< Mateyu 5 >
1 Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye,
But, seeing the multitudes, he went up into a mountain, —and, when he had taken a seat, his disciples came unto him;
2 ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,
and, opening his mouth, he began teaching them, saying: —
3 “Odala ndi amene ali osauka mu mzimu, chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.
Happy, the destitute, in spirit; for, theirs, is the kingdom of the heavens;
4 Odala ndi amene ali achisoni, chifukwa adzatonthozedwa.
Happy, they who mourn; for, they, shall be comforted:
5 Odala ndi amene ali ofatsa, chifukwa adzalandira dziko lapansi.
Happy, the meek; for, they, shall inherit the earth:
6 Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo, chifukwa adzakhutitsidwa.
Happy, they who hunger and thirst for righteousness; for, they, shall be filled:
7 Odala ndi amene ali ndi chifundo, chifukwa adzawachitira chifundo.
Happy, the merciful; for, they, shall receive mercy:
8 Odala ndi amene ali oyera mtima, chifukwa adzaona Mulungu.
Happy, the pure, in heart; for, they, shall, see God:
9 Ndi odala amene amabweretsa mtendere, chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.
Happy, the peacemakers; for, they, shall be, called sons of God:
10 Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo, pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”
Happy, they who have been persecuted for righteousness’ sake; for, theirs, is the kingdom of the heavens.
11 “Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine.
Happy, are ye, whensoever they may reproach you and persecute you, and say every evil thing against you, falsely, for my sake:
12 Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.
Rejoice and exult, because, your reward, is great in the heavens; for, so, persecuted they the prophets who were before you.
13 “Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.
Ye, are the salt of the earth; but, if the salt become tasteless, wherewith shall it be salted? it is good, for nothing, any more, save, being cast out, to be trampled on by men.
14 “Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika.
Ye, are the light of the world: it is impossible for a city to be hid, on the top of a mountain, lying.
15 Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo.
Neither light they a lamp, and place it under the measure; but upon the lampstand, and it giveth light to all that are in the house.
16 Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.
In like manner, let your light shine before men, —that they may see your good works, —and glorify your Father who is in the heavens.
17 “Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa.
Do not think, that I came to pull down the law, or the prophets, —I came not to pull down, but to fulfil.
18 Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa.
For, verily, I say unto you, until the heaven and the earth shall pass away, one least letter, or one point, may in nowise pass away from the law, till all be accomplished.
19 Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba.
Whosoever, therefore, shall relax one of these commandments, the least, and teach men so, shall be called, least, in the kingdom of the heavens; but, whosoever shall do and teach, the same, shall be called, great, in the kingdom of the heavens.
20 Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.
For I say unto you, that, unless your righteousness exceed that of the Scribes and Pharisees, in nowise, may ye enter into the kingdom of the heavens.
21 “Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’
Ye have heard, that it was said, to them of olden time, —Thou shalt not commit murder, and, whosoever shall commit murder, shall be, liable, to judgment.
22 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna )
But, I, say unto you, that, every one who is angry with his brother, shall be, liable, to judgment, —and, whosoever shall say to his brother, Worthless one!, shall be, liable, to the high council; and, whosoever shall say, Rebel!, shall be, liable, unto the fiery gehenna. (Geenna )
23 “Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa,
If, therefore, thou be bearing thy gift towards the altar, and, there, shouldst remember that, thy brother, hath aught against thee,
24 usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.
leave, there, thy gift before the altar, and withdraw, —first, be reconciled unto thy brother, and, then, coming, be offering thy gift.
25 “Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende.
Be making agreement with thine adversary, quickly, while thou art with him, in the way, —lest once thine adversary deliver thee up unto the judge, and the judge, unto the officer, and, into prison, thou be cast.
26 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.
Verily, I say unto thee, In nowise, mayest thou come out from thence, until thou pay the last halfpenny.
27 “Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’
Ye have heard, that it was said, Thou shalt not commit adultery:
28 Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake.
But, I, say unto you, that, Every one who looketh on a woman so as to covet her, already, hath committed adultery with her, in his heart.
29 Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
And, if, thy right eye, is causing thee to stumble, pluck it out, and cast it from thee, —for it profiteth thee, that, one of thy members, should perish, and not, thy whole body, be cast into gehenna. (Geenna )
30 Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna )
And, if, thy right hand, is causing thee to stumble, cut it off, and cast it from thee, —for it profiteth thee, that, one of thy members, should perish, and not, thy whole body, into gehenna, depart. (Geenna )
31 “Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’
It was said, moreover, Whosoever shall divorce his wife, let him give her a writing of divorcement;
32 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.
But, I, say unto you, that, Everyone who divorceth his wife—saving for unfaithfulness, causeth her to be made an adulteress, —[and, whosoever shall marry a divorced woman, committeth adultery].
33 “Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’
Again, ye have heard that it was said, to them of olden time, Thou shalt not swear falsely, —but shalt render unto the Lord, thine oaths.
34 Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu.
But, I, tell you—not to swear, at all: Neither by heaven, because it is the, throne of God, —
35 Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu.
Nor by the earth, because it is his, footstool; nor by Jerusalem, because, it is the, city, of the Great King;
36 Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi.
Nor, by thine own head, mayest thou swear, because thou art not able to make, one hair, white or black.
37 Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.
But let your word be, Yea, yea, —Nay, nay; and, what goeth beyond these, is, of evil.
38 “Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’
Ye have heard, that it was said, —Eye for eye, and tooth for tooth.
39 Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo.
But, I, tell you, not to resist evil, —Nay, whoever is smiting thee on the right cheek, turn to him, the other also;
40 Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako.
And, him who is desiring thee to be judged, and to take, thy tunic, let him have, thy mantle also.
41 Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri.
And, whoever shall impress thee one mile, go with him two:
42 Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.
To him who is asking thee, give; and, him who is desiring from thee to borrow, do not thou turn away.
43 “Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’
Ye have heard, that it was said, Thou shalt love thy neighbour, and hate thine enemy.
44 Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani
But, I, say unto you, Be loving your enemies, and praying for them who are persecuting you:
45 kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’
That ye may become sons of your Father who is in the heavens: because, his sun, he maketh arise on evil and good, and sendeth rain, on just and unjust.
46 Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi?
For, if ye love them that love you, what reward have ye? are not, even the tax-collectors, the same thing, doing?
47 Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi?
And, if ye salute your brethren only, what, more than common, are ye doing? are not, even the nations, the same thing, doing?
48 Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”
Ye, therefore, shall become, perfect: as, your heavenly Father, is perfect.