< Mateyu 28 >

1 Litapita tsiku la Sabata, mmawa wa tsiku loyamba la Sabata, Mariya wa ku Magadala ndi Mariya wina anapita kukaona manda.
Now after the Sabbath, as it began to dawn on the first day of the week, Maryam Magdelaitha and the other Maryam came to see the tomb.
2 Kunachitika chivomerezi chachikulu, pakuti mngelo wa Ambuye anabwera kuchokera kumwamba ndipo anapita ku manda, nakagubuduza mwala nawukhalira.
And look, there was a great earthquake, for an angel of the Lord descended from the sky, and came and rolled away the stone, and sat on it.
3 Maonekedwe ake anali ngati mphenzi ndipo zovala zake zinali mbuu ngati matalala.
His appearance was like lightning, and his clothing white as snow.
4 Alondawo anachita naye mantha kwambiri kotero kuti ananjenjemera ndi kuwuma ngati akufa.
For fear of him, the guards shook, and became like dead men.
5 Mngelo anati kwa amayiwo, “Musachite mantha popeza ndikudziwa kuti mukufuna Yesu amene anapachikidwa.
The angel answered the women, "Do not be afraid, for I know that you seek Yeshua, who has been crucified.
6 Iye muno mulibe, wauka monga mmene ananenera. Bwerani, dzaoneni malo amene anagona.
He is not here, for he has risen, just like he said. Come, see the place where he was lying.
7 Ndipo pitani msanga kawuzeni ophunzira ake kuti, ‘Wauka kwa akufa ndipo watsogola kupita ku Galileya. Mukamuona Iye kumeneko.’ Taonani ndakuwuzani.”
Go quickly and tell his disciples, 'He has risen from the dead, and look, he goes before you into Galila; there you will see him.' See, I have told you."
8 Pamenepo amayiwo anachoka mofulumira ku mandako ali ndi mantha komabe atadzaza ndi chimwemwe, ndipo anathamanga kukawuza ophunzira ake.
They departed quickly from the tomb, frightened yet with great joy, and ran to bring his disciples word.
9 Mwadzidzidzi Yesu anakumana nawo nati, “Moni.” Iwo anabwera kwa Iye, nagwira mapazi ake namulambira.
And look, Yeshua met them, saying, "Rejoice!" And they came and took hold of his feet, and worshiped him.
10 Ndipo Yesu anawawuza kuti, “Musachite mantha, pitani kawuzeni abale anga kuti apite ku Galileya ndipo kumeneko akandiona Ine.”
Then Yeshua said to them, "Do not be afraid. Go tell my brothers that they should go into Galila, and there they will see me."
11 Amayi aja akupita, ena mwa alonda aja anapita ku mzinda nafotokozera akulu a ansembe zonse zimene zinachitika.
Now while they were going, look, some of the guards came into the city, and told the chief priests all the things that had happened.
12 Akulu a ansembe atakumana ndi akuluakulu anapangana zochita. Anapatsa alonda aja ndalama zambiri,
When they were assembled with the elders, and had taken counsel, they gave a large amount of silver to the soldiers,
13 nawawuza kuti, “Muzinena kuti, ‘Ophunzira ake anabwera usiku ndipo amuba ife tili mtulo.’
saying, "Say that his disciples came by night, and stole him away while we slept.
14 Ngati nkhani iyi imupeze bwanamkubwa, ife tidzamukhazika mtima pansi ndipo simudzakhala mʼmavuto.”
If this comes to the governor's ears, we will persuade him and make you free of worry."
15 Pamenepo alondawo anatenga ndalamazo nachita monga mmene anawuzidwira. Ndipo mbiri iyi inawanda pakati pa Ayuda mpaka lero lino.
So they took the money and did as they were told. This saying was spread abroad among the Jewish people, and continues until this day.
16 Ndipo ophunzira khumi ndi mmodzi aja anapita ku Galileya, ku phiri limene Yesu anawawuza kuti apite.
But the eleven disciples went into Galila, to the mountain where Yeshua had sent them.
17 Atamuona Iye, anamulambira; koma ena anakayika.
When they saw him, they bowed down to him, but some doubted.
18 Kenaka Yesu anabwera kwa iwo nati, “Ulamuliro wonse kumwamba ndi dziko lapansi wapatsidwa kwa Ine.
Yeshua came to them and spoke to them, saying, "All authority has been given to me in heaven and on earth.
19 Chifukwa chake, pitani kaphunzitseni anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza mʼdzina la Atate ndi la Mwana ndi la Mzimu Woyera,
Therefore go, and make disciples of all nations, baptizing them in the name of the Father and of the Son and of the Rukha d'Qudsha,
20 ndi kuwaphunzitsa amvere zonse zimene ndinakulamulirani. Ndipo onani, Ine ndidzakhala pamodzi ndi inu kufikira kutha kwa dziko lapansi pano.” (aiōn g165)
teaching them to obey all things that I commanded you. And look, I am with you every day, even to the end of the age." (aiōn g165)

< Mateyu 28 >