< Mateyu 24 >
1 Yesu anatuluka mʼNyumba ya Mulungu ndipo akuchoka ophunzira ake anadza kwa Iye ndi kumuonetsa mamangidwe a Nyumbayo.
A wyszedłszy Jezus z kościoła szedł; i przystąpili uczniowie jego, aby mu ukazali budowanie kościelne.
2 Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuona zinthu zonsezi? Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti palibe mwala pano umene udzasiyidwe pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
I rzekł im Jezus: Izaż nie widzicie tego wszystkiego? Zaprawdę powiadam wam, nie zostanie tu kamień na kamieniu, który by nie był rozwalony.
3 Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?” (aiōn )
A gdy siedział na górze oliwnej, przystąpili do niego uczniowie osobno, mówiąc: Powiedz nam, kiedy się to stanie, i co za znak przyjścia twego i dokonania świata? (aiōn )
4 Yesu anayankha kuti, “Onetsetsani kuti wina asakunyengeni.
I odpowiadając Jezus, rzekł im: Patrzcie, aby was kto nie zwiódł.
5 Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati, ‘Ndine Khristu,’ ndipo adzanyenga ambiri.
Albowiem wiele ich przyjdzie pod imieniem mojem, mówiąc: Jam jest Chrystus; i wiele ich zwiodą.
6 Mudzamva za nkhondo ndi mbiri za nkhondo, koma onetsetsani kuti musadzidzimuke nazo. Zotere ziyenera kuchitika, koma chimaliziro sichinafike.
I usłyszycie wojny i wieści o wojnach; patrzcież, abyście sobą nie trwożyli; albowiem musi to wszystko być, ale jeszcze nie tu jest koniec.
7 Mtundu ndi mtundu udzawukirana, ndipo ufumu ndi ufumu udzawukirana. Kudzakhala njala ndi zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana.
Albowiem powstanie naród przeciwko narodowi, i królestwo przeciwko królestwu, i będą głody i mory i trzęsienia ziemi miejscami.
8 Zonsezi ndi chiyambi chabe cha zowawa.
Ale to wszystko jest początkiem boleści.
9 “Pamenepo adzakuperekani kuti mukazunzidwe ndi kuphedwa, ndipo mitundu yonse idzakudani chifukwa cha Ine.
Tedy was podadzą w udręczenie, i będą was zabijać, i będziecie w nienawiści u wszystkich narodów dla imienia mego.
10 Pa nthawi imeneyo ambiri adzasiya chikhulupiriro ndipo adzadana ndi kuperekana wina ndi mnzake,
A tedy wiele się ich zgorszy, a jedni drugich wydadzą, i jedni drugich nienawidzieć będą.
11 ndipo aneneri onama ambiri adzaoneka ndi kunyenga anthu ambiri.
I wiele fałszywych proroków powstanie, i zwiodą wielu.
12 Chifukwa cha kuchuluka kwa zoyipa, chikondi cha ambiri chidzazirala,
A iż się rozmnoży nieprawość, oziębnie miłość wielu.
13 koma wopirira kufikira chimaliziro adzapulumuka.
Ale kto wytrwa aż do końca, ten zbawion będzie.
14 Ndipo uthenga wa ufumu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi ngati umboni kwa mitundu yonse, ndipo pomwepo chimaliziro chidzafika.”
I będzie kazana ta Ewangielija królestwa po wszystkim świecie, na świadectwo wszystkim narodom. A tedyć przyjdzie koniec.
15 “Tsono mukadzaona chinthu chonyansa chosakaza chitayima pamalo oyera chimene anayankhula mneneri Danieli, owerengayo azindikire.
Przetoż gdy ujrzycie obrzydliwość spustoszenia, opowiedzianą przez Danijela proroka, stojącą na miejscu świętem, (kto czyta, niechaj uważa),
16 Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire ku mapiri.
Tedy ci, co będą w ziemi Judzkiej, niech uciekają na góry;
17 Yemwe ali pa denga la nyumba yake asatsike kukatulutsa chinthu chilichonse mʼnyumba.
A kto na dachu, niechaj nie zstępuje, aby co wziął z domu swego;
18 Yemwe ali ku munda asapite kukatenga mkanjo wake.
A kto na roli, niech się nazad nie wraca, aby wziął szaty swe.
19 Kudzakhala koopsa kwambiri masiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi kwa oyamwitsa!
A biada brzemiennym i piersiami karmiącym w one dni!
20 Pempherani kuti kuthawa kwanu kusadzachitike nthawi yozizira kapena pa Sabata.
Przetoż módlcie się, aby nie było uciekanie wasze w zimie, albo w sabat.
21 Popeza kudzakhala masautso aakulu, omwe safanana ndi ena ali onse chiyambireni cha dziko lapansi mpaka lero lino ndipo sadzafanananso ndi ena.
Albowiem naonczas będzie wielki ucisk, jaki nie był od początku świata aż dotąd, ani potem będzie.
22 Ngati masiku amenewo sakanafupikitsidwa, palibe mmodzi akanapulumuka, koma chifukwa cha osankhidwawo masiku amenewo adzafupikitsidwa.
A gdyby nie były skrócone one dni, nie byłoby zbawione żadne ciało: ale dla wybranych będą skrócone one dni.
23 Pa nthawi imeneyo ngati wina adzati kwa inu, ‘Onani, Khristu ali pano!’ Kapena, ‘Uyo ali ukoyo!’ Musakhulupirire.
Tedy jeźliby wam kto rzekł: Oto tu jest Chrystus, albo tam, nie wierzcie.
24 Chifukwa akhristu onama ndi aneneri onama adzaoneka ndipo adzachita zizindikiro zazikulu ndi zodabwitsa kuti akanyenge ngakhale osankhidwawo ngati kukanakhala kotheka kutero.
Albowiem powstaną fałszywi Chrystusowie, i fałszywi prorocy, i czynić będą znamiona wielkie i cuda, tak iżby zwiedli (by można) i wybrane.
25 Onani, ndakuwuzani izi nthawi isanafike.
Otom wam przepowiedział.
26 “Ndiye ngati wina akuwuzani inu kuti, ‘Uyo ali ku chipululu,’ inu musapiteko; kapena akati, ‘Uyu ali kuno mʼchipinda chamʼkati,’ musakhulupirire.
Jeźliby wam tedy rzekli: Oto na puszczy jest, nie wychodźcie; oto w komorach, nie wierzcie.
27 Monga momwe mphenzi ingʼanima kuchokera kummawa kupita kumadzulo, momwemonso kudzakhala kubwera kwa Mwana wa Munthu.
Albowiem jako błyskawica wychodzi od wschodu słońca i ukazuje się aż na zachód, tak będzie i przyjście Syna człowieczego.
28 Kulikonse kuli chinthu cha kufa, makwangwala adzasonkhanako.
Bo gdziekolwiek będzie ścierw, tam się zgromadzą i orły.
29 “Akadzangotha mavuto a masiku amenewo, “‘dzuwa lidzadetsedwa, ndipo mwezi sudzawala; nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba, ndipo mphamvu za mmwamba zidzagwedezeka.’
A zaraz po utrapieniu onych dni słońce się zaćmi, a księżyc nie da jasności swojej, i gwiazdy będą padać z nieba, i mocy niebieskie poruszą się.
30 “Pa nthawi imeneyo chizindikiro cha Mwana wa Munthu chidzaoneka mlengalenga, ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalira. Idzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
Tedyć się ukaże znamię Syna człowieczego na niebie, a tedy będą narzekać wszystkie pokolenia ziemi, i ujrzą Syna człowieczego, przychodzącego na obłokach niebieskich, z mocą i z chwałą wielką;
31 Ndipo adzatuma angelo ake, ndi kulira kwa lipenga kwakukulu, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mphepo zinayi, ndi kuchokera kumathero a thambo kufika mbali ina.
I pośle Anioły swoje z trąbą głosu wielkiego, i zgromadzą wybrane jego od czterech wiatrów, od krajów niebios aż do krajów ich.
32 “Tsopano kuchokera ku mtengo wamkuyu phunzirani ichi: Pamene uyamba kuphukira, masamba ake akatuluka, mumadziwa kuti dzinja layandikira.
A od drzewa figowego nauczcie się tego podobieństwa: Gdy się już gałąź jego odmładza i liście wypuszcza, poznajecie, iż blisko jest lato.
33 Momwemonso, pamene mudzaona zinthu zonsezi mudzadziwe kuti ali pafupi pa khomo penipeni.
Także i wy, gdy ujrzycie to wszystko, poznawajcie, iż blisko jest, a we drzwiach.
34 Zoonadi, ndikuwuzani kuti mʼbado uwu sudzatha mpaka zinthu zonse zitachitika.
Zaprawdę powiadam wam, że nie przeminie ten wiek, ażby się to wszystko stało.
35 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Niebo i ziemia przeminą, ale słowa moje nie przeminą.
36 “Palibe amene adziwa za tsikulo kapena nthawi, angakhale angelo akumwamba, angakhale Mwana, koma Atate okha.
A o onym dniu i godzinie nikt nie wie, ani Aniołowie niebiescy, tylko sam Ojciec mój.
37 Monga momwe zinalili nthawi ya Nowa, momwemonso zidzatero pobwera kwa Mwana wa Munthu.
Ale jako było za dni Noego, tak będzie i przyjście Syna człowieczego.
38 Pakuti masiku amenewo chisanafike chigumula, anthu amadya ndi kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo;
Albowiem jako za dni onych przed potopem jedli, i pili, i ożeniali się i za mąż wydawali, aż do onego dnia, którego wszedł Noe do korabia,
39 ndipo sanadziwe za chimene chikanachitika mpaka pamene chigumula chinafika ndi kuwamiza onse. Umu ndi mmene zidzakhalira pobwera kwa Mwana wa Munthu.
I nie spostrzegli się, aż przyszedł potop i zabrał wszystkie: tak będzie i przyjście Syna człowieczego.
40 Amuna awiri adzakhala mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
Tedy będą dwaj na roli; jeden będzie wzięty, a drugi zostawiony;
41 Amayi awiri adzakhala akusinja pa mtondo; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
Dwie będą mleć we młynie; jedna będzie wzięta, a druga zostawiona;
42 “Chifukwa chake yangʼanirani, popeza simudziwa tsiku lanji limene Ambuye anu adzabwera.
Czujcież tedy, ponieważ nie wiecie, której godziny Pan wasz przyjdzie.
43 Koma zindikirani ichi: Ngati mwini nyumba akanadziwa nthawi yanji ya usiku imene mbala imabwera, sakanagona ndipo sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
A to wiedzcie, że, gdyby wiedział gospodarz, o której straży złodziej ma przyjść, wżdyby czuł, i nie dałby podkopać domu swego.
44 Inunso tsono muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa nthawi imene inu simukumuyembekezera.
Przetoż i wy bądźcie gotowi; bo której się godziny nie spodziejecie, Syn człowieczy przyjdzie.
45 “Kodi wantchito wokhulupirika ndi wanzeru amene ambuye ake anamuyika kukhala woyangʼanira antchito a mʼnyumba kuti awapatse chakudya chawo pa nthawi yake ndani?
Któryż tedy jest sługa wierny i roztropny, którego postanowił pan jego nad czeladzią swoją, aby im dawał pokarm na czas słuszny?
46 Chidzakhala chabwino kwa wantchitoyo ngati mbuye wake pofika adzamupeza akuchita zimenezi.
Błogosławiony on sługa, którego by, przyszedłszy Pan jego, znalazł tak czyniącego;
47 Zoonadi, ndikuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
Zaprawdę powiadam wam, że go nad wszystkiemi dobrami swemi postanowi.
48 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo ndi woyipa, nati kwa iye yekha, ‘Mbuye wanga akuchedwa kubwera,’
A jeźliby rzekł on zły sługa w sercu swojem: Odwłacza pan mój z przyjściem swojem;
49 nayamba kumenya antchito anzake, nadya ndi kumwa ndi zidakwa.
I począłby bić spółsługi, a jeść i pić z pijanicami:
50 Mbuye wa wantchitoyo adzabwera pa tsiku limene iye samamuyembekezera ndi pa nthawi imene iye sakuyidziwa.
Przyjdzie pan sługi onego, dnia, którego się nie spodzieje, i godziny, której nie wie;
51 Adzamulanga koopsa ndipo adzamuyika kokhala anthu achiphamaso, kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
I odłączy go, a część jego położy z obłudnikami; tam będzie płacz i zgrzytanie zębów.