAdR^ishaH prabalo jha nbhshanila udatiShThat, yena mahAtara Nga utthAya taraNiM ChAditavAn, kintu sa nidrita AsIt|
25 Ophunzira ake anapita namudzutsa nati, “Ambuye! Tipulumutseni! Tikumira!”
tadA shiShyA Agatya tasya nidrAbha NgaM kR^itvA kathayAmAsuH, he prabho, vayaM mriyAmahe, bhavAn asmAkaM prANAn rakShatu|
26 Iye anawayankha kuti, “Inu achikhulupiriro chochepa, chifukwa chiyani mukuchita mantha?” Ndipo anayimirira nadzudzula mphepoyo ndi mafunde ndipo panali bata lalikulu.
tadA sa tAn uktavAn, he alpavishvAsino yUyaM kuto vibhItha? tataH sa utthAya vAtaM sAgara ncha tarjayAmAsa, tato nirvvAtamabhavat|
27 Ndipo ophunzirawo anadabwa nafunsa kuti, “Ndi munthu wotani uyu? Kuti ngakhale mphepo ndi mafunde zimvera Iye!”
aparaM manujA vismayaM vilokya kathayAmAsuH, aho vAtasaritpatI asya kimAj nAgrAhiNau? kIdR^isho. ayaM mAnavaH|
28 Ndipo atafika ku mbali ina ya dera la Gadara, anakumana ndi anthu awiri ogwidwa ndi ziwanda akuchokera ku manda. Iwowa anali woopsa kwambiri kotero kuti panalibe munthu akanatha kudzera njira imeneyo.
anantaraM sa pAraM gatvA giderIyadesham upasthitavAn; tadA dvau bhUtagrastamanujau shmashAnasthAnAd bahi rbhUtvA taM sAkShAt kR^itavantau, tAvetAdR^ishau prachaNDAvAstAM yat tena sthAnena kopi yAtuM nAshaknot|
29 Ndipo iwo anafuwulira kwa Yesu nati, “Mukufuna chiyani kwa ife, Inu Mwana wa Mulungu? Kodi mwabwera kuno kudzatizunza nthawi yake isanafike?”
tAvuchaiH kathayAmAsatuH, he Ishvarasya sUno yIsho, tvayA sAkam AvayoH kaH sambandhaH? nirUpitakAlAt prAgeva kimAvAbhyAM yAtanAM dAtum atrAgatosi?
30 Ndipo patali pake panali gulu la nkhumba zimene zimadya.
tadAnIM tAbhyAM ki nchid dUre varAhANAm eko mahAvrajo. acharat|
31 Ndipo ziwandazo zinamupempha Yesu kuti, “Ngati mutitulutsa ife mutitumize mu nkhumba izo.”
tato bhUtau tau tasyAntike vinIya kathayAmAsatuH, yadyAvAM tyAjayasi, tarhi varAhANAM madhyevrajam AvAM preraya|
32 Iye anati kwa ziwandazo, “Pitani!” Ndipo pamenepo zinatuluka ndi kukalowa mʼnkhumbazo ndipo nkhumba zonse zinathamangira mʼnyanja ndi kufera momwemo.
tadA yIshuravadat yAtaM, anantaraM tau yadA manujau vihAya varAhAn Ashritavantau, tadA te sarvve varAhA uchchasthAnAt mahAjavena dhAvantaH sAgarIyatoye majjanto mamruH|
33 Koma amene amaziweta anathawa nalowa mʼmudzi nafotokoza zonse, kuphatikizapo zimene zinachitika ndi anthu ogwidwa ndi ziwanda aja.
tato varAharakShakAH palAyamAnA madhyenagaraM tau bhUtagrastau prati yadyad aghaTata, tAH sarvvavArttA avadan|
34 Ndipo anthu onse a mʼmudziwo anatuluka kukakumana ndi Yesu. Ndipo atamuona Iye, anamupempha kuti achoke mʼdera lawo.
tato nAgarikAH sarvve manujA yIshuM sAkShAt karttuM bahirAyAtAH ta ncha vilokya prArthayA nchakrire bhavAn asmAkaM sImAto yAtu|

< Mateyu 8 >