< Mateyu 24 >
1 Yesu anatuluka mʼNyumba ya Mulungu ndipo akuchoka ophunzira ake anadza kwa Iye ndi kumuonetsa mamangidwe a Nyumbayo.
Og Jesus gik ud, bort fra Helligdommen, og hans Disciple kom til ham for at vise ham Helligdommens Bygninger.
2 Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuona zinthu zonsezi? Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti palibe mwala pano umene udzasiyidwe pa unzake; uliwonse udzagwetsedwa pansi.”
Men han svarede og sagde til dem: “Se I ikke alt dette? Sandelig, siger jeg eder, her skal ikke lades Sten paa Sten, som jo skal nedbrydes.”
3 Pamene Yesu anakhala pansi pa phiri la Olivi, ophunzira ake anabwera kwa Iye mwamseri nati, “Tiwuzeni, kodi izi zidzachitika liti, ndipo chizindikiro cha kubwera kwanu ndi zizindikiro za kutha kwa dziko zidzakhala chiyani?” (aiōn )
Men da han sad paa Oliebjerget, kom hans Disciple til ham afsides og sagde: “Sig os, naar skal dette ske? Og hvad er Tegnet paa din Tilkommelse og Verdens Ende?” (aiōn )
4 Yesu anayankha kuti, “Onetsetsani kuti wina asakunyengeni.
Og Jesus svarede og sagde til dem: “Ser til, at ingen forfører eder!
5 Pakuti ambiri adzabwera mʼdzina langa nadzati, ‘Ndine Khristu,’ ndipo adzanyenga ambiri.
Thi mange skulle paa mit Navn komme og sige: Jeg er Kristus; og de skulle forføre mange.
6 Mudzamva za nkhondo ndi mbiri za nkhondo, koma onetsetsani kuti musadzidzimuke nazo. Zotere ziyenera kuchitika, koma chimaliziro sichinafike.
Men I skulle faa at høre om Krige og Krigsrygter. Ser til, lader eder ikke forskrække; thi det maa ske; men Enden er ikke endda.
7 Mtundu ndi mtundu udzawukirana, ndipo ufumu ndi ufumu udzawukirana. Kudzakhala njala ndi zivomerezi mʼmalo osiyanasiyana.
Thi Folk skal rejse sig mod Folk, og Rige mod Rige, og der skal være Hungersnød og Jordskælv her og der.
8 Zonsezi ndi chiyambi chabe cha zowawa.
Men alt dette er Veernes Begyndelse.
9 “Pamenepo adzakuperekani kuti mukazunzidwe ndi kuphedwa, ndipo mitundu yonse idzakudani chifukwa cha Ine.
Da skulle de overgive eder til Trængsel og slaa eder ihjel, og I skulle hades af alle Folkeslagene for mit Navns Skyld.
10 Pa nthawi imeneyo ambiri adzasiya chikhulupiriro ndipo adzadana ndi kuperekana wina ndi mnzake,
Og da skulle mange forarges og forraade hverandre og hade hverandre.
11 ndipo aneneri onama ambiri adzaoneka ndi kunyenga anthu ambiri.
Og mange falske Profeter skulle fremstaa og forføre mange.
12 Chifukwa cha kuchuluka kwa zoyipa, chikondi cha ambiri chidzazirala,
Og fordi Lovløsheden bliver mangfoldig, vil Kærligheden blive kold hos de fleste.
13 koma wopirira kufikira chimaliziro adzapulumuka.
Men den, som holder ud indtil Enden, han skal frelses.
14 Ndipo uthenga wa ufumu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi ngati umboni kwa mitundu yonse, ndipo pomwepo chimaliziro chidzafika.”
Og dette Rigets Evangelium skal prædikes i hele Verden til et Vidnesbyrd for alle Folkeslagene; og da skal Enden komme.
15 “Tsono mukadzaona chinthu chonyansa chosakaza chitayima pamalo oyera chimene anayankhula mneneri Danieli, owerengayo azindikire.
Naar I da se Ødelæggelsens Vederstyggelighed, hvorom der er talt ved Profeten Daniel, staa paa hellig Grund, (den, som læser det, han give Agt!)
16 Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire ku mapiri.
da skulle de, som ere i Judæa, fly ud paa Bjergene;
17 Yemwe ali pa denga la nyumba yake asatsike kukatulutsa chinthu chilichonse mʼnyumba.
den, som er paa Taget, stige ikke ned for at hente, hvad der er i hans Hus;
18 Yemwe ali ku munda asapite kukatenga mkanjo wake.
og den, som er paa Marken, vende ikke tilbage for at hente sine Klæder!
19 Kudzakhala koopsa kwambiri masiku amenewo kwa amayi oyembekezera ndi kwa oyamwitsa!
Men ve de frugtsommelige og dem, som give Die, i de Dage!
20 Pempherani kuti kuthawa kwanu kusadzachitike nthawi yozizira kapena pa Sabata.
Og beder om, at eders Flugt ikke skal ske om Vinteren, ej heller paa en Sabbat;
21 Popeza kudzakhala masautso aakulu, omwe safanana ndi ena ali onse chiyambireni cha dziko lapansi mpaka lero lino ndipo sadzafanananso ndi ena.
thi der skal da være en Trængsel saa stor, som der ikke har været fra Verdens Begyndelse indtil nu og heller ikke skal komme.
22 Ngati masiku amenewo sakanafupikitsidwa, palibe mmodzi akanapulumuka, koma chifukwa cha osankhidwawo masiku amenewo adzafupikitsidwa.
Og dersom disse Dage ikke bleve afkortede, da blev intet Kød frelst; men for de udvalgtes Skyld skulle disse Dage afkortes.
23 Pa nthawi imeneyo ngati wina adzati kwa inu, ‘Onani, Khristu ali pano!’ Kapena, ‘Uyo ali ukoyo!’ Musakhulupirire.
Dersom nogen da siger til eder: Se, her er Kristus, eller der! da skulle I ikke tro det.
24 Chifukwa akhristu onama ndi aneneri onama adzaoneka ndipo adzachita zizindikiro zazikulu ndi zodabwitsa kuti akanyenge ngakhale osankhidwawo ngati kukanakhala kotheka kutero.
Thi falske Krister og falske Profeter skulle fremstaa og gøre store Tegn og Undergerninger, saa at ogsaa de udvalgte skulde blive forførte, om det var muligt.
25 Onani, ndakuwuzani izi nthawi isanafike.
Se, jeg har sagt eder det forud.
26 “Ndiye ngati wina akuwuzani inu kuti, ‘Uyo ali ku chipululu,’ inu musapiteko; kapena akati, ‘Uyu ali kuno mʼchipinda chamʼkati,’ musakhulupirire.
Derfor, om de sige til eder: Se, han er i Ørkenen, da gaar ikke derud; se, han er i Kamrene, da tror det ikke!
27 Monga momwe mphenzi ingʼanima kuchokera kummawa kupita kumadzulo, momwemonso kudzakhala kubwera kwa Mwana wa Munthu.
Thi ligesom Lynet udgaar fra Østen og lyser indtil Vesten, saaledes skal Menneskesønnens Tilkommelse være.
28 Kulikonse kuli chinthu cha kufa, makwangwala adzasonkhanako.
Hvor Aadselet er, der ville Ørnene samle sig.
29 “Akadzangotha mavuto a masiku amenewo, “‘dzuwa lidzadetsedwa, ndipo mwezi sudzawala; nyenyezi zidzagwa kuchokera kumwamba, ndipo mphamvu za mmwamba zidzagwedezeka.’
Men straks efter de Dages Trængsel skal Solen formørkes og Maanen ikke give sit Skin og Stjernerne falde ned fra Himmelen, og Himmelens Kræfter skulle rystes.
30 “Pa nthawi imeneyo chizindikiro cha Mwana wa Munthu chidzaoneka mlengalenga, ndipo mitundu yonse ya pa dziko lapansi idzalira. Idzaona Mwana wa Munthu akubwera ndi mitambo, mphamvu ndi ulemerero waukulu.
Og da skal Menneskesønnens Tegn vise sig paa Himmelen; og da skulle alle Jordens Stammer jamre sig, og de skulle se Menneskesønnen komme paa Himmelens Skyer med Kraft og megen Herlighed.
31 Ndipo adzatuma angelo ake, ndi kulira kwa lipenga kwakukulu, nadzasonkhanitsa osankhidwa ake kuchokera ku mphepo zinayi, ndi kuchokera kumathero a thambo kufika mbali ina.
Og han skal udsende sine Engle med stærktlydende Basun, og de skulle samle hans udvalgte fra de fire Vinde, fra den ene Ende af Himmelen til den anden.
32 “Tsopano kuchokera ku mtengo wamkuyu phunzirani ichi: Pamene uyamba kuphukira, masamba ake akatuluka, mumadziwa kuti dzinja layandikira.
Men lærer Lignelsen af Figentræet: Naar dets Gren allerede er bleven blød, og Bladene skyde frem, da skønne I, at Sommeren er nær.
33 Momwemonso, pamene mudzaona zinthu zonsezi mudzadziwe kuti ali pafupi pa khomo penipeni.
Saaledes skulle ogsaa I, naar I se alt dette, skønne, at han er nær for Døren.
34 Zoonadi, ndikuwuzani kuti mʼbado uwu sudzatha mpaka zinthu zonse zitachitika.
Sandelig, siger jeg eder, denne Slægt skal ingenlunde forgaa, førend alle disse Ting ere skete.
35 Kumwamba ndi dziko lapansi zidzatha, koma mawu anga sadzatha.”
Himmelen og Jorden skulle forgaa, men mine Ord skulle ingenlunde forgaa.
36 “Palibe amene adziwa za tsikulo kapena nthawi, angakhale angelo akumwamba, angakhale Mwana, koma Atate okha.
Men om den Dag og Time ved ingen, end ikke Himmelens Engle, heller ikke Sønnen, men kun Faderen alene.
37 Monga momwe zinalili nthawi ya Nowa, momwemonso zidzatero pobwera kwa Mwana wa Munthu.
Og ligesom Noas Dage vare, saaledes skal Menneskesønnens Tilkommelse være.
38 Pakuti masiku amenewo chisanafike chigumula, anthu amadya ndi kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa, mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo;
Thi ligesom de i Dagene før Syndfloden aade og drak, toge til Ægte og bortgiftede, indtil den Dag, da Noa gik ind i Arken,
39 ndipo sanadziwe za chimene chikanachitika mpaka pamene chigumula chinafika ndi kuwamiza onse. Umu ndi mmene zidzakhalira pobwera kwa Mwana wa Munthu.
og ikke agtede det, førend Syndfloden kom og tog dem alle bort, saaledes skal ogsaa Menneskesønnens Tilkommelse være.
40 Amuna awiri adzakhala mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
Da skulle to Mænd være paa Marken; den ene tages med, og den anden lades tilbage.
41 Amayi awiri adzakhala akusinja pa mtondo; wina adzatengedwa ndi wina adzatsala.
To Kvinder skulle male paa Kværnen; den ene tages med, og den anden lades tilbage.
42 “Chifukwa chake yangʼanirani, popeza simudziwa tsiku lanji limene Ambuye anu adzabwera.
Vaager derfor, thi I vide ikke, paa hvilken Dag eders Herre kommer.
43 Koma zindikirani ichi: Ngati mwini nyumba akanadziwa nthawi yanji ya usiku imene mbala imabwera, sakanagona ndipo sakanalola kuti nyumba yake ithyoledwe.
Men dette skulle I vide, at dersom Husbonden vidste, i hvilken Nattevagt Tyven vilde komme, da vaagede han og tillod ikke, at der skete Indbrud i hans Hus.
44 Inunso tsono muyenera kukhala okonzeka, chifukwa Mwana wa Munthu adzabwera pa nthawi imene inu simukumuyembekezera.
Derfor vorder ogsaa I rede; thi Menneskesønnen kommer i den Time, som I ikke mene.
45 “Kodi wantchito wokhulupirika ndi wanzeru amene ambuye ake anamuyika kukhala woyangʼanira antchito a mʼnyumba kuti awapatse chakudya chawo pa nthawi yake ndani?
Hvem er saa den tro og forstandige Tjener, som hans Herre har sat over sit Tyende til at give dem deres Mad i rette Tid?
46 Chidzakhala chabwino kwa wantchitoyo ngati mbuye wake pofika adzamupeza akuchita zimenezi.
Salig er den Tjener, hvem hans Herre, naar han kommer, finder handlende saaledes.
47 Zoonadi, ndikuwuzani kuti adzamuyika kukhala woyangʼanira katundu wake yense.
Sandelig siger jeg eder, han skal sætte ham over alt, hvad han ejer.
48 Koma tiyerekeze kuti wantchitoyo ndi woyipa, nati kwa iye yekha, ‘Mbuye wanga akuchedwa kubwera,’
Men dersom den onde Tjener siger i sit Hjerte: Min Herre tøver,
49 nayamba kumenya antchito anzake, nadya ndi kumwa ndi zidakwa.
og saa begynder at slaa sine Medtjenere og spiser og drikker med Drankerne,
50 Mbuye wa wantchitoyo adzabwera pa tsiku limene iye samamuyembekezera ndi pa nthawi imene iye sakuyidziwa.
da skal den Tjeners Herre komme paa den Dag, han ikke venter, og i den Time, han ikke ved,
51 Adzamulanga koopsa ndipo adzamuyika kokhala anthu achiphamaso, kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
og hugge ham sønder og give ham hans Lod sammen med Hyklerne; der skal der være Graad og Tænders Gnidsel.