< Mateyu 5 >

1 Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye,
ANAE jalie si Jesus y linajyan taotao, cajulo gui un sabana, ya matachong; ya y disipuluña manmato guiya güiya.
2 ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,
Ya jababa y pachotña ya jafanagüe, ilegña:
3 “Odala ndi amene ali osauka mu mzimu, chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.
Mandichoso y mamoble gui Espiritu, sa uiyonñija y raenon langet.
4 Odala ndi amene ali achisoni, chifukwa adzatonthozedwa.
Mandichoso y mantriste, sa sija umanafanmagof.
5 Odala ndi amene ali ofatsa, chifukwa adzalandira dziko lapansi.
Mandichoso y manmanso, sa sija ufanmaereda ni y tano.
6 Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo, chifukwa adzakhutitsidwa.
Mandichoso y manñalang yan manmajo ni tininas, sa sija umanafanjaspog.
7 Odala ndi amene ali ndi chifundo, chifukwa adzawachitira chifundo.
Mandichoso y manyóase, sa sija ufantinaca ni minaase.
8 Odala ndi amene ali oyera mtima, chifukwa adzaona Mulungu.
Mandichoso y mangasgas corasonñija, sa sija ujalie si Yuus.
9 Ndi odala amene amabweretsa mtendere, chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.
Mandichoso y fumatitinas y pas, sa sija ufanmafanaan famaguon Yuus.
10 Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo, pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”
Mandichoso y manmapetsigue pot causa y tininas; sa uiyonñija y raenon langet.
11 “Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine.
Mandichoso jamyo, yaguin manmamatdise jamyo, yan manmapetsigue jamyo, yan manmasangane jamyo todo taelaye pot y naanjo, ya manmandague.
12 Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.
Fanmagof, ya infansenmagof, sa y premionmiyo gui langet sendangculo: sa taegüenaoja locue manmapetsigueñija y profeta sija ni y antes di jamyo.
13 “Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.
Jamyo y asigan y tano; ya yaguin y asiga malingo y maaseña, jafa taemano manasne? taya baliña, na umayute juyong ya umagacha ni y taotao.
14 “Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika.
Jamyo y candet y tano. Y siuda ni maplanta gui jilo y tano táquilo ti siña umatog.
15 Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo.
Taya candet umasonggue ya umapolo gui papa un medida; lao umapolo gui candelero, ya umanainina todo y mangaegue gui jalom guma.
16 Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.
Polo ya umanina y candetmiyo gui menan y taotao sija, para ujalie y mauleg chechonmiyo, ya innamagof y tatanmiyo ni y gaegue gui langet.
17 “Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa.
Chamiyo jumajaso na mato yo para juyulang y tinago pat y profeta sija; ti mato yo para juyulang, lao para jucumple.
18 Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa.
Sa magajet jusangane jamyo, nu y langet yan y tano ufalingo; lao ni un punto ni un pongpong gui tinago ufalingo, asta qui güiya todo macumple.
19 Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba.
Ya jayeja y yumulang uno güine gui sendiquique na tinago, ya mamanagüe ni taotao, diquique umafanaan gui raenon langet; lao jayeja y fumatinas ya mamanagüe umafanaan dangculo gui raenon langet.
20 Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.
Sa guajo sumangane jamyo: na y tininasmiyo yaguin ti mudongña qui y tininas y escriba yan y Fariseo sija, ti siña jamyo manjalom gui raenon langet.
21 “Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’
Injingogja y munjayan masangane sija gui manmalofan na tiempo: Chamo famumuno, ya jayeja y mamuno, peligroña gui juisio.
22 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena. (Geenna g1067)
Lao guajo sumangane jamyo na jayeja y lalalo ni cheluña, peligroña gui juisio, na jayeja y umalog ni cheluña, taetiningo jao, peligroña gui tribunal, lao jayeja y umalog bababa jao, peligroña gui guafen sasalaguan. (Geenna g1067)
23 “Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa,
Yaguin unchule y ninaimo guato gui attat, ya ayo nae unjaso na guaja linachimo gui chelumo;
24 usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.
Polo güije y ninaimo gui menan y attat, ya unjanao finena ya inatungo yan y chelumo, ya ayo nae untalo guato ya unnaenñaejon y ninaimo.
25 “Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende.
Atungo yan y contrariumo enseguidas, mientros gaegue jamyo gui chalanmiyo, noseaja, y cotrariumo unenentrega gui jues, ya y jues unenentrega gui ofisiat ya unmapolo gui preso.
26 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.
Magajet jusangane jamyo: Seguro na ti unjuyong güije, asta qui anapase y uttimo na coble.
27 “Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’
Injingogja y munjayan masangan: Munga umábale,
28 Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake.
Ya guajo sumangane jamyo, na jayeja y umatan y palaoan nu ábale na minalagoña, jafatinas yan güiya y ábale gui jalom corasonña.
29 Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna g1067)
Yaguin y agapa na atadogmo uninapodong jao, chule ya yute guiya jago; sa maulegña na ufalingo un pidaso guiya jago, qui todo y tataotaomo umayute guiya sasalaguan. (Geenna g1067)
30 Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. (Geenna g1067)
Ya yaguin y agapa na canaemo uninapodong jao, utut ya yute guiya jago; sa maulegña, na ufalingo un pidaso guiya jago, qui todo y tataotaomo umayute guiya sasalagüan. (Geenna g1067)
31 “Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’
Munjayan locue masangan: Jayeja y dumingo y asaguaña, umatugue y papet y inapattan umasagua.
32 Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.
Lao guajo sumangane jamyo, na y dumingo y asaguaña ya ti pot inábale, jafatinas y ábale; ya jayeja y umasagua ayo y umadingo, jafatinas y ábale.
33 “Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’
Injingogja locue y munjayan masangane sija gui manmalofan na tiempo: Munga manjula pot namaesa jao; lao unfatinas ni y Señot gui jinilamo.
34 Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu.
Lao guajo sumangane jamyo: Chamiyo fanmanjujula pot jafa; ti pot y langet, sa raenon Yuus;
35 Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu.
Ni pot y tano, sa sagan y adengña; ni pot Jerusalem, sa siuda y dangculo na Ray;
36 Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi.
Ni pot y ilumo unfanjula; sa ti siña y gaponulo uno naapaca, ni uno naatulong.
37 Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.
Lao yaguin manguentos jamyo, alog: Junggan, junggan; Aje, aje; sa yaguin mas qui este, taelaye jumuyong.
38 “Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’
Injingogja y munjayan masangan: Atadog yan atadog, nifen yan nifen,
39 Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo.
Lao guajo sumangane jamyo: Chamiyo fumatinas jafa contra y tinaelaye; yaguin jayejao pumatmada gui agapa na fasumo, birayeja ni y otro.
40 Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako.
Ya jayeja y munaquequemumojao ya jachule y magagomo, nae locue y capamo.
41 Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri.
Ya jayeja y umafuetsas jao na unjanao yan güiya un miya; unjanao yan güiya dos.
42 Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.
Y gumagao jao, nae; ya y mumalago umayao jao, chamo jao rumiuusa.
43 “Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’
Injingogja y munjayan masangan: Guaeya y tiguangmo ya chatlie y enemigomo.
44 Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani
Lao guajo sumangane jamyo: Guaeya y enemigonmiyo; bendise y mumatdidise jamyo; fantinas mauleg ni y chumatlie jamyo, tayuyute sija as Yuus ni y munamamajlao jamyo yan y pumetsigue jamyo,
45 kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’
Para infanfamaguon y tatanmiyo ni y gaegue gui langet, nu y janafanina y atdao gui jilo y manaelaye yan y manmauleg; ya janauchan gui jilo y manunas yan y timanunas.
46 Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi?
Sa yaguin inguaeya ayo y gumaeya jamyo, jafa premionmiyo? Ada ti jafatinas locue taegüenao y publicano sija?
47 Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi?
Yaguin unsaluda y mañelunmiyo, jafa unfatinas mauleg? Ada ti jafatinas locue taegüenao y ti mangilisyano?
48 Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”
Nafangabales jamyo taegüije y tatanmiyo ni y gaegue gui langet, cabales.

< Mateyu 5 >