< Mateyu 6 >
1 “Samalani kuti musachite ntchito zanu zolungama pamaso pa anthu kuti akuoneni. Popeza ngati mutero simudzalandira mphotho yochokera kwa Atate anu akumwamba.
»Pazite se, da svoje miloščine ne izkazujete pred ljudmi, da bi jo le-ti videli, sicer nimate nobene nagrade od svojega Očeta, ki je v nebesih.
2 “Pamene mupereka zachifundo, musachite modzionetsera monga amachita achiphamaso mʼmasunagoge ndi pa misewu kuti atamidwe ndi anthu. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwowo alandiriratu mphotho yawo yonse.
Zato kadar daješ svojo miloščino, ne trobi pred seboj, kakor počno hinavci v sinagogah in na ulicah, da bi lahko imeli slavo od ljudi. Resnično, povem vam: ›Imajo svojo nagrado.‹
3 Koma pamene mupereka zachifundo, dzanja lanu lamanzere lisadziwe chimene dzanja lanu lamanja likuchita,
Toda kadar ti daješ miloščino, naj tvoja levica ne ve kaj počne tvoja desnica,
4 kotero kuti kupereka kwanu kukhale mwachinsinsi. Ndipo Atate anu amene amaona zochitika mwachinsinsi, adzakupatsani mphotho.
da bo tvoja miloščina lahko na skrivnem in tvoj Oče, ki sam vidi na skrivnem, te bo javno nagradil.
5 “Pamene mupemphera, musakhale ngati achiphamaso, chifukwa iwo amakonda kupemphera choyimirira mʼmasunagoge ndi pa mphambano za mʼmisewu kuti anthu awaone. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwo alandiriratu mphotho yawo yonse.
In kadar moliš, ne bodi kakor so hinavci, kajti ti radi molijo, stoječ v sinagogah in na vogalih ulic, da jih ljudje lahko vidijo. Resnično, povem vam: ›Imajo svojo nagrado.‹
6 Koma pamene mupemphera, lowani mʼchipinda chanu chamʼkati, ndi kutseka chitseko ndipo mupemphere kwa Atate anu amene saoneka. Ndipo Atate anu, amene amaona zochitika mseri, adzakupatsani mphotho.
Toda ti, kadar ti moliš, vstopi v svojo sobico in ko si zaprl svoja vrata, moli k svojemu Očetu, ki je na skrivnem; in tvoj Oče, ki vidi na skrivnem, te bo nagradil javno.
7 Ndipo pamene mukupemphera, musamabwerezabwereza monga akunja, pakuti iwo amaganiza kuti adzamveka chifukwa chochulutsa mawu.
Toda ko molite, ne uporabljajte jalovih ponavljanj, kakor to počno pogani, kajti mislijo, da bodo uslišani zaradi svojega mnogega govorjenja.
8 Musakhale ngati iwo chifukwa Atate anu amadziwa zimene musowa musanapemphe.
Ne bodite jim zato podobni, kajti vaš Oče ve, katere stvari potrebujete, preden ga prosite.
9 “Chifukwa chake pempherani motere: “‘Atate athu akumwamba, dzina lanu lilemekezedwe,
Zatorej molíte na ta način: ›Oče naš, ki si v nebesih: ›Posvečuje naj se tvoje ime.
10 Ufumu wanu ubwere, chifuniro chanu chichitike pansi pano monga kumwamba.
Pridi tvoje kraljestvo. Zgôdi se tvoja volja na zemlji, kakor je v nebesih.
11 Mutipatse chakudya chathu chalero.
Daj nam danes naš vsakdanji kruh.
12 Mutikhululukire mangawa athu, monga ifenso tawakhululukira amangawa athu.
In odpusti nam naše dolge, kakor mi odpuščamo svojim dolžnikom.
13 Ndipo musatitengere kokatiyesa; koma mutipulumutse kwa woyipayo.’
In ne vôdi nas v skušnjavo, temveč nas osvobodi pred zlom, kajti tvoje je kraljestvo in moč in slava, na veke. Amen.‹
14 Ngati inu mukhululukira anthu pamene akuchimwirani, Atate anu akumwamba adzakukhululukirani.
Kajti če ljudem odpustite njihove prekrške, bo prav tako vaš nebeški Oče odpustil vam.
15 Koma ngati inu simukhululukira anthu zolakwa zawo, Atate anunso sadzakukhululukirani machimo anu.
Toda če ljudem ne odpustite njihovih prekrškov, tudi vaš Oče ne bo odpustil vaših prekrškov.
16 “Pamene mukusala kudya, musaonetse nkhope yachisoni monga achita achiphamaso, pakuti iwo amasintha nkhope zawo kuonetsa anthu kuti akusala kudya. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwo alandiriratu mphotho yawo yonse.
Poleg tega, kadar se postite, ne bodite kakor hinavci, potrtega obličja; kajti kazijo svoje obraze, da bi bilo ljudem videti, da se postijo. Resnično, povem vam: ›Imajo svojo nagrado.‹
17 Koma pamene ukusala kudya, samba mʼmaso nudzole mafuta kumutu,
Toda kadar se ti postiš, mazili svojo glavo in umij svoj obraz,
18 kuti usaonekere kwa anthu kuti ukusala kudya koma kwa Atate ako ali mseri; ndipo Atate ako amene amaona za mseri adzakupatsa mphotho.
da ne bo videti ljudem, da se postiš, temveč tvojemu Očetu, ki je na skrivnem, in tvoj Oče, ki vidi na skrivnem, te bo nagradil javno.
19 “Musadziwunjikire chuma pa dziko lapansi, pamene njenjete ndi dzimbiri zimawononga ndi pamene mbala zimathyola ndi kuba.
Ne shranjujte si zakladov na zemlji, kjer molj in rja delata razkroj in kjer tatovi vlamljajo in kradejo,
20 Koma mudziwunjikire chuma kumwamba kumene njenjete ndi dzimbiri siziwononga ndipo mbala sizithyola ndi kuba.
temveč si zase shranjujte zaklade v nebesih, kjer niti molj niti rja ne delata razkroja in kjer tatovi ne vlamljajo niti ne kradejo,
21 Pakuti kumene kuli chuma chako, mtima wako udzakhala komweko.
kajti kjer je tvoj zaklad, tam bo tudi tvoje srce.
22 “Diso ndi nyale ya thupi. Ngati maso ako ali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mʼkuwala.
Svetloba telesa je oko; če je torej tvoje oko enovito, bo tvoje celotno telo polno svetlobe.
23 Koma ngati maso ako sali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mu mdima. Koma ngati kuwala kuli mwa iwe ndi mdima, ndiye kuti mdimawo ndi waukulu bwanji!
Toda če bo tvoje oko hudobno, bo tvoje celotno telo polno teme. Če bo torej svetloba, ki je v tebi, tema, kako velika je ta tema!
24 “Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri. Pakuti pena adzamuda mmodzi ndi kukonda winayo kapena adzagwira ntchito mokhulupirika kwa mmodzi, nadzanyoza winayo. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa chuma pa nthawi imodzi.
Nihče ne more služiti dvema gospodarjema; kajti ali bo enega sovražil in drugega ljubil, ali pa se bo držal k enemu in preziral drugega. Ne morete služiti Bogu in mamonu.
25 “Nʼchifukwa chake ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu kuti mudzadya chiyani kapena mudzamwa chiyani; kapenanso za thupi lanu kuti mudzavala chiyani. Kodi moyo suposa chakudya? Kodi thupi siliposa zovala?
Zatorej vam pravim: ›Ne vznemirjajte se in ne skrbite glede svojega življenja, kaj boste jedli ali kaj boste pili niti za svoje telo, kaj boste oblekli. Kaj ni življenje več kot hrana in telo več kot oblačilo?
26 Onani mbalame zamlengalenga sizifesa kapena kukolola kapena kusunga mʼnkhokwe komabe Atate anu akumwamba amazidyetsa. Kodi inu simuziposa kwambiri?
Poglejte perjad neba, kajti ne seje niti ne žanje niti ne zbira v skednje, vendar jih vaš nebeški Oče hrani. Ali niste mnogo boljši kakor one?
27 Kodi ndani wa inu podandaula angathe kuwonjeza ora limodzi pa moyo wake?
Kdo izmed vas lahko z vznemirjanjem in skrbmi svoji postavi doda en komolec?
28 “Ndipo bwanji inu mudera nkhawa za zovala? Onani makulidwe a maluwa akutchire. Sagwira ntchito kapena kuwomba nsalu.
In zakaj se vznemirjate in skrbite za oblačilo? Preudarite o lilijah travnika, kako rastejo; ne garajo niti ne predejo.‹
29 Ndikukuwuzani kuti angakhale Solomoni mu ulemerero wake sanavale mofanana ndi limodzi la maluwa amenewa.
In vendar vam povem: ›Da celó Salomon, v vsej svoji slavi, ni bil oblečen tako kakor ena izmed teh.‹
30 Ngati umu ndi mmene Mulungu avekera udzu wa kutchire umene ulipo lero ndipo mawa uponyedwa ku moto, kodi sadzakuvekani koposa? Aa! Inu a chikhulupiriro chochepa!
Zatorej, če Bog tako oblači travo polja, ki danes je, jutri pa je vržena v peč, ali ne bo mnogo bolj oblačil vas, oh vi, maloverni?
31 Chifukwa chake musadere nkhawa ndi kuti, ‘Tidzadya chiyani?’ kapena ‘Tidzamwa chiyani?’ kapena ‘Tidzavala chiyani?’
Zato se ne vznemirjate in ne skrbite, rekoč: ›Kaj bomo jedli?‹ ali: ›Kaj bomo pili?‹ ali: ›S čim bomo oblečeni?‹
32 Pakuti anthu akunja amazifuna zinthu zonsezi ndipo Atate anu akumwamba adziwa kuti musowa zimenezi.
(Kajti za vsemi temi stvarmi povprašujejo pogani), kajti vaš nebeški Oče ve, da potrebujete vse te stvari.
33 Koma muyambe mwafuna ufumu wake ndi chilungamo chake ndipo zinthu zonsezi zidzapatsidwa kwa inu.
Toda iščite najprej Božje kraljestvo in njegovo pravičnost in vse te stvari vam bodo dodane.
34 Chifukwa chake musadere nkhawa ndi za mawa, popeza tsiku lililonse lili ndi zovuta zake zokwanira.
Zato se ne vznemirjate in ne skrbite za jutrišnji dan, kajti jutrišnji dan bo sam poskrbel za stvari. Zadostno je dnevu le tega zlo.«