< Mateyu 5 >
1 Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye,
Побачивши ж народ, зійшов на гору, і,як сїв, приступили до Него ученики Його;
2 ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,
і відкрив Він уста свої, і навчав їх, глаголючи:
3 “Odala ndi amene ali osauka mu mzimu, chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.
Блаженні вбогі духом, бо їх царство небесне.
4 Odala ndi amene ali achisoni, chifukwa adzatonthozedwa.
Блаженні сумні, бо такі втїшять ся.
5 Odala ndi amene ali ofatsa, chifukwa adzalandira dziko lapansi.
Блаженні тихі, бо такі осягнуть землю.
6 Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo, chifukwa adzakhutitsidwa.
Блаженні голодні й жадні правди, бо такі наситять ся.
7 Odala ndi amene ali ndi chifundo, chifukwa adzawachitira chifundo.
Блаженні милостиві, бо такі будуть помилувані.
8 Odala ndi amene ali oyera mtima, chifukwa adzaona Mulungu.
Блаженні чисті серцем, бо такі побачять Бога.
9 Ndi odala amene amabweretsa mtendere, chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.
Блаженні миротворці, бо такі синами Божими звати муть ся.
10 Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo, pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”
Блаженні, кого гонять за правду, бо їх царство небесне.
11 “Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine.
Блаженні ви, коли вас безчестити муть, та гонити муть, та казати муть на вас усяке лихе слово не по правдї, ради мене.
12 Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.
Радуйтесь і веселітесь: бо велика нагорода ваша на небі; так бо гонили й пророків, що бували перше вас.
13 “Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.
Ви сіль землї; коли ж сіль звітріє, то чим солити? Нї-на-що не годить ся тоді вона, тільки щоб викинути геть і щоб топтали її люде.
14 “Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika.
Ви сьвітло сьвіту. Не може город сховати ся, стоячи на горі;
15 Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo.
і, засьвітивши сьвічку, не став лять під посудину, а на сьвічнику то й сьвітить вона всїм, хто в хатї.
16 Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.
так нехай сяє сьвітло ваше перед людьми, щоб вони бачили ваші добрі дїла, й прославляли Отця вашого, що на небі.
17 “Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa.
Не думайте, що я прийшов знївечити закон або пророків; не прийшов я знївечити, а сповнити.
18 Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa.
Істино бо глаголю вам: Доки перейде небо й земля, одна йота, або одна титла не перейде з закону, аж поки все станеть ся.
19 Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba.
Тим, хто поламле одну найменшу з сих заповідей і навчить так людей, той звати меть ся найменшим у царстві небесному; а хто сповнить і навчить, той звати меть ся великим у царстві небесному.
20 Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.
Глаголю бо вам: Що коли ваша правда не переважить письменників та Фарисеїв, то не ввійдете в царство небесне.
21 “Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’
Чували ви, що сказано старосьвіцьким: Не вбий, а хто вбє, на того буде суд.
22 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna )
Я ж вам глаголю: Хто сердить ся на брата свого без причини, на того буде суд; а хто скаже на брата свого: Рака [Безчесний], на того буде громадський суд; хто ж скаже: дурню, на того буде огонь пекельний. (Geenna )
23 “Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa,
Тим, коли принесеш дар свій до жертівнї, й згадаєш там, що твій брат має що проти тебе;
24 usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.
зостав свій дар перед жертівнею, і йди геть, помирись перш із братом твоїм, а тоді прийди й подай дар твій.
25 “Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende.
Мирись із твоїм противником хутко, доки ти ще в дорозі з ним, щоб не віддав тебе противник судді, а суддя не віддав тебе осавулї (слузї), і не вкинуто тебе в темницю.
26 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.
Істино глаголю тобі: Не вийдеш звідтіля, доки не віддаси й останнього шеляга.
27 “Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’
Чували ви, що сказано старосьвіцьким: Не чини перелюбу.
28 Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake.
Я ж вам глаголю: Хто спогляне на жінку жадібним оком, той уже вчинив перелюб із нею в серці своїм.
29 Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
Коли ж око твоє праве блазнить тебе, вирви його, й кинь од себе; бо більша користь тобі, щоб один із членів твоїх згинув, а не все тіло вкинуто в пекло. (Geenna )
30 Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
І коли права рука твоя блазнить тебе відотни її, й кинь од себе; більша бо користь тобі, щоб один із членів твоїх згинув, а не все тіло твоє вкинуто в пекло. (Geenna )
31 “Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’
Сказано ж: Що хто розводить ся з жінкою своєю, нехай дасть їй розвідний лист.
32 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.
Я ж вам глаголю: Що хто розведеть ся з жінкою своєю, хиба що за перелюб, доводить її до перелюбу; й хто оженить ся з розвідкою, чинить перелюб.
33 “Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’
Знов чували, що сказано старосьвіцьким: Не кленись криво, а сповняй перед Господом обітниці твої.
34 Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu.
Я ж вам глаголю: Не клянїть ся зовсім: нї небом, бо воно престол Божий;
35 Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu.
нї землею, бо вона підніжок ніг Його; нї Єрусалимом, бо се город великого царя;
36 Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi.
нї головою твоєю не клянись, бо не зможеш зробити нї одного волоса білим або чорним.
37 Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.
Слово ж ваще нехай буде: так, так; нї, нї; бо що більш над се, те від лихого.
38 “Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’
Чували ви, що сказано: Око за око, й зуб за зуб.
39 Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo.
Я ж вам глаголю: Не противтесь лихому, а хто вдарить тебе у праву щоку твою, повернись до него й другою.
40 Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako.
І хто схоче судитись із тобою і зняти з тебе свиту, віддай йому й жупанок.
41 Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri.
І хто силувати ме тебе йти милю, йди з ним дві.
42 Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.
Дай, хто в тебе просить, і хто хоче в тебе позичити, не одвертайсь од него.
43 “Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’
Чували ви, що сказано: Люби ближнього твого, й ненавидь ворога твого.
44 Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani
Я ж вам глаголю: Любіть ворогів ваших, благословляйте, хто клене вас, робіть добро, хто ненавидить вас, і моліть ся за тих, що обижають вас і гонять вас;
45 kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’
щоб вам бути синами Отця вашого, що на небі; Він бо велить сонцю своєму сходити над лихими й над добрими, й посилає дощ на праведних і неправедних.
46 Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi?
Бо коли ви любите тих, що люблять вас, то за що вам нагорода? хиба й митники не те саме роблять?
47 Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi?
І коли витаєте тільки братів ваших, то що надто робите? хиба й митники не так роблять?
48 Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”
Оце ж бувайте звершені, як Отець ваш, що на небі, звершений.