< Mateyu 5 >
1 Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye,
Daro derey shiiqidaysa beyida wode Yesusay pude zuma bolla kezidi utides, iza kaalizaytika izakko yida.
2 ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,
Izikka ista hizigidi tamarso oykides.
3 “Odala ndi amene ali osauka mu mzimu, chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.
ayanan bena kawushizayti anjetidayta ays gikko salo kawothi istasa.
4 Odala ndi amene ali achisoni, chifukwa adzatonthozedwa.
qadhetizayti anjetidayta ays gikko isti ministana.
5 Odala ndi amene ali ofatsa, chifukwa adzalandira dziko lapansi.
ashketi anjetidayta ays gikko isti biitta latana.
6 Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo, chifukwa adzakhutitsidwa.
xiloteth gafetizaytine saamotizayti anjetidayta ays gikko isti kalana.
7 Odala ndi amene ali ndi chifundo, chifukwa adzawachitira chifundo.
asas lo7o othizayti anjetidayta ays gikko istikka lo7oy othistana??
8 Odala ndi amene ali oyera mtima, chifukwa adzaona Mulungu.
wozana xilloti anjtidayta ays gikko isti Xoos beyana.
9 Ndi odala amene amabweretsa mtendere, chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.
saroteth oothizayti anjetidayta ays gikko isti xoosa nayta geeteti xeygistana.
10 Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo, pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”
xillotetha gish goodetizayti anjetidayta ays gikko salo kawotethi istasa.
11 “Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine.
Ta gedon asay intena cayikko, goodikonne iita yo wordora inte bolla haasa7ikko inte anjetidayta.
12 Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.
Inte salon demana waagay keehi gita gidida gish ufaysan guppitte. Ays gikko intefe kase nabetakka hessaththo gooddida.
13 “Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.
inte ha biita asas maxine mala. Maxiney ba mal7otetha yediza gidiko zaridi demanas danda7ize? gede kare yegetidi yedheteespe atin.
14 “Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika.
Inte deres po7o. Zuma bola diza katamaya qotistanas danda7uku.
15 Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo.
Asi xoomppe oythidi kethan diza asa wursos po7ana mala dhoqason wothetes atin gema son wothi eretena.
16 Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.
Hesathokka asay inte lo7o otho beydi inte salon diza inte aawa bonchana mala inte po7oy asa sinthan po7o.
17 “Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa.
Tani Musse wogane nabeta qaala sharana yida intes milatopo; polanas yadis atin sharanas yabeykke.
18 Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa.
Ta intess tumu gays, saloyne bitay adhana gakanas Musse wogay wuri polistana atin wogappe isi pidaleykka woykko issi qerinakka shaaretuku.
19 Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba.
Hessa gish onikka ha azazoyntafe guxizaro gidikokka othonta yegi adhikko, hankoytakka yedhi adhana mala tamarsikko salo kawotethan he uray guth geteti xeygistana. Gido atin hayta azazota othi polishe hankoyta polana mala tamarsikko izi salo kawotethan gta getistana.
20 Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.
Ta intes gays, inte xillotethi Parsawistapene Musse woga tamarsizayta xillotethafe aadhonta agikko salo kawoteth gelana danda7ekista.
21 “Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’
Kasse asatas wodhopa, wodhida ura bolla pirdistana getetidaysa inte siydista.
22 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna )
Ta qasse intes gizay ba isha bolla wogay baynda hanqetiza ura bolla pirdistana, onikka ba isha napay gizadey dere dulata sinthan oychistana, eya giza ura ganame tama pirday naages. (Geenna )
23 “Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa,
Hessa gish neni yarsho shishizason Xoossas yarshana gishin ne ishay ne bolla michetidazi nes qofetikko,
24 usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.
ne yarshizaysa hen yarshoson aga gada koyro bada ne ishara giga, hessafe guye simada ne yarshoza Xoossas shisha.
25 “Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende.
nena kasasida ne morkey ne bolla pirdsonta mala pirdiza danay qachizaysas nena athi imonta mala qasho kethan ne wodhontamala buro ogge bolla dashe ne morkke urara elela giga gida.
26 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.
Ta nes tumu gays izi pirdisi wursida gidikko wusetha isi santimiyo qanxana gakans qashoppe birshistakka.
27 “Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’
laymatoppa gizaysa inte siydista
28 Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake.
Tani gidikko intena hiz gays macasha amo ayferra xelida uray wuri ba wozinan izira laymatadess.
29 Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
Nagara othans ne oshacha ayfey nes gaso gidiko neppe kessa wora yega, ne asatethay kumeth gede ganame taman yegistanape ne asatethafe isay pacikko lo7o. (Geenna )
30 Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
Ne oshacha kushey nagara othos gaso gidiko neppe qanxa diga ne asatethay kumeth ganamen yegistanaysafe ne asatethafe issi bilitey ness pace gidiko lo7o. (Geenna )
31 “Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’
machcho anjizadey anjida firma waraqata izis imana beses getetidees.
32 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.
Tani qasse intena hizgays hara urara laymatishin beyonta dishe ba maco anjizadey wuri iza laymatana mala othes. Hesathokka anjetizaro ekizadeykka laymatida mala qodetes.
33 “Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’
kasse asatas wordo caqofa; Xoossa sinthan ne caqidaysa naga getetidaysa inte siyidista.
34 Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu.
Ta qass intena aykkokka caqofite gays saloy Xoossa wonbara gidida gish salon caqofite.
35 Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu.
Bitay Xoossa soy shempizaso gidida gish bitankka caqopite woga kawo katama gidida gish Yerusalamenkka caqopite.
36 Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi.
Inte hu7enikka caqopite inte hu7e iskistappe issineyokka bothu woykko kareth histanas danda7ekista.
37 Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.
hessa gish inte inte garsan hasa7etishin inte hasa7ay E ganaz E gite akkay ganas akkay gite, hessappe kare gididay wuri ita urappe yizaza.
38 “Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’
Ayfe gishas ayfe acha gishas acha getetidaysa inte siyidista
39 Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo.
Ta kass intes gizay ita othida urara eqetofite gido attin nes oshacha shagala baqizades hankoysakka yusha bessa.
40 Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako.
Issi uray ne garsara maydaysa neppe ekkanas nena motikko bolara maydaysakka gujada izas imma
41 Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri.
Issi ass nena issi sate ooge ne bana mala wolqathikko issippe nam7u dakko gidana ogge iza bays.
42 Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.
Nena wosizades imma, neppe tal7e ekkanas koyzades zokko zaroppa.
43 “Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’
Ne lagge siqa, ne morke siqa getetidaysa siyidista
44 Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani
Ta qass intena inte morketa dosite, intena godizaytas wosite gays.
45 kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’
Inte hessaththo othikko inte salo awas nayta gidana. Izi awa arshe itatasine lo7otas issi bola omo imess irakka xilotasine nagaranchatas issi bola bukises.
46 Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi?
Intena dosizayta xalala inte dosikko intes aza wagay dize? Qaraxa ekizayti hessaththo othetene?
47 Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi?
Inte ishata xala inte sarothikko hankoytappe azan lo7eti? amnontaytikka hessaththo othetes.
48 Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”
hessa gish inte salo away wothoy bayndade gidida mala intekka wothoy bayndade gidite.