< Mateyu 8 >

1 Iye atatsika ku phiri kuja, anthu ambirimbiri anamutsata.
Bhwakati Yesu aselili pasi kuh'oma pa kid'onda, bhumati m'mbaha bhwamfwatili.
2 Ndipo munthu wakhate anadza kwa Yesu namugwadira nati, “Ambuye, ngati mufuna, mukhoza kundiyeretsa.”
Langai, mkoma ahidili ni kusujudu m'b'ele j'ha muene, akajobha, “Bwana, ikaj'hiaghe ujhe tayari ghwibhwesya kunibhomba nj'hiaghe kinofu”.
3 Yesu anatambasula dzanja lake namukhudza munthuyo nati, “Ndikufuna, yeretsedwa!” Nthawi yomweyo anachiritsidwa khate lake.
Yesu anyosisi kibhoko kya muene ni kun'gusa, akajobha, “Nj'hela tayari. Uj'hiaghe n'safi.” Bahuapu atakasibhu bhukhoma bhuake.
4 Ndipo Yesu anati kwa iye, “Taona, usawuze wina aliyense. Koma upite kwa mkulu wa ansembe ukadzionetse wekha ndi kupereka mphatso imene Mose analamulira, kuti ukhale umboni kwa iwo.”
Yesu an'jobhili, “Langai kwamba usijobhi kwa munu j'hej'hioha. Kamulai nj'hela j'ha bhebhe, na ghwilasiaghe ghwimuene kwa kuhani na uh'omesiaghe zawadi ambayo Musa alaghisi, kwa ndabha j'ha bhushuhuda bhuakhu”
5 Yesu atalowa mʼKaperenamu, Kenturiyo anabwera kwa Iye napempha chithandizo,
Bhwakati Yesu afikiri Kapernaumu, Jemedari akahida kwa muene akan'kota
6 nati, “Ambuye, wantchito wanga ali chigonere ku nyumba, sakuthanso kuyenda, akumva kuwawa kwambiri.”
akajobha, “Bwana, n'tumishi ghuangu agonili kunyumba apoozili na ajhele ni maumivu gha kutisya.” Yesu akan'jobhela,
7 Ndipo Yesu anati kwa iye, “Ine ndibwera kudzamuchiritsa.”
“Nibetakuhida ni kumponesya”.
8 Kenturiyo uja anayankha kuti, “Ambuye, ndine wosayenera kuti Inu mukalowe mʼnyumba mwanga. Koma mungonena mawu ndipo wantchito wanga adzachiritsidwa.
Jemedari ajibili ni kun'jobhela, “Bwana, nene ghwa thamani lepi hata uhidai ni kuj'hingila mugati mu dari j'ha nene, jobhai lilobhi tu ni n'tumishi ghwangu ibetakupona.
9 Pakuti inenso ndili pansi pa ulamuliro ndipo ndili ndi asilikali amene ndiwalamulira. Ndikalamulira mmodzi kuti, ‘Pita,’ amapita; ndi kwa wina kuti, ‘Bwera,’ amabwera. Ndikawuza wantchito wanga kuti, ‘Chita ichi,’ iye amachita.”
Kwa kujha nene pia ndo munu j'haniyele ni mamlaka, na njele ni askari bhabhajhele pasi pa nene. Nikajobhai kwa oj'ho “Lotai' na ilota, na kwa j'hongi 'Hidajhi' na ihida, ni kwa n'tumishi bhwangu, 'Bhombaghe naha,' nu muene ibhomba naha”
10 Yesu atamva zimenezi, anadabwa ndipo anati kwa omutsatira, “Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti sindinapeze wina aliyense mu Israeli wachikhulupiriro chachikulu chotere.
Bhwakati Yesu ap'heliki aghu asyangele ni kubhajobhela bhala ambabho bhamfuateghe, “Bhukweli nikabhajobhela. Nibhwajhili lepi kubhona munu mwenye imani kama oj'ho mu Israeli.
11 Ndikuwuzani kuti ambiri adzabwera kuchokera kummawa ndi kumadzulo, nadzakhala nawo pa phwando pamodzi ndi Abrahamu, Isake ndi Yakobo mu ufumu wakumwamba.
Nikabhajobhela, bhingi bhibetakuhida kuh'omela mashariki ni magharibi, bhibetakutama mu meza pamonga ni Abrahamu, Isaka, ni Yakobo mu bhufalme bhwa mbinguni.
12 Koma eni ake ufumuwo adzaponyedwa ku mdima wakunja kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
Lakini bhana bha ufalme bhibeta kutaghibhwa mu ngisi lya kubhala, ambapo kwibekujha ni khilelu ni kusiagha minu.”
13 Pamenepo Yesu anati kwa Kenturiyo, “Pita! Zichitike monga momwe wakhulupirira.” Ndipo wantchito wake anachira pa nthawi yomweyo.
Yesu akabhajobhela Jemedari, “Lotaghe! Kama kyaumalili kukiera, na j'hibhombekaghe naha kwa bhebhe.” Ni n'tumishi aponyisibhu mu lisaa lelue'lu.
14 Ndipo Yesu atalowa mʼnyumba ya Petro, anaona mpongozi wake wa Petro ali gone akudwala malungo.
Bhwakati Yesu afikiri pa nyuma j'ha Petro, ambwene nkwibhi ghwa Petro agonili akaj'ha n'tamu ghwa homa.
15 Ndipo Yesu anakhudza dzanja lake ndipo pomwepo anachira nayamba kumutumikira.
Yesu ankamuili kibhoko kya muene, ni homa j'ha muene j'hikan'ndeka. Kisha akaj'humuka akaj'handa kun'hudumila
16 Itafika nthawi yamadzulo, anthu anabweretsa kwa Iye anthu ambiri ogwidwa ndi ziwanda ndipo anatulutsa ziwandazo ndi mawu okha, nachiritsa odwala onse.
Na bhoj'hifikiri kimihi, bhanu bhakandetela Yesu bhingi bhabhatawalibhu ni pepo. Akabh'enga mapepo ni bhala bhabhaj'he bhabhine abhaponisi.
17 Uku kunali kukwaniritsa zimene ananena mneneri Yesaya kuti, “Iye anatenga zofowoka zathu, nanyamula nthenda zathu.”
Kwa jinsi ej'he ghatimili ghala ghaghamali kujobhibhwa ni Isaya nabii, “Muene atolili bhubhine bhwetu na ap'hendili maradhi ghitu”
18 Yesu ataona gulu la anthu litamuzungulira, analamula kuti awolokere kutsidya lina la nyanja.
Kisha Yesu bho alibhwene likusanyiku lya bhanu lin'syonguikhi, apisili maelekezo gha kulota lubhafu longi mwa Bahari j'ha Galilaya.
19 Ndipo mphunzitsi wa malamulo anabwera kwa Iye nati, “Aphunzitsi, ine ndidzakutsatani kulikonse kumene muzipita.”
Kisha mwandishi ahidili kwa muene ni kun'jobhela, “Mwalimu, nibetakufuata popoa pala paghwibeta kul'ota.”
20 Yesu anayankha kuti, “Nkhandwe zili ndi mapanga ndi mbalame zamlengalenga zili ndi zisa, koma Mwana wa Munthu alibe malo ogona ngakhale potsamira mutu wake.”
Yesu an'jhobhili, “Mbweha bhana mal'ende ni fidege fya angani bhaj'he ni fiota, lakini mwana ghwa Adamu aj'helepi ni sehemu j'ha kugoneka mutu bhwakhe.”
21 Wophunzira wina anati kwa Iye, “Ambuye, mundilole ndiyambe ndakayika maliro a abambo anga.”
Mwanafunzi j'hongi an'jobhili, “Bwana, niruhusiaghe oti nilotaghe kun'siela tata ghwangu.”
22 Koma Yesu anamuwuza kuti, “Nditsate Ine ndipo uwaleke akufa ayikane akufa okhaokha.”
Lakini Yesu an'jobhili, “Un'kesiaghe, na ubhalekai bhafu bhasyelayi bhafu bha j'hinu.”
23 Iye atalowa mʼbwato, ophunzira ake anamutsatira.
Yesu bho aj'hingili mu bhuatu, bhanafunzi bhakankesya mu bhuatu.
24 Ndipo taonani mwadzidzidzi mphepo yayikulu yamkuntho inawomba pa nyanjapo, kotero kuti bwatolo linayamba kumizidwa ndi mafunde. Koma Yesu anali mtulo.
Langai, lyaj'handili linyegha libhaa panani pa bahari, kiasi kwamba bhuatu bhwafunikibhu ni manyegha. Lakini Yesu agonili lugono.
25 Ophunzira ake anapita namudzutsa nati, “Ambuye! Tipulumutseni! Tikumira!”
Bhanafunzi bhakahida kwa muene ni kunjumusya bhakaj'ha bhijobha, “Bwana, tuokolayi tete, twilota kufwa!”
26 Iye anawayankha kuti, “Inu achikhulupiriro chochepa, chifukwa chiyani mukuchita mantha?” Ndipo anayimirira nadzudzula mphepoyo ndi mafunde ndipo panali bata lalikulu.
Yesu akabhajobhela, kwa ndabha j'ha kiki mwitila, muenga j'ha muj'he ni imani idusu?” Ndipo akaj'humuka ni kubhubesya mp'ongo ni bahari. Kisha kukabhwa ni bhutulivu m'mbaha,
27 Ndipo ophunzirawo anadabwa nafunsa kuti, “Ndi munthu wotani uyu? Kuti ngakhale mphepo ndi mafunde zimvera Iye!”
bhagosi bhakamuliki ni mshangao m'baha bhakajobha, “Oj'ho ghwa namna gani, kwamba hata mp'ongo ni bahari figudeme kwa muene?”
28 Ndipo atafika ku mbali ina ya dera la Gadara, anakumana ndi anthu awiri ogwidwa ndi ziwanda akuchokera ku manda. Iwowa anali woopsa kwambiri kotero kuti panalibe munthu akanatha kudzera njira imeneyo.
Bhwakati Yesu ahidili lubhafu longilwa nchi j'ha Magadala, bhagosi bhabhele bha bhatawalibhu ni pepo bhabhonene naku. Bhakaj'ha bhihomela kumakaburi na bhakaj'ha bhibhomba vurugu sana, kiasi kwamba aj'he lepi msafiri ghwa kubhwesya kup'heta nj'hela j'hela.
29 Ndipo iwo anafuwulira kwa Yesu nati, “Mukufuna chiyani kwa ife, Inu Mwana wa Mulungu? Kodi mwabwera kuno kudzatizunza nthawi yake isanafike?”
Langaghe, bhakwesili sauti ni kujobha, “Tuj'he ni kiki kya kubhomba kwa bhebhe, mwana ghwa K'yara? Uhidili apa kututesya kabla j'ha bhwakati kufika?”
30 Ndipo patali pake panali gulu la nkhumba zimene zimadya.
Henu likundi libhaha lya maghorobhi aj'hele likidima, paj'helelepi patali ni pabhaj'hele,
31 Ndipo ziwandazo zinamupempha Yesu kuti, “Ngati mutitulutsa ife mutitumize mu nkhumba izo.”
pepo bhaj'handelili kulalamika kwa Yesu ni kujobha, “Ikaj'hiaghe wibetakutuamuru kubhoka, tulongosiaghe mu likundi lya maghorobhi.”
32 Iye anati kwa ziwandazo, “Pitani!” Ndipo pamenepo zinatuluka ndi kukalowa mʼnkhumbazo ndipo nkhumba zonse zinathamangira mʼnyanja ndi kufera momwemo.
Yesu akabhajobhela, “Mlotaghe!” Pepo bhakabhoka ni kubanga kwa maghorobhi. Na langaghe, likundi lyoha lyaselili kuhomela kukid'onda kuserelela ku bahari na lyoha lyafwelili mu masi.
33 Koma amene amaziweta anathawa nalowa mʼmudzi nafotokoza zonse, kuphatikizapo zimene zinachitika ndi anthu ogwidwa ndi ziwanda aja.
Bhagosi bhabhaj'hele bhidima maghorobhi bhajumbili. Na bho bhalotili kumjini bhakaj'helesya khila khenu, hususani kyakyatokili kwa bhagosi bhabhatawalibhu ni mapepo.
34 Ndipo anthu onse a mʼmudziwo anatuluka kukakumana ndi Yesu. Ndipo atamuona Iye, anamupempha kuti achoke mʼdera lawo.
Langaghe, mji bhuoha ukahida kubhonana ni Yesu. Bho bhabhuene, bhakan'sihi abhokai mu mkoa ghwa bhene.

< Mateyu 8 >