< Mateyu 3 >
1 Mʼmasiku amenewo, Yohane Mʼbatizi anadza nalalikira mʼchipululu cha Yudeya
Ngalezonsuku kwafika uJohane uMbhabhathizi, etshumayela enkangala yeJudiya,
2 kuti, “Tembenukani mtima chifukwa ufumu wakumwamba wayandikira.”
esithi: Phendukani; ngoba umbuso wamazulu ususondele.
3 Uyu ndi amene mneneri Yesaya ananena za iye kuti, “Mawu a wofuwula mʼchipululu, ‘Konzani njira ya Ambuye, wongolani njira zake.’”
Ngoba nguye okwakhulunywa ngaye nguIsaya umprofethi, esithi: Ilizwi lomemezayo enkangala, lithi: Lungisani indlela yeNkosi; qondisani indledlana zayo.
4 Zovala za Yohane zinali zopangidwa ndi ubweya wa ngamira, ndipo amamangira lamba wachikopa mʼchiwuno mwake. Chakudya chake chinali dzombe ndi uchi wa kuthengo.
Njalo uJohane lo wayelesembatho sakhe soboya bekamela, lozwezwe lwesikhumba ekhalweni lwakhe; lokudla kwakhe kwakuzintethe loluju lweganga.
5 Anthu ankapita kwa iye kuchokera ku Yerusalemu ndi ku Yudeya konse ndi ku madera onse a Yorodani.
Kwasekuphumela kuye iJerusalema leJudiya yonke lelizwe lonke elizingelezele iJordani;
6 Ndipo akavomereza machimo awo ankabatizidwa mu mtsinje wa Yorodani.
basebebhabhathizwa nguye eJordani bevuma izono zabo.
7 Koma iye ataona Afarisi ndi Asaduki ambiri akubwera kumene ankabatiza, anawawuza kuti, “Ana a njoka inu! Ndani anakuchenjezani kuthawa mkwiyo umene ukubwera?
Kwathi ebona abanengi babaFarisi labaSadusi besiza ekubhabhathizeni kwakhe, wathi kubo: Nzalo yezinyoka, ngubani olibonise ukubalekela ulaka oluzayo?
8 Onetsani chipatso cha kutembenuka mtima.
Ngakho thelani izithelo ezifanele ukuphenduka;
9 Ndipo musaganize ndi kunena mwa inu nokha kuti, ‘Tili nawo abambo athu Abrahamu.’ Ndinena kwa inu kuti Mulungu akhoza kusandutsa miyala iyi kukhala ana a Abrahamu.
njalo lingacabangi ukutsho phakathi kwenulithi: SiloAbrahama ongubaba; ngoba ngithi kini: UNkulunkulu ulamandla okumvusela uAbrahama abantwana kula amatshe.
10 Tikukamba pano nkhwangwa yayikidwa kale pa mizu ya mitengo, ndipo mtengo umene subala chipatso chabwino udulidwa ndi kuponyedwa pa moto.
Lakhathesi ihloka selibekiwe empandeni yezihlahla; ngakho sonke isihlahla esingatheli isithelo esihle siyaganyulwa siphoselwe emlilweni.
11 “Ine ndikubatizani ndi madzi kusonyeza kutembenuka mtima. Koma pambuyo panga akubwera wina amene ali ndi mphamvu kuposa ine, amene sindiyenera kunyamula nsapato zake. Iyeyu adzakubatizani ndi Mzimu Woyera ndi moto.
Mina ngilibhabhathiza ngamanzi kube sekuphendukeni; kodwa yena oza emva kwami ulamandla kulami, engingafanele ukuphatha amanyathela akhe; yena uzalibhabhathiza ngoMoya oNgcwele langomlilo;
12 Mʼdzanja lake muli chopetera ndipo adzayeretsa popunthirapo pake nadzathira tirigu wake mʼnkhokwe ndi kutentha zotsalira zonse ndi moto wosazima.”
okhomane lwakhe lokwela lusesandleni sakhe, njalo uzathanyelisisa isibuya sakhe, abesebuthela amabele akhe esiphaleni sakhe, kodwa amakhoba uzawatshisa ngomlilo ongacitshekiyo.
13 Pamenepo Yesu anabwera kuchokera ku Galileya kudzabatizidwa ndi Yohane mu mtsinje wa Yorodani.
Khona uJesu evela eGalili wafika eJordani kuJohane, ukuze abhabhathizwe nguye.
14 Koma Yohane anayesetsa kumukanira nati, “Ndiyenera kubatizidwa ndi Inu, bwanji Inu mubwera kwa ine?”
Kodwa uJohane wayemalela esithi: Mina ngiswela ukubhabhathizwa nguwe, kanti wena uza kimi?
15 Yesu anayankha kuti, “Zibatero tsopano, ndi koyenera kwa ife kuchita zimenezi kukwaniritsa chilungamo chonse.” Ndipo Yohane anavomera.
Kodwa uJesu ephendula wathi kuye: Vuma khathesi; ngoba kusifanele ukuthi sigcwalise ngokunjalo ukulunga konke. Wasemvumela.
16 Yesu atangobatizidwa, nthawi yomweyo potuluka mʼmadzi, kumwamba kunatsekuka ndipo taonani, Mzimu wa Mulungu anatsika ngati nkhunda natera pa Iye.
UJesu esebhabhathiziwe wahle wakhuphuka emanzini; njalo khangela, amazulu amvulekela, wasebona uMoya kaNkulunkulu esehla kungathi lijuba esiza phezu kwakhe.
17 Ndipo mawu anamveka kuchokera kumwamba kuti, “Uyu ndiye mwana wanga wokondedwa amene ndikondwera naye.”
Njalo khangela, ilizwi livela emazulwini, lisithi: Lo uyiNdodana yami ethandekayo, engithokoza ngayo.