< Mateyu 24 >

1 Yesu anatuluka mʼNyumba ya Mulungu ndipo akuchoka ophunzira ake anadza kwa Iye ndi kumuonetsa mamangidwe a Nyumbayo.
І вийшов Ісус і від храму пішов. І підійшли Його учні, щоб Йому показати будинки храмо́ві.
2 Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuona zinthu zonsezi? Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti palibe mwala pano umene udzasiyidwe pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
Він же промовив у відповідь їм: „Чи бачите ви все оце? Поправді кажу́ вам: Не зали́шиться тут навіть камінь на камені, який не зруйнується!“
3 Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?” (aiōn g165)
Коли ж Він сидів на Оли́вній горі, підійшли Його учні до Нього само́тньо й спитали: „Скажи нам, — коли станеться це? І яка буде ознака прихо́ду Твого й кінця віку?“ (aiōn g165)
4 Yesu anayankha kuti, “Onetsetsani kuti wina asakunyengeni.
Ісус же промовив у відповідь їм: „Стережіться, щоб вас хто не звів!
5 Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati, ‘Ndine Khristu,’ ndipo adzanyenga ambiri.
Бо багато хто при́йде в Ім'я́ Моє, кажучи: „Я Христос“. І зведуть багатьох.
6 Mudzamva za nkhondo ndi mbiri za nkhondo, koma onetsetsani kuti musadzidzimuke nazo. Zotere ziyenera kuchitika, koma chimaliziro sichinafike.
Ви ж про війни почуєте, і про воєнні чутки́, — глядіть, не лякайтесь, бо „статись належить тому“. Але це не кінець ще.
7 Mtundu ndi mtundu udzawukirana, ndipo ufumu ndi ufumu udzawukirana. Kudzakhala njala ndi zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana.
Бо „повстане наро́д на народ, і царство на царство“, і голод, мор та землетруси настануть місця́ми.
8 Zonsezi ndi chiyambi chabe cha zowawa.
А все це — поча́ток терпінь породільних.
9 “Pamenepo adzakuperekani kuti mukazunzidwe ndi kuphedwa, ndipo mitundu yonse idzakudani chifukwa cha Ine.
На муки тоді видаватимуть вас, і вбиватимуть вас, і вас будуть нена́видіти всі народи за Ймення Моє.
10 Pa nthawi imeneyo ambiri adzasiya chikhulupiriro ndipo adzadana ndi kuperekana wina ndi mnzake,
І багато-хто в той час спокусяться, і видавати один о́дного будуть, і один о́дного будуть нена́видіти.
11 ndipo aneneri onama ambiri adzaoneka ndi kunyenga anthu ambiri.
Постане багато фальшивих пророків, — і зведу́ть багатьо́х.
12 Chifukwa cha kuchuluka kwa zoyipa, chikondi cha ambiri chidzazirala,
І через розрі́ст беззаконства любов багатьох охоло́не.
13 koma wopirira kufikira chimaliziro adzapulumuka.
А хто витерпить аж до кінця, — той буде спасе́ний!
14 Ndipo uthenga wa ufumu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi ngati umboni kwa mitundu yonse, ndipo pomwepo chimaliziro chidzafika.”
І проповідана буде ця Євангелія Царства по ці́лому світові, на свідо́цтво наро́дам усім. І тоді при́йде кінець!
15 “Tsono mukadzaona chinthu chonyansa chosakaza chitayima pamalo oyera chimene anayankhula mneneri Danieli, owerengayo azindikire.
Тож, коли ви побачите ту „гидоту спусто́шення“, що про неї звіщав був пророк Даниїл, на місці святому, — хто читає, нехай розуміє, —
16 Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire ku mapiri.
тоді ті, хто в Юдеї, нехай в го́ри втікають.
17 Yemwe ali pa denga la nyumba yake asatsike kukatulutsa chinthu chilichonse mʼnyumba.
Хто на покрівлі, нехай той не сходить узяти речі з дому свого́.
18 Yemwe ali ku munda asapite kukatenga mkanjo wake.
І хто на полі, — хай назад не вертається взяти одежу свою.
19 Kudzakhala koopsa kwambiri masiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi kwa oyamwitsa!
Горе ж вагі́тним і тим, хто годує грудьми́, за днів тих!
20 Pempherani kuti kuthawa kwanu kusadzachitike nthawi yozizira kapena pa Sabata.
Моліться ж, щоб ваша втеча не сталась зимою, ані в суботу.
21 Popeza kudzakhala masautso aakulu, omwe safanana ndi ena ali onse chiyambireni cha dziko lapansi mpaka lero lino ndipo sadzafanananso ndi ena.
Бо скорбо́та велика настане тоді, „якої не було́ з первопо́чину світу аж досі“й не бу́де.
22 Ngati masiku amenewo sakanafupikitsidwa, palibe mmodzi akanapulumuka, koma chifukwa cha osankhidwawo masiku amenewo adzafupikitsidwa.
І коли б не вкороти́лись ті дні, не спаслася б ніяка люди́на; але через ви́браних дні ті вкоро́тяться.
23 Pa nthawi imeneyo ngati wina adzati kwa inu, ‘Onani, Khristu ali pano!’ Kapena, ‘Uyo ali ukoyo!’ Musakhulupirire.
Тоді, як хто скаже до вас: „Ото, Христос тут" чи „Отам“, — не йміть віри.
24 Chifukwa akhristu onama ndi aneneri onama adzaoneka ndipo adzachita zizindikiro zazikulu ndi zodabwitsa kuti akanyenge ngakhale osankhidwawo ngati kukanakhala kotheka kutero.
Бо постануть христи́ неправдиві, і неправдиві пророки, і будуть чинити великі ознаки та чуда, що звели́ б, коли б можна, і ви́браних.
25 Onani, ndakuwuzani izi nthawi isanafike.
Оце Я наперед вам сказав.
26 “Ndiye ngati wina akuwuzani inu kuti, ‘Uyo ali ku chipululu,’ inu musapiteko; kapena akati, ‘Uyu ali kuno mʼchipinda chamʼkati,’ musakhulupirire.
А коли скажуть вам: „Ось Він у пустині“— не виходьте, „Ось Він у криївках“— не вірте!
27 Monga momwe mphenzi ingʼanima kuchokera kummawa kupita kumadzulo, momwemonso kudzakhala kubwera kwa Mwana wa Munthu.
Бо як бли́скавка та вибігає зо схо́ду, і з'являється аж до за́ходу, так буде і при́хід Сина Лю́дського.
28 Kulikonse kuli chinthu cha kufa, makwangwala adzasonkhanako.
Бо де труп, — там зберуться орли́.
29 “Akadzangotha mavuto a masiku amenewo, “‘dzuwa lidzadetsedwa, ndipo mwezi sudzawala; nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba, ndipo mphamvu za mmwamba zidzagwedezeka.’
І зараз, по скорботі тих днів, „сонце затьми́ться, і місяць не дасть свого світла“, і зорі попа́дають з неба, і сили небесні пору́шаться.
30 “Pa nthawi imeneyo chizindikiro cha Mwana wa Munthu chidzaoneka mlengalenga, ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalira. Idzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
І того ча́су на небі з'я́виться знак Сина Лю́дського, і тоді „заголосять всі зе́мні племе́на“, і побачать вони „Сина Лю́дського, що йтиме на хмарах небесних" із великою поту́гою й славою.
31 Ndipo adzatuma angelo ake, ndi kulira kwa lipenga kwakukulu, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mphepo zinayi, ndi kuchokera kumathero a thambo kufika mbali ina.
І пошле анголі́в Своїх Він із голосним сурмови́м гуком, і зберуть Його ви́браних — „від вітрі́в чотирьох, від кінців неба аж до кі́нців його“.
32 “Tsopano kuchokera ku mtengo wamkuyu phunzirani ichi: Pamene uyamba kuphukira, masamba ake akatuluka, mumadziwa kuti dzinja layandikira.
Від дерева ж фіґового навчіться при́кладу: коли віття його вже розпу́кується, і ки́неться листя, то ви знаєте, що близько вже літо.
33 Momwemonso, pamene mudzaona zinthu zonsezi mudzadziwe kuti ali pafupi pa khomo penipeni.
Так і ви: коли все це побачите, знайте, що бли́зько, — під дверима!
34 Zoonadi, ndikuwuzani kuti mʼbado uwu sudzatha mpaka zinthu zonse zitachitika.
Поправді кажу́ вам: не пере́йде цей рід, аж усе оце станеться.
35 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Небо й земля промине́ться, але не минуться слова́ Мої!
36 “Palibe amene adziwa za tsikulo kapena nthawi, angakhale angelo akumwamba, angakhale Mwana, koma Atate okha.
А про день той й годину не знає ніхто: ані анголи́ небесні, ані Син, — лише́ Сам Отець.
37 Monga momwe zinalili nthawi ya Nowa, momwemonso zidzatero pobwera kwa Mwana wa Munthu.
Як було за днів Но́євих, так буде і при́хід Сина Лю́дського.
38 Pakuti masiku amenewo chisanafike chigumula, anthu amadya ndi kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo;
Бо так само, як за днів до пото́пу всі їли й пили, женилися й заміж вихо́дили, аж до дня, „коли Ной увійшов до ковче́гу“,
39 ndipo sanadziwe za chimene chikanachitika mpaka pamene chigumula chinafika ndi kuwamiza onse. Umu ndi mmene zidzakhalira pobwera kwa Mwana wa Munthu.
і не знали, аж поки пото́п прийшов та й усіх забрав, — так буде і при́хід Сина Лю́дського.
40 Amuna awiri adzakhala mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
Будуть двоє на полі тоді, — один ві́зьметься, а другий поли́шиться.
41 Amayi awiri adzakhala akusinja pa mtondo; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
Дві будуть молоти на жо́рнах, — одна ві́зьметься, а друга полишиться.
42 “Chifukwa chake yangʼanirani, popeza simudziwa tsiku lanji limene Ambuye anu adzabwera.
Тож пильнуйте, бо не знаєте, котрого дня при́йде Господь ваш.
43 Koma zindikirani ichi: Ngati mwini nyumba akanadziwa nthawi yanji ya usiku imene mbala imabwera, sakanagona ndipo sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
Знайте ж це, що коли б знав госпо́дар, о котрі́й сторожі при́йде зло́дій, то він пильнував би, і підкопа́ти свого дому не дав би.
44 Inunso tsono muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa nthawi imene inu simukumuyembekezera.
Тому бу́дьте готові й ви, — бо при́йде Син Лю́дський тієї години, коли ви не ду́маєте!
45 “Kodi wantchito wokhulupirika ndi wanzeru amene ambuye ake anamuyika kukhala woyangʼanira antchito a mʼnyumba kuti awapatse chakudya chawo pa nthawi yake ndani?
Хто ж вірний і мудрий раб, якого пан поставив над своїми челя́дниками давати своєчасно поживу для них?
46 Chidzakhala chabwino kwa wantchitoyo ngati mbuye wake pofika adzamupeza akuchita zimenezi.
Блаженний той раб, що пан його при́йде та зна́йде, що робить він так!
47 Zoonadi, ndikuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
Поправді кажу́ вам, що над ці́лим маєтком своїм він поставить його.
48 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo ndi woyipa, nati kwa iye yekha, ‘Mbuye wanga akuchedwa kubwera,’
А як той злий раб скаже у серці своїм: „Заба́риться пан мій прийти“,
49 nayamba kumenya antchito anzake, nadya ndi kumwa ndi zidakwa.
і зачне бити товаришів своїх, а їсти та пити з п'яни́цями,
50 Mbuye wa wantchitoyo adzabwera pa tsiku limene iye samamuyembekezera ndi pa nthawi imene iye sakuyidziwa.
то пан того раба при́йде дня, якого він не сподівається, і о годині, якої не знає.
51 Adzamulanga koopsa ndipo adzamuyika kokhala anthu achiphamaso, kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
І він пополови́ні розі́тне його́, і визначить долю йому з лицемірами, — буде плач там і скре́гіт зубів!

< Mateyu 24 >