< Mateyu 7 >

1 “Musaweruze ena, kuti inunso mungadzaweruzidwe.
« Ne jugez pas, afin que vous ne soyez pas jugés.
2 Pakuti momwe inu muweruzira ena, inunso mudzaweruzidwa chimodzimodzi, muyeso umene muyesera ena inunso mudzayesedwa ndi womwewo.
Car, de quelque jugement que vous jugiez, on vous jugera, et de quelque mesure que vous mesuriez, on vous mesurera.
3 “Chifukwa chiyani iwe uyangʼana kachitsotso ka mʼdiso la mʼbale wako koma susamalira chimtengo chili mʼdiso mwako?
Pourquoi vois-tu la tache qui est dans l'œil de ton frère, et ne considères-tu pas la poutre qui est dans ton propre œil?
4 Kodi unganene bwanji kwa mʼbale wako kuti, ‘Ndikuchotse kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene nthawi zonse chimtengo uli nacho mʼdiso mwako?
Ou comment diras-tu à ton frère: « Laisse-moi enlever la paille de ton œil », et voici que la poutre est dans ton propre œil?
5 Wachiphamaso iwe! Yamba wachotsa chimtengo chili mʼdiso mwako ndipo pamenepo udzatha kuona bwino ndi kuchotsa kachitsotso kali mʼdiso mwa mʼbale wako.
Hypocrite! Enlève d'abord la poutre de ton œil, et tu verras ensuite clairement pour enlever la paille de l'œil de ton frère.
6 “Musapatse agalu zinthu zopatulika; kapena musaponyere nkhumba ngale zanu. Pakuti ngati mutero, zidzaziponda ndipo pomwepo zidzakutembenukirani ndi kukudulani nthulinthuli.
« Ne donnez pas aux chiens ce qui est sacré, et ne jetez pas vos perles devant les cochons, de peur qu'ils ne les foulent aux pieds, ne se retournent et ne vous mettent en pièces.
7 “Pemphani ndipo mudzapatsidwa; funafunani ndipo mudzapeza; gogodani ndipo adzakutsekulirani.
« Demandez, et l'on vous donnera. Cherchez, et vous trouverez. Frappez, et l'on vous ouvrira.
8 Pakuti wopempha aliyense amalandira; ndi wofuna amapeza; ndipo iye amene agogoda, adzamutsekulira.
Car quiconque demande reçoit. Celui qui cherche trouve. A celui qui frappe, on ouvrira.
9 “Ndani mwa inu, mwana wake akamupempha buledi amamupatsa mwala?
Ou bien, qui est parmi vous qui, si son fils lui demande du pain, lui donnera une pierre?
10 Kapena ngati mwana apempha nsomba, kodi amamupatsa njoka?
Ou, s'il demande un poisson, qui lui donnera un serpent?
11 Tsono ngati inu woyipitsitsa mumadziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, nanga Atate anu akumwamba sadzapereka mphatso zabwino kwa iwo amene amupempha?
Si donc, méchants comme vous l'êtes, vous savez donner de bonnes choses à vos enfants, à combien plus forte raison votre Père qui est dans les cieux donnera-t-il de bonnes choses à ceux qui les lui demandent.
12 Nʼchifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu akuchitireni, yambani ndinu kuwachitira, pakuti izi ndi zimene malamulo ndi aneneri amaphunzitsa.
C'est pourquoi, tout ce que vous voulez que les hommes vous fassent, vous le leur ferez aussi; car c'est là la loi et les prophètes.
13 “Lowani pa chipata chopapatiza. Pakuti chipata cholowera kuchiwonongeko nʼchachikulu ndipo msewu wake ndi waukulunso. Ndipo anthu ambiri amalowera pamenepo.
« Entrez par la porte étroite; car la porte est large, et le chemin est spacieux, qui mène à la perdition, et il y a beaucoup de gens qui entrent par là.
14 Koma chipata ndi chopapatiza ndi msewu ndi waungʼono umene utsogolera anthu ku moyo wosatha ndipo ndi owerengeka okha amene ayipeza njirayo.
Que la porte est étroite et le chemin resserré qui mène à la vie! Il y en a peu qui la trouvent.
15 “Chenjerani nawo aneneri onyenga. Amabwera kwa inu atavala zikopa zankhosa, koma mʼkati mwawo ali mimbulu yolusa.
« Gardez-vous des faux prophètes, qui viennent à vous en habits de brebis, mais qui sont en réalité des loups ravisseurs.
16 Mudzawazindikira iwo ndi zipatso zawo. Kodi anthu amathyola mpesa pa mtengo wa minga, kapena nkhuyu pa nthula?
C'est à leurs fruits que vous les reconnaîtrez. Cueillez-vous des raisins sur des épines ou des figues sur des chardons?
17 Chimodzimodzinso mtengo wabwino umabala chipatso chabwino, koma mtengo woyipa umabala chipatso choyipa.
De même, tout bon arbre produit de bons fruits, mais l'arbre corrompu produit de mauvais fruits.
18 Mtengo wabwino sungabale chipatso choyipa, ndi mtengo woyipa sungabale chipatso chabwino.
Un bon arbre ne peut pas produire de mauvais fruits, et un arbre corrompu ne peut pas non plus produire de bons fruits.
19 Mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino umadulidwa ndi kuponyedwa pa moto.
Tout arbre qui ne produit pas de bons fruits est coupé et jeté au feu.
20 Momwemonso, ndi zipatso zawo iwo mudzawazindikira.
C'est donc à leurs fruits que vous les reconnaîtrez.
21 “Si munthu aliyense amene amanena kwa Ine, ‘Ambuye, Ambuye,’ adzalowe mu ufumu wakumwamba, koma ndi yekhayo amene amachita chifuniro cha Atate anga amene ali kumwamba.
« Tous ceux qui me disent: « Seigneur, Seigneur » n'entreront pas dans le Royaume des cieux, mais celui qui fait la volonté de mon Père qui est dans les cieux.
22 Ambiri adzati kwa Ine pa tsikulo, ‘Ambuye, Ambuye, kodi sitinkanenera mʼdzina lanu ndi mʼdzina lanunso tinkatulutsa ziwanda ndi kuchita zodabwitsa zambiri?’
En ce jour-là, plusieurs me diront: « Seigneur, Seigneur, n'avons-nous pas prophétisé en ton nom, chassé des démons en ton nom, et fait beaucoup de miracles en ton nom?
23 Pamenepo ndidzawawuza momveka bwino kuti, ‘Sindinakudziweni inu. Chokani kwa Ine, inu ochita zoyipa!’
Alors je leur dirai: « Je ne vous ai jamais connus. Retirez-vous de moi, vous qui commettez l'iniquité ».
24 “Nʼchifukwa chake aliyense amene amva mawu anga ndi kuwachita akufanana ndi munthu wanzeru amene anamanga nyumba yake pa thanthwe.
« Quiconque entend ces paroles que je dis et les met en pratique, je le comparerai à un homme sage qui a bâti sa maison sur le roc.
25 Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo; koma sinagwe, chifukwa maziko ake anali pa thanthwe.
La pluie est tombée, les inondations sont survenues, les vents ont soufflé et ont battu cette maison, mais elle n'est pas tombée, car elle était fondée sur le roc.
26 Koma aliyense amene amva mawu angawa ndi kusawachita ali ngati munthu wopusa amene anamanga nyumba yake pa mchenga.
Quiconque entend ces paroles que je dis et ne les met pas en pratique est semblable à un homme insensé qui a bâti sa maison sur le sable.
27 Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo, ndipo inagwa ndipo kugwa kwake kunali kwakukulu.”
La pluie est tombée, les inondations sont arrivées, les vents ont soufflé et frappé cette maison, et elle est tombée, et sa chute a été grande. »
28 Yesu atamaliza kunena zonsezi, magulu a anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake,
Lorsque Jésus eut achevé de dire ces choses, la foule fut frappée de son enseignement,
29 chifukwa anaphunzitsa ngati amene anali ndi ulamuliro osati ngati aphunzitsi amalamulo.
car il les enseignait avec autorité, et non comme les scribes.

< Mateyu 7 >